< Jeremia 40 >
1 Detta är det ord, som af Herranom skedde till Jeremia, då NebuzarAdan, höfvitsmannen, gaf honom lös i Rama; ty han var ock bunden med kedjor ibland alla dem som i Jerusalem och Juda fångne voro, att man dem till Babel bortföra skulle.
Yehova anayankhula ndi Yeremiya pamene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anamasula Yeremiyayo ku Rama. Anamupeza Yeremiya ali womangidwa ndi unyolo pamodzi ndi amʼndende ena onse a ku Yerusalemu ndi a ku Yuda amene ankapita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
2 Då nu höfvitsmannen hade låtit hemta Jeremia till sig, sade han till honom: Herren din Gud hafver talat denna olyckona öfver detta rummet;
Mtsogoleriyu anamupeza Yeremiya, anamuwuza kuti, “Yehova Mulungu wako analengeza kale zakuti malo ano adzawonongedwa.
3 Och Herren hafver också låtit kommat, och gjort som han det sagt hafver; ty I hafven syndat emot Herran, och icke lydt hans röst, derföre är eder sådant vederfaret.
Ndipo tsopano Yehova wachitadi zimenezi monga mmene ananenera. Izi zonse zachitika chifukwa anthu inu munachimwira Yehova ndipo simunamumvere.
4 Nu si, jag hafver i dag gjort dig lös utu kedjorna, der dina händer med bundna voro; lyster dig draga med mig till Babel, så kom, jag vill veta ditt bästa; lyster dig ock icke draga med mig till Babel, så låt det blifva; Si, der hafver du hela landet för dig; hvar dig tycker godt vara och dig behagar, dit gack.
Koma tsopano taona, lero ndikukumasula unyolo umene unali mʼmanja mwako. Ngati ukufuna kupita nane ku Babuloni, tiye ndipo adzakusamala bwino. Koma ngati sukufuna kupita, ndiye usapite. Dziko ndi limeneli monga ukulioneramo. Uli ndi ufulu kupita kulikonse kumene ukufuna.”
5 Ty fram länger varder ingen omvändning mer; derföre må du vända om igen till Gedalia, Ahikams son, Saphans sons, den Konungen i Babel öfver Juda städer satt hafver, och blifva när honom ibland folket, eller gå bort, dit dig bäst täckes. Och höfvitsmannen gaf honom täring och skänker, och lät honom gå.
Yeremiya asanayankhe, Nebuzaradani anamuwuzanso kuti, “Ngati supita ndiye pita, ubwerere kwa Gedaliya, mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani, amene mfumu ya ku Babuloni inamusankha kuti akhale bwanamkubwa wa Yuda. Ukakhale naye pakati pa anthu, kapena upite kulikonse ukufuna.” Ndipo mtsogoleri uja anamupatsa Yeremiya chakudya ndi mphatso zina ndi kumulola kuti apite.
6 Alltså kom Jeremia till Gedalia, Ahikams son, i Mizpa, och blef när honom ibland folket, som ännu i landena qvart blifvet var.
Motero Yeremiya anapita kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu ku Mizipa ndipo anakakhala naye kumeneko pakati pa anthu amene anatsala mʼdzikomo.
7 Då nu de höfvitsmän, som i markene lågo, samt med deras folk, fingo veta, att Konungen i Babel hade satt Gedalia, Ahikams son, öfver landet, och både öfver män och qvinnor, barn och de ringesta i landena, som till Babel icke förde voro,
Panali atsogoleri ena a nkhondo ndi anthu awo amene sanadzipereke nawo. Iwowa anamva kuti mfumu ya ku Babuloni inasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu kukhala bwanamkubwa wa dzikolo ndipo kuti yamuyika kukhala wolamulira amuna, akazi ndi ana amene anali osauka kwambiri mʼdzikomo, amene sanawagwire ukapolo kupita nawo ku Babuloni.
8 Kommo de till Gedalia i Mizpa, nämliga: Ismael, Nethanja son, Johanan och Jonathan, Kareahs söner, och Seraja, Thanhumeths son, och Ephai söner af Nethophat, och Jesania, Mahachati son, samt med deras män.
