< Jeremia 44 >

1 Detta är det ord, som till Jeremia, skedde, till alla Judar som uti Egypti land bodde; nämliga i Migdol, i Thahpanhes, i Noph, och de som I det landet Pathros bodde, och sade:
Uthenga umene Yeremiya analandira wonena za Ayuda onse amene ankakhala ku Igupto, ku mizinda ya Migidoli, Tapanesi ndi Mefisi, ndiponso ku Patirosi ndi uwu:
2 Detta säger Herren Zebaoth, Israels Gud: I hafven sett allt det onda, som jag hafver komma låtit öfver Jerusalem, och öfver alla Juda städer, och si, i denna dag äro de öde, och der bor ingen uti;
“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Inu mwaona mavuto aakulu amene ndinawabweretsa pa Yerusalemu ndi mizinda yonse ya Yuda. Lero mizinda yonseyo yasanduka mabwinja, yopanda munthu wokhalamo.
3 Och det för deras ondskos skull, som de bedrefvo, på det de skulle förtörna mig, och gingo bort, och rökte, och tjente androm gudom, hvilka hvarken de, eller I, eller edre fäder, känden.
Zimenezi zinachitika chifukwa cha zoyipa zomwe anachita. Iwo anaputa mkwiyo wanga pofukiza lubani ndi potumikira milungu ina imene iwo kapena inu ngakhalenso makolo anu sanayidziwe.
4 Och jag sände tidigt till eder alla mina tjenare Propheterna, och lät säga eder: Görer dock icke sådana styggelse, de jag hatar.
Kawirikawiri Ine ndakhala ndikutuma atumiki anga, aneneri, amene anati, ‘Musachite chinthu chonyansachi chimene Ine ndimadana nacho!’
5 Men de lydde intet, och böjde ej heller sin öron ifrå sine ondsko, att de måtte omvändt sig, och androm gudom icke rökt.
Koma iwo sanamvere kapena kulabadira; sanatembenuke kusiya zoyipa zawo kapena kuleka kufukiza lubani kwa milungu ina.
6 Derföre upptändes ock min vrede och grymhet, och brann öfver Juda städer, och öfver gatorna i Jerusalem, så att de äro förstörde och öde vordne, såsom det i denna dag finnes.
Nʼchifukwa chake mkwiyo wanga unayaka ngati moto kutentha mizinda ya ku Yuda ndi misewu ya mu Yerusalemu ndi kuyisandutsa bwinja mpaka lero.
7 Nu, så säger Herren Gud Zebaoth, Israels Gud: Hvi gören I dock detta stora onda emot edart eget lif? på det ibland eder skall utrotad varda både man och qvinna, både barn och spenabarn af Juda, och intet af eder qvart blifva;
“Ndiye tsopano Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, ‘Chifukwa chiyani mukufuna kudziwononga chotere? Kodi mukufuna kuti amuna, akazi, ana ndi makanda onse aphedwe ndi kuti mu Yuda musatsale ndi munthu mmodzi yemwe?
8 Att I så förtörnen mig genom edra händers verk, och röken androm gudom uti Egypti land, dit I dragne ären, till att bo der; på det I skolen utrotade varda, och komma till bannor och försmädelse ibland alla Hedningar på jordene.
Chifukwa chiyani mukuputa mkwiyo wanga popembedza mafano pofukiza lubani kwa milungu ina mʼdziko lino la Igupto mʼmene mukukhalamo. Kodi mukuchita zimenezi kuti mudziwononge nokha ndi kuti mudzisandutse chinthu choseketsa ndi chonyozeka pakati pa mitundu yonse ya dziko lapansi?
9 Hafven I förgätit edra fäders olycko, Juda Konungars olycko, deras hustrurs olycko, dertill edra egna olycko, och edra hustrurs olycko, som vederfaren är uti Juda land, och på gatomen i Jerusalem?
Kodi mwayiwala zoyipa zimene anachita makolo anu, mafumu a ku Yuda ndi akazi awo, ndiponso zoyipa zimene munachita inuyo ndi akazi anu mʼdziko la Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu?
10 Likväl äro de ännu intill denna dag intet ödmjukade, och rädas heller intet; och vandra icke uti min lag och rätter, som jag eder och edra fäder föresatt hafver.
Koma mpaka lero simunalape. Simunandilemekeze kapena kumvera malamulo anga amene ndinayikira inuyo ndi makolo anu.
11 Derföre säger Herren Zebaoth, Israels Gud, alltså: Si, jag skall sätta mitt ansigte emot eder till en olycko, och hela Juda skall utrotad varda.
“Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, ‘Ine ndatsimikiza zobweretsa mavuto pa inu ndi kuwatheratu anthu a ku Yuda.
