< Job 3 >

1 Derefter upplät Job sin mun, och förbannade sin dag;
Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa.
2 Utbrast, och sade:
Ndipo Yobu anati:
3 Den dagen vare förtappad, på hvilkom jag född är; och den natten, då man sade: En man är aflad.
“Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’
4 Den samme dagen vare mörk, och Gud fråge intet efter honom ofvanefter; ingen klarhet skine öfver honom.
Tsiku limenelo lisanduke mdima; Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso; kuwala kusaonekenso pa tsikulo.
5 Mörkret behålle honom, och töcken blifve öfver honom med tjockt moln; och dimba om dagen göre honom gräselig.
Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli; mtambo uphimbe tsikuli; mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.
6 Den samma nattena begripe mörker; och glädje sig icke ibland årsens dagar, och komme icke i månadetalet.
Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani; usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka, kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.
7 Si, vare den natten ensam, och ingen glädje komme deruti.
Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino; kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.
8 De der dagen förbanna, de förbanne henne; och de som redo äro till att uppväcka Leviathan.
Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo, iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.
9 Hennes stjernor varde mörka; förvänte ljus, och det komme intet; och se intet morgonrodnans ögnabryn;
Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima; tsikulo liyembekezere kucha pachabe ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.
10 Att hon icke igenlyckte mins lifs dörr, och icke bortgömde olyckona för min ögon.
Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.
11 Hvi blef jag icke straxt död i moderlifvet? Hvi vardt jag icke förgjord, då jag utu moderlifvet kommen var?
“Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?
12 Hvi hafva de tagit mig upp i skötet? Hvi hafver jag ditt spenar?
Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo ndi mawere woti andiyamwitsepo?
13 Så låge jag nu, och vore stilla; sofve och hade ro;
Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere; ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo
14 Med Konungar och rådherrar på jordene, som bygga det öde är;
pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi, amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,
15 Eller med Förstar, som guld hafva, och sin hus full med silfver;
pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide, amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.
16 Eller som den der otida född är fördold, och vore icke till; såsom de unga barn, som aldrig hafva sett ljuset.
Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale, ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?
17 Der måste ju de ogudaktige låta af sitt öfvervåld; der hvilas dock de som mycket omak haft hafva.
Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto, ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.
18 Der hafva fångar frid med androm, och höra icke trugarens röst.
A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere; sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.
19 Der äro både små och store; tjenaren och den som ifrå sin herra fri är.
Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko, ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.
20 Hvi är ljus gifvet dem arma, och lif de bedröfvade hjerta;
“Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto, ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,
21 (De der vänta efter döden, och han kommer icke; och uppgrofvo honom väl utu fördold rum;
kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera, amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,
22 De der fröjda sig mycket, och äro glade, att de kunna få grafvena; )
amene amakondwa ndi kusangalala akamalowa mʼmanda?
23 Och dem månne, hvilkens väg fördold är, och för honom af Gudi skyld varder?
Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu amene njira yake yabisika, amene Mulungu wamuzinga ponseponse?
24 Förty min suckan är min dagliga spis; mine tårar äro min dryck.
Mʼmalo moti ndidye, ndimalira, ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.
25 Ty det jag fruktade, det är kommet öfver mig; och det jag räddes, hafver råkat på mig.
Chimene ndinkachiopa chandigwera; chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.
26 Var jag icke lyckosam? Var jag icke stilla? Hade jag icke goda ro? Och sådana oro kommer.
Ndilibe mtendere kapena bata, ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”

< Job 3 >