< Jeremia 38 >
1 Men Sephatja, Matthans son, och Gedalia, Pashurs son, och Juchal, Selemja son, och Pashur, Malchia son, hörde de orden, som Jeremia till allt folket talade, och sade:
Sefatiya mwana wa Matani, Gedaliya mwana wa Pasi-Huri, Yukali mwana wa Selemiya, ndi Pasi-Huri mwana wa Malikiya anamva zimene Yeremiya ankawuza anthu onse kuti,
2 Detta säger Herren: Den som blifver i denna stadenom, han måste dö för svärd, hunger och pestilentie; men den som utgår till de Chaldeer, han skall blifva lefvandes, och gå af med sitt lif, såsom med ett byte.
“Yehova akuti, ‘Aliyense amene akhale mu mzinda muno adzafa ndi nkhondo njala kapena mliri. Koma aliyense amene atatuluke kukadzipereka kwa Ababuloni adzapulumutsa moyo wake; iyeyo adzakhala ndi moyo.
3 Ty så säger Herren: Denne staden skall gifven varda Konungens här af Babel, och de skola vinna honom.
Mzinda uno udzaperekedwa ndithu kwa gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni, amene adzawulande.’”
4 Då sade Förstarna till Konungen: Låt dock dräpa denna mannen; ty med det sättet afvänder han det krigsfolk, som ännu qvart är i denna stadenom; sammalunda ock allt folket, efter han sådana ord till dem säger; ty den mannen söker icke efter det som folkets bästa är, utan det värsta.
Tsono akuluakuluwo anawuza mfumu kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa. Iye akutayitsa mtima asilikali pamodzi ndi anthu onse amene atsala mu mzinda muno, chifukwa cha zimene akuwawuza. Munthu ameneyu sakufunira zabwino anthuwa koma chiwonongeko chawo.”
5 Konungen Zedekia sade: Si, han är i edra händer; ty Konungen förmår intet emot eder.
Mfumu Zedekiya anayankha kuti, “Munthuyu ali mʼmanja mwanu. Ine sindingakuletseni chimene mukufuna kumuchitira.”
6 Då togo de Jeremia, och kastade honom uti Malchia kulo, Hammelechs sons, den på gården för fångahuset var; och släppte honom med tåg neder i kulona, der intet vatten, utan träck, uti var; och Jeremia sank neder i träcken.
Choncho iwo anatenga Yeremiya nakamuponya mʼchitsime cha Malikiya, mwana wa mfumu, chimene chinali mʼbwalo la alonda. Iwo anamutsitsira mʼdzenjemo ndi chingwe. Munalibe madzi koma matope okhaokha, ndipo Yeremiya anamira mʼmatopewo.
7 Då nu EbedMelech, den Ethiopen, en kamererare i Konungshusena, hörde att de hade kastat Jeremia uti kulona, och Konungen satt uti BenJamins port,
Koma Ebedi-Meleki, Mkusi, mmodzi mwa anthu ofulidwa ogwira ntchito mʼnyumba ya mfumu, anamva kuti Yeremiya anamuponya mʼchitsime. Nthawi imeneyo nʼkuti mfumu ili ku chipata cha Benjamini.
8 Så gick EbedMelech utu Konungshusena, och talade med Konungenom, och sade;
Ebedi-Meleki anatuluka ku nyumba ya mfumu kukayiwuza kuti,
9 Min herre Konung, de män handla illa med Propheten Jeremia, att de hafva kastat honom i kulona, der han må af hunger dö; ty i stadenom är intet bröd mer.
“Mbuye wanga mfumu, zimene anthu awa amuchitira mneneri Yeremiya ndi zoyipa kwambiri. Iwo amuponya mʼchitsime, ndipo adzafa ndi njala chifukwa buledi watha mu mzinda muno.”
10 Då befallde Konungen EbedMelech den Ethiopen, och sade: Tag tretio män med dig af dessa, och tag Propheten Jeremia upp utu kulone, förr än han dör.
Tsono mfumu inalamula Ebedi-Meleki, Mkusi, kuti, “Tenga anthu makumi atatu, ndipo mukamutulutse mʼchitsimemo mneneri Yeremiya asanafe.”
11 Och EbedMelech tog männerna med sig, och gick uti Konungshuset under fataburen, och tog der gamla och utslitna paltor, och lät dem neder med ett rep till Jeremia i kulona.
Pamenepo Ebedi-Meleki anatenga anthuwo, napita nawo ku nyumba ya mfumu ya pansi pa chipinda chosungiramo chuma. Kumeneko anakatengako sanza ndipo anatsitsira sanzazo ndi chingwe mʼchitsime mʼmene munali Yeremiya.
12 Och EbedMelech, den Ethiopen, sade till Jeremia: Låt denna gamla och utslitna paltorna under dina armar omkring repet. Och Jeremia gjorde så.
Ebedi-Meleki, Mkusi, anawuza Yeremiya kuti, “Ika sanzazo mkwapa mwako kuti zingwe zingakupweteke.” Yeremiya anachitadi zimenezi,
13 Och de drogo Jeremia upp med repena utu kulone, och Jeremia blef så i gårdenom för fångahuset.
ndipo anamukoka ndi zingwe ndi kumutulutsa mʼchitsimecho. Ndipo Yeremiya anakhalabe ku bwalo la alonda.