12 Och jag skall taga de öfverblefna af Juda, som sitt ansigte ställt hafva till att draga in uti Egypti land, och bo der; en ände skall varda med dem allom uti Egypti land; genom svärd skola de falla, och genom hunger skola de förgås, både små och store; de skola dö genom svärd och hunger, och skola varda till ett svärjande, vidunder, bannor och försmädelse.
Ndidzatenga anthu otsala a ku Yuda amene atsimikiza zopita ku Igupto ndi kukakhala kumeneko. Onse adzathera ku Igupto. Adzaphedwa ndi lupanga kapena kufa ndi njala. Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, adzaphedwa ndi lupanga kapena kufa ndi njala. Adzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, chinthu choseketsa ndi chonyozeka.
13 Jag skall också hemsöka Egypti lands inbyggare med svärd, hunger och pestilentie, lika som jag i Jerusalem gjort hafver;
Ndidzalanga Ayuda okhala ku Igupto ndi lupanga, njala ndi mliri, ngati mmene ndinalangira anthu a ku Yerusalemu.
14 Så att ingen af Juda återlefvor skall undkomma eller igenblifva, hvilka dock fördenskull hit i Egypti land dragne äro, till att bo här, att de åter måtte komma uti Juda land igen, dit de gerna igenkomma ville, och bo der; men de skola intet komma dit igen, undantagnom dem allena, som hädan fly.
Motero mwa anthu amene anapita ku Igupto palibe ndi mmodzi yemwe adzapulumuke, kapena kukhala ndi moyo, kapena kubwerera ku Yuda. Palibe amene adzabwerere kupatula othawa nkhondo.’”
15 Då svarade alle män, som väl visste att deras hustrur rökte androm gudom, och alla qvinnor, som der i en stor hop stodo, samt med allo folkena, som uti Egypti land och i Pathros bodde, och sade till Jeremia:
Tsono amuna onse amene anadziwa kuti akazi awo ankafukiza lubani kwa milungu ina, ndiponso akazi onse amene anali pamenepo, gulu lalikulu la anthu, pamodzi ndi anthu onse amene amakhala ku Patirosi mʼdziko la Igupto, anati kwa Yeremiya,
16 Efter det ord, som du oss säger i Herrans Namn, vilje vi intet höra dig;
“Ife sitimvera uthenga umene watiwuza mʼdzina la Yehova!
17 Utan vi vilje göra efter allt det ord, som utaf vårom mun går, och vilje röka himmelens Drottning, och offra henne drickoffer, såsom vi och våre fäder, våre Konungar och Förstar, gjort hafva i Juda städer, och uppå gatomen i Jerusalem; då hade vi ock bröd nog, och oss gick väl, och sågom ingen olycko.
Koma tidzachitadi chilichonse chimene tinanena kuti tidzachita: Tidzafukiza lubani kwa mfumukazi yakumwamba ndipo tidzayipatsa nsembe yachakumwa ngati mmene tinkachitira ifeyo ndi makolo athu, mafumu athu ndi akuluakulu mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu. Nthawi imeneyo ife tinali ndi chakudya chochuluka ndipo tinali pabwino, sitimapeza mavuto.
18 Men sedan vi återvände att röka himmelens Drottning, och offra henne drickoffer, hafve vi alla vedermödo lidit, och äre genom svärd och hunger förgångne.
Koma kuchokera nthawi imene tinasiya kufukiza lubani ndi kupereka chopereka cha chakumwa kwa mfumukazi yakumwamba, ifeyo takhala tikusowa zinthu ndipo takhala tikuphedwa ndi lupanga ndi kufa ndi njala.”
19 Och om vi än röke himmelens Drottning, och drickoffer offre, det göre vi ju icke utan våra mäns vilja, att vi bake henne kakor, och drickoffer offre till hennes tjenst?
Akazi anawonjezera kunena kuti, “Pamene tinkafukiza lubani kwa mfumukazi yakumwamba ndi kuyipatsa chopereka cha chakumwa, kodi suja amuna athu ankavomereza mmene timayipangira mfumukazi yakumwambayo makeke abwino olembapo chinthunzi chake ndi kuyipatsa chopereka cha chakumwa?”
20 Då sade Jeremia till allt folket, både män, qvinnor och allt folket, som honom så svarat hade:
Yeremiya atamva kuyankha kumeneku anawawuza kuti,
21 Ja, jag menar ock, att Herren hafver tänkt uppå det rökande, som I uti Juda städer och på Jerusalems gator bedrifvit hafven, samt med edra fäder, Konungar, Förstar, och allt folket i landena, och hafver lagt det uppå hjertat;
“Kodi mukuganiza kuti Yehova nʼkuyiwala kuti inuyo ndi makolo anu, mafumu anu ndi akuluakulu anu, ndiponso anthu onse, munkafukiza lubani kwa mafano a mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu?