Iwowa anapita ku Mizipa kwa Gedaliya. Amene anapitawo ndi awa: Ismaeli mwana wa Netaniya, Yohanani ndi Yonatani ana a Kareya, Seraya mwana wa Tanihumeti, ana a Efai a ku Netofa, ndi Yezaniya mwana wa Maaka, iwowo pamodzi ndi anthu awo.
9 Och Gedalia, Ahikams son, Saphans sons, gjorde dem och deras män en ed, och sade: Frukter eder intet att vara de Chaldeer underdånige; blifver i landena, och varer Konungenom i Babel underdånige, så varder eder väl gåendes.
Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani, anawalonjeza iwo pamodzi ndi anthuwo mwalumbiro. Ndipo anati, “Musaope kuwatumikira Ababuloni. Khalani mʼdziko muno, tumikirani mfumu ya ku Babuloni, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino.
10 Si, jag bor här i Mizpa, på det jag skall tjena de Chaldeer, som till oss komma; derföre församler in vin, och fikon, och oljo, och låter det uti edor fat, och bor uti edra städer, som I fått hafven.
Ine ndidzakhala ku Mizipa kuti ndizikuyimirirani kwa Ababuloni amene azidzabwera kwa ife, koma inu muzikolola vinyo wanu, zipatso zanu, mafuta anu ndi kuzisunga mʼmitsuko yanu, nʼkumakhala mʼmizinda imene mwalandayo.”
11 Och alle de Judar, som i Moabs land voro, och Ammons barnas, och i Edom, och i all land, då de hörde att Konungen i Babel hade låtit somliga qvara blifva i Juda, och satt Gedalia, Ahikams son, Saphans sons, öfver dem,
Nawonso Ayuda onse a ku Mowabu, ku Amoni, ku Edomu ndi a ku mayiko ena onse anamva kuti mfumu ya ku Babuloni inasiyako anthu ena ku Yuda ndipo kuti inasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kukhala bwanamkubwa wawo.
12 Kommo de alle igen ifrån all rum, dit de hade fördrefne varit, in uti Juda land, till Gedalia i Mizpa, och församlade in ganska mycket vin och fikon.
Tsono Ayuda onsewo anabwerera ku Yuda, ku Mizipa kwa Gedaliya, kuchokera ku mayiko onse kumene anabalalikira. Ndipo anakolola zipatso zochuluka ndi vinyo wambiri.
13 Men Johanan, Kareahs son, samt med alla höfvitsmännerna, som i markene legat hade, kommo till Gedalia i Mizpa;
Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri a ankhondo onse amene sanadzipereke aja anabwera ku Mizipa kwa Gedaliya
14 Och sade till honom: Vetst du ock, att Baalis, Ammons barnas Konung, hafver sändt hit Ismael, Nethanja son, att han skall slå dig ihjäl. Så ville Gedalia, Ahikans son, icke tro dem.
ndipo anamufunsa kuti, “Kodi sukudziwa kuti Baalisi mfumu ya Aamoni watuma Ismaeli mwana wa Netaniya kuti akuphe?” Koma Gedaliya mwana wa Ahikamu sanawankhulupirire.
15 Då sade Johanan, Kareahs son, till Gedalia hemliga i Mizpa: Käre, jag vill gå bort, och slå Ismael, Nethanja son, ihjäl, så att ingen skall få vetat; hvi skall han slå dig, att alle de Judar, som till dig församlade äro, skola förströdde varda, och de som ännu af Juda qvare blefne äro, förgås?
Tsono Yohanani mwana wa Kareya, mwamseri anawuza Gedaliya ku Mizipa kuti, “Loleni ndipite ndikaphe Ismaeli mwana wa Netaniya, ndipo palibe amene ati adziwe. Akuphereninji ndi kuchititsa Ayuda onse, amene akuzungulirani kuti abalalike ndi kuti otsala a ku Yuda awonongeke?”
16 Men Gedalia, Ahikams son, sade till Johanan, Kareahs son: Det skall du icke göra; det är intet sant, som du om Ismael säger.
Koma Gedaliya mwana wa Ahikamu anawuza Yohanani mwana wa Kareya kuti, “Usachite zimenezo! Zimene ukunena za Ismaeli ndi zabodza.”