< Jeremia 43 >

1 Då Jeremia all Herrans deras Guds ord till allt folket uttalat hade, såsom Herren deras Gud honom all dessa ord till dem befallt hade,
Yeremiya atatsiriza kuwawuza anthuwo mawu onse a Yehova Mulungu wawo, amene Yehova anamutuma kuti akawawuze,
2 Sade Asaria, Hosaja son, och Johanan, Kareahs son, och alle öfverdådige män till Jeremia: Du ljuger; Herren vår Gud hafver intet sändt dig till oss, eller sagt: I skolen icke draga in uti Egypten, till att bo der;
Azariya mwana wa Hosayia ndi Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi anthu onse odzikuza anawuza Yeremiya kuti, “Ukunama iwe! Yehova Mulungu wathu sanakutume kuti unene kuti, ‘Musapite ku Igupto kukakhala kumeneko.’
3 Men Baruch, Neria son, eggar dig emot oss, på det vi skolom de Chaldeer öfvergifne varda, att de skola döda oss, och bortföra oss till Babel.
Koma ndi Baruki mwana wa Neriya amene akukulimbikitsa kuti utiletse zopita ku Igupto ndi kuti mʼmalo mwake tidzipereke mʼmanja mwa Ababuloni, kuti iwo atiphe kapena kutitenga ukapolo ku Babuloni.”
4 Alltså ville Johanan, Kareahs son, och alle höfvitsmännerna, samt med allo folkena, intet lyda Herrans röst, att de måtte blifvit i Juda lande;
Motero Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi anthu onse sanamvere lamulo la Yehova loti akhale mʼdziko la Yuda.
5 Utan Johanan, Kareahs son, och alle höfvitsmännerna togo till sig alla qvarlefda af Juda, de som ifrån all folk dit flydde och igenkomne voro, till att bo i Juda lande;
Mʼmalo mwake, Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo anatenga anthu onse otsala a ku Yuda amene anabwera kudzakhala mʼdziko la Yuda kuchokera ku mayiko onse kumene anabalakirako.
6 Nämliga män, qvinnor och barn; dertill Konungens döttrar, och alla själar som NebuzarAdan, höfvitsmannen när Gedalia, Ahikams sone, Saphans sons, låtit hade, och Propheten Jeremia, och Baruch, Neria son;
Mʼgulu la anthu otengedwalo munali amuna onse, akazi ndi ana, ana aakazi a mfumu, ndiponso anthu amene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anawasiya kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani pamodzinso ndi mneneri Yeremiya ndi Baruki mwana wa Neriya.
7 Och drogo in uti Egypti land; ty de ville intet höra Herrans röst; och kommo till Thahpanhes.
Kotero anthuwo analowa mʼdziko la Igupto chifukwa anakana kumvera Yehova, nakafika ku Tapanesi.
8 Och Herrans ord skedde till Jeremia i Thahpanhes, och sade:
Ndipo Yehova anayankhula ndi Yeremiya ku Tapanesi kuti,
9 Tag stora stenar, och graf dem neder uti enom tegelugn, som är vid porten åt Pharaos hus i Thahpanhes, så att de män af Juda se deruppå;
“Tenga miyala inayi yayikulu ndipo uyikwirire mʼdothi pa chiwundo cha polowera ku nyumba yaufumu ya Farao ku Tapanesi. Uchite zimenezi Ayuda onse akuona.
10 Och säg till dem: Så säger Herren Zebaoth, Israels Gud: Si jag skall sända bort, och låta hemta min tjenare NebucadNezar, Konungen i Babel, och skall sätta hans stol ofvanuppå dessa stenarna, som jag här nedgräfvit hafver, och han skall slå sin tjäll deröfver.
Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Ndidzayitana mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo adzakhazika mpando wake waufumu pa miyala imene ndayikwirira apayi. Iye adzafunyulula tenti yake yaufumu pa miyala imeneyi.
11 Och han skall komma, och slå Egypti land, och dräpa hvem det uppå råkar; för fångar bortföra hvem det uppå råkar; med svärd slå hvem det uppå råkar.
Iye adzabwera kudzathira nkhondo Igupto. Iwo oyenera kufa ndi mliri adzafa ndi mliri, iwo oyenera kutengedwa ukapolo adzatengedwa ukapolo, ndipo iwo oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga.
12 Och jag skall tända eld uppå de afgudars hus uti Egypten, att han dem uppbränner och bortförer; och han skall utikläda sig Egypti land, lika som en herde utikläder sig sin mantel, och draga sin väg dädan med frid.
Adzayatsa moto mʼnyumba zopembedzera milungu ya Igupto. Adzayeretsa dziko la Igupto monga momwe mʼbusa amayeretsera chovala chake pochotsamo nsabwe. Pambuyo pake adzachoka mʼdziko la Igupto mwa mtendere.
13 Och han skall sönderslå de belätestodar i BethSemes, i Egypti land, och uppbränna de afgudakyrkor uti Egypten med eld.
Ku Iguptoko adzagwetsa zipilala zachipembedzo za ku nyumba yopembedzera mulungu wa dzuwa. Adzatentha ndi moto nyumba za milungu ya ku Igupto.’”

< Jeremia 43 >