14 Och Konung Zedekia sände bort, och lät hemta Propheten Jeremia till sig, till den tredje ingången på Herrans hus; och Konungen sade till Jeremia: Jag vill fråga dig något; käre, fördölj intet för mig.
Tsiku lina Mfumu Zedekiya anayitana mneneri Yeremiya ndipo anabwera naye ku chipata chachitatu cha Nyumba ya Yehova. Mfumu inawuza Yeremiya kuti, “Ndikufuna kukufunsa kanthu kena, ndipo usandibisire chilichonse.”
15 Jeremia sade till Zedekia: Om jag säger dig något, så dräper du mig dock; och om jag gifver dig råd, så lyder du mig intet.
Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Ndikakuyankhani, kodi simundipha? Ngakhaletu ine nditakulangizani, inu simudzandimvera.”
16 Då svor Konung Zedekia Jeremia hemliga, och sade: Så sant som Herren lefver, den oss denna själena gjort hafver, vill jag icke dräpa dig, eller få dig de män i händer, som efter ditt lif stå.
Koma Mfumu Zedekiya mwachinsinsi inalumbira kwa Yeremiya kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene amatipatsa moyo, sindidzakupha ngakhalenso kukupereka kwa amene akufuna kukuphawa.”
17 Och Jeremia sade till Zedekia: Detta säger Herren Gud Zebaoth, Israels Gud: Om du utgår till Konungens Förstar af Babel, så skall du blifva lefvandes, och denne staden skall icke uppbränd varda, utan du och ditt hus skolen vid lif blifva.
Pamenepo Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ngati mutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mudzakhala ndi moyo ndipo mzinda uno sadzawutentha, inu pamodzi ndi banja lanu mudzakhala ndi moyo.
18 Men om du icke utgår till Konungens Förstar af Babel, så varder denne staden uti de Chaldeers händer gifven, och de skola uppbränna honom i eld, och du skall ej heller undkomma deras händer.
Koma ngati simutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mzinda uno udzaperekedwa kwa Ababuloni ndipo adzawutentha; inuyo simudzapulumuka mʼdzanja mwawo.’”
19 Konung Zedekia sade till Jeremia: Jag befruktar mig, att jag må varda gifven de Judar i händer, som till de Chaldeer fallne äro, att de skola bespotta mig.
Mfumu Zedekiya inati kwa Yeremiya, “Ine ndikuopa Ayuda amene anathawira kale kwa Ababuloni, pakuti mwina Ababuloniwo adzandipereka kwa Ayudawo ndipo iwowo adzandizunza.”
20 Jeremia sade: Man varder dig intet gifvandes; käre, hör dock Herrans röst, den jag dig säger; så skall dig väl gå, och du skall lefvandes blifva.
Yeremiya anayankha kuti, “Ngati mumvera Yehova ndi kuchita zimene ndakuwuzani, ndiye kuti zinthu zidzakuyenderani bwino. Inu simudzaphedwa.
21 Men om du icke utgår, så är detta det ord, som Herren mig undervist hafver:
Koma mukakana kudzipereka, chimene Yehova wandiwululira ndi ichi:
22 Si, alla de qvinnor, som ännu qvara äro uti Juda Konungs hus, de måste ut till Konungens Förstar af Babel; de samma skola då säga: Ack! dine tröstare hafva bedragit och förfört dig, och fört dig neder i träcken, och låta dig nu ligga.
Akazi onse amene atsala mʼnyumba ya mfumu ya Yuda adzaperekedwa kwa akuluakulu a mfumu ya ku Babuloni. Akazi amenewo adzakuwuzani kuti, “‘Abwenzi ako okhulupirika aja anakusokeretsa, ndipo anakugonjetsa. Poti tsopano miyendo yako yazama mʼmatope; abwenzi ako aja akusiya.’
23 Alltså skola då alla dina hustrur och barn utkomma till de Chaldeer, och du sjelf skall icke kunna undkomma deras händer; utan du skall varda gripen af Konungenom i Babel, och denne staden skall med eld uppbränd varda.
“Akazi pamodzi ndi ana anu adzaperekedwa kwa Ababuloni. Inuyo simudzapulumuka mʼmanja mwawo koma mfumu ya ku Babuloni idzakugwirani; mzinda uno adzawutentha.”
24 Och Zedekia sade till Jeremia: Si till, att ingen får dessa orden veta, så varder du icke dödad.
Pamenepo Zedekiya anati kwa Yeremiya, “Usawuze munthu wina aliyense zimene takambiranazi, ukatero udzaphedwa.
25 Och om Förstarna få veta, att jag hafver talat med dig, och de komma till dig, och säga: Säg, hvad hafver du talat med Konungenom? dölj det icke för oss, så vilje vi icke dräpa dig; och hvad hafver Konungen talat med dig?
Akuluakulu akamva kuti ndinayankhula nawe ndipo akabwera kwa