22 Så att Herren icke mer lida kunde edart onda väsende och styggelse, som I gjorden; derföre ock edart land är vordet till öde, vidunder, och till bannor, så att der ingen inne bor, såsom det i denna dag tillgår.
Ndiye Yehova sakanathanso kupirira ndi machitidwe anu ndi zonyansa zimene munkachita. Nʼchifukwa chake dziko lanu linasanduka chipululu, chinthu choopsa ndi chotembereredwa. Dziko lopandamo anthu monga zilili lero lino.
23 Derföre att I rökten, och emot Herran syndaden, och icke lydden Herrans röst, och vandraden i hans lag, rätter och vittnesbörder; fördenskull är eder ock sådana olycka vederfaren, såsom det i denna dag befinnes.
Mavuto awa akugwerani chifukwa munkafukiza lubani ndipo munkachimwira Yehova pokana kumvera mawu ake ndi kutsatira malamulo ndi malangizo ake.”
24 Och Jeremia sade till allt folket, och till alla qvinnorna: Hörer Herrans ord, alle I af Juda, som uti Egypti land ären.
Kenaka Yeremiya anawuza anthu onse, makamaka akazi kuti, “Imvani mawu a Yehova, anthu onse a ku Yuda amene muli mu Igupto.
25 Detta, säger Herren Zebaoth, Israels Gud: I och edra qvinnor hafva med edrom mun talat, och med edra händer fullkomnat det I saden: Vi vilje hålla vår löfte, som vi himmelens Drottning lofvat hafve, att vi henne röke, och drickoffer offre; nu väl, I hafven hållit edart löfte, och fullföljt det med gerningarna.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Inu ndi akazi anu munalonjeza ndi pakamwa panu, ndipo malonjezowo mwakwaniritsa. Inu munanena kuti, ‘Tidzachita zimene tinalonjeza, kufukizira lubani mfumukazi yakumwamba ndi kuyipatsa chopereka cha zakumwa.’ Tsopano chitanitu zimene munalonjezazo! Kwaniritsani malumbiro anu. “Yambani, chitani zimene munalonjeza! Kwaniritsani malumbiro anu!
26 Så hörer nu Herrans ord, I alle af Juda, I som bon uti Egypti land; si, jag svär vid mitt stora Namn, säger Herren, att mitt Namn icke mer skall, genom någors mans munn af Juda, uti hela Egypti land nämndt varda, den der säger: Så visst som Herren Herren lefver.
Koma imvani mawu a Yehova, inu Ayuda nonse amene mukukhala mu Igupto: Yehova akuti, ‘Ine ndikulumbira mʼdzina langa lopambana kuti palibe wochokera ku Yuda amene akukhala mu Igupto amene adzatchule dzina langa polumbira kuti, ‘Pali Ambuye Yehova wamoyo.’
27 Si, jag vill vaka öfver dem till ondt, och intet godt, så att ho som af Juda uti Egypti land är, han skall genom svärd och hunger förgås, tilldess att det hafver en ända med dem.
Pakuti ndionetsetsa kuti ndiwachitire choyipa, osati chabwino. Anthu a ku Yuda amene akukhala ku Igupto adzaphedwa pa nkhondo. Ena adzafa ndi njala mpaka onse atatheratu.
28 Men de som svärdet undkomma, de skola likväl komma utur Egypti land in uti Juda. land igen, med en liten hop; och alltså skola då alle de öfverblefne af Juda, som in uti Egypti land dragne voro, till att bo der, förnimma, hvilkens ord sant vordet är, mitt eller deras.
Amene adzapulumuke ku lupanga ndi kubwerera ku dziko la Yuda kuchokera ku Igupto adzakhala ochepa kwambiri. Choncho otsala onse a ku Yuda amene anapita kukakhala ku Igupto adzadziwa kuti mawu woona ndi ati, anga kapena awo.
29 Och detta skall vara till ett tecken, säger Herren, att jag eder i desso rummena hemsöka vill, på det I skolen veta, att min ord skola sann varda öfver eder till olycko.
“Ine Yehova ndikukupatsani chizindikiro chakuti ndidzakulangani ku malo ano. Motero mudzadziwa kuti mawu anga akuti ndidzakulangani ndi woona.
30 Så säger Herren: Si, jag skall öfvergifva Pharao Hophra, Konungen i Egypten, uti hans fiendars händer, och deras som efter hans lif stå, likasom jag Zedekia, Juda Konung, öfvergifvit hafver uti NebucadNezars, Konungens i Babel, hans fiendas, hand, och den efter hans lif stod.
Yehova akuti, ‘Ine ndidzamupereka Farao Hofira mfumu ya Igupto kwa adani ake amene akufuna kumupha, monga momwe ndinaperekera Zedekiya mfumu ya Yuda kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, mdani wake amene ankafuna kumupha.’”

< Jeremia 44 >