< Job 15 >
1 Då svarade Eliphas af Thema, och sade:
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 Skall en vis man tala så i vädret, och uppfylla sin buk med väder?
“Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
3 Du straffar med onyttigom ordom, och ditt tal kommer intet till gagns.
Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
4 Du hafver bortkastat räddhågan, och talar förakteliga för Gudi;
Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
5 Ty så lärer din ondska din mun, och du hafver utvalt ena skalkatungo.
Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
6 Din mun skall fördöma dig, och icke jag; dina läppar skola svara dig.
Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
7 Äst du den första menniska, som född är? Äst du för all berg aflader?
“Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
8 Hafver du hört Guds hemliga råd? Och är sjelfva visdomen ringare än du?
Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
9 Hvad vetst du, det vi icke vete? Hvad förstår du, det som icke är när oss?
Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
10 Gråhårote och gamle äro när oss, som länger hafva lefvat än dine fäder.
Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
11 Skulle Guds hugsvalelse så ringa aktas för dig? Men du hafver något hemligit stycke när dig.
Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
12 Hvad tager ditt hjerta före? Hvi ser du så stolt ut?
Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
13 Hvi sätter ditt sinne sig emot Gud, att du låter sådana ord gå af dinom mun?
moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
14 Hvad är en menniska, att hon skulle vara ren; och att han skulle vara rättfärdig, som af qvinno född är?
“Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
15 Si, ibland hans helga är ingen ostraffelig, och himlarna äro icke rene för honom.
Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
16 Huru mycket mer menniskan, som är stygg och ond; den der orättfärdighetena dricker såsom vatten?
nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
17 Jag vill visa dig det, hör mig; jag vill förtälja dig, hvad jag sett hafver;
“Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
18 Hvad de vise sagt hafva, och för deras fader icke hafver fördoldt varit;
zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
19 Hvilkom allena landet gifvet är, så att ingen främmande må gå ibland dem.
(Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
20 En ogudaktig bäfvar i alla sina lifsdagar, och enom tyrann är hans åratal fördoldt.
Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
21 Hvad han hörer, det förskräcker honom; och ändå att frid är, så hafver han dock den sorg, att han skall förderfvas.
Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
22 Han tror icke, att han skall kunna undfly olyckona, och förmodar sig alltid svärdet.
Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
23 När han far ut hit och dit efter sin näring, så tycker honom att hans olyckos tid är för handene.
Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
24 Ångest och nöd förskräcka honom, och slå honom ned, såsom en Konung med enom här;
Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
25 Ty han hafver utsträckt sina hand emot Gud, och emot den Allsmägtiga förstärkt sig.
chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
26 Han löper med hufvudet emot honom, och står halsstyf emot honom.
Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
27 Han hafver upphäfvit sig emot honom, och satt sig hårdt emot honom.
“Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
28 Men han skall bo i nederslagna städer, der inga hus äro; utan ligga i enom hop.
munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
29 Han skall icke varda rik, och hans gods skall icke förökas; och skall icke utspridas i landena.
Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
30 Han skall icke undfly olycko; eldslågen skall förtorka hans grenar; och skall varda borttagen af hans muns anda.
Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
31 Han är så bedragen, att han icke tror att det skall varda värre med honom.
Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
32 Han får en ända, när honom obeqvämt är; och hans gren skall icke grönskas.
Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
33 Han varder afhemtad såsom en omogen drufva af vinträt, och såsom ett oljoträ bortfaller sitt blomster.
Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
34 Ty de skrymtares församling skall blifva ensam, och elden skall förtära hans hus, som gåfvor tager.
Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
35 Han anar olycko, och föder vedermödo; och deras buk bär list fram.
Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”