< Job 31 >

1 Jag hafver gjort ett förbund med min ögon, att jag intet skall sköta efter någon jungfru.
“Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
2 Men hvad gifver mig Gud till löna ofvan efter, och hvad arfvedel den Allsmägtige af höjdene?
Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
3 Skulle icke heldre den orättfärdige hafva den vedermödona, och en ogerningsman sådana jämmer lida?
Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
4 Ser han icke mina vägar, och räknar alla mina gånger?
Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
5 Hafver jag vandrat i fåfängelighet, eller min fot skyndat sig till bedrägeri?
“Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
6 Man väge mig på en rätt våg, så skall Gud förnimma min fromhet.
Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
7 Hafver min gång vikit utaf vägen, och mitt hjerta efterföljt min ögon, och något lådat vid mina händer,
ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
8 Så låt mig så, och en annar äte det; och min ätt varde utrotad.
Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
9 Hafver mitt hjerta låtit sig draga till qvinno, och hafver vaktat vid mins nästas dörr,
“Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
10 Så varde min hustru af enom androm skämd, och andre besofve henne;
pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
11 Ty det är en last och en missgerning för domarena.
Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
12 Ty det vore en eld, som förtärer intill förderf, och all min tilldrägt utrotade.
Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
13 Hafver jag föraktat, mins tjenares eller mine tjenarinnos rätt, då de med mig trätte?
“Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
14 Hvad ville jag göra, när Gud reser sig upp? Och hvad ville jag svara, när han hemsöker?
ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
15 Hafver ock icke han gjort honom, den mig i moderlifvet gjorde; och hafver ju så väl tillredt honom i lifvena?
Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
16 Hafver jag dem torftigom förnekat hvad de begärde, och låtit enkones ögon försmäkta?
“Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
17 Hafver jag ätit min beta allena, att den faderlöse icke också hafver ätit deraf?
ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
18 Ty ifrå minom ungdom hafver jag hållit mig såsom en fader, och allt ifrå mitt moderlif hafver jag gerna hugsvalat.
chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
19 Hafver jag någon sett förgås, derföre att han icke hade kläder; och låtit den fattiga gå oskyldan?
ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
20 Hafva icke hans sidor välsignat mig, då han af min lambs skinn värmad vardt?
ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
21 Hafver jag låtit komma mina hand vid den faderlösa, ändock jag såg mig i portenom magt hafva,
ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
22 Så falle mina skuldror ifrå mina axlar, och min arm gånge sönder ifrå läggenom.
pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
23 Ty jag fruktade Gud såsom en olycko öfver mig, och kunde hans tunga icke bära.
Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
24 Hafver jag satt guld till min tröst, och sagt till guldklimpen: Du äst mitt hopp?
“Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
25 Hafver jag gladt mig, att jag myckna ägodelar hade, och min hand allahanda förvärfvat hade?
ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
26 Hafver jag sett på ljuset, då det klarliga sken, och på månan, då han i fyllo gick?
ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
27 Hafver mitt hjerta hemliga låtit sig tälja i det sinnet, att min mun skulle kyssa mina hand?
ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
28 Hvilket ock en missgerning är för domarena; förty dermed hade jag nekat Gud i höjdene.
pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
29 Hafver jag gladt mig, när minom fiende gick illa, och upphäfvit mig, att olycka råkade uppå honom?
“Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
30 Ty jag lät min mun icke synda, så att han önskade hans själ ena banno.
ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
31 Hafva icke de män i mine hyddo måst säga: Ack! att vi icke måtte af hans kött mättade varda.
ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
32 Ute måste den främmande icke blifva; utan dem vägfarande lät jag mina dörr upp.
Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
33 Hafver jag såsom en menniska skylt mina skalkhet, att jag skulle hemliga fördölja min missgerning?
ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
34 Hafver jag grufvat mig för stora hopen; eller hafver frändernas föraktelse mig förskräckt? Jag blef stilla, och gick icke ut genom dörrena.
chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
35 Ho gifver mig en förhörare, att den Allsmägtige må höra mitt begär? Att någor måtte skrifva en bok om mine sak;
“Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
36 Så ville jag taga henne uppå mine axlar, och ombinda mig henne såsom en krono.
Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
37 Jag ville förkunna talet på mina gånger, och såsom en Förste ville jag det frambära.
Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
38 Om min jord ropar emot mig, och dess fårar alle tillika gråta;
“Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
39 Hafver jag dess frukt obetalad ätit, och gjort åkermännernas lefverne tungt;
ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
40 Så växe mig tistel för hvete, och törne för bjugg. En ända hafva Jobs ord.
pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.

< Job 31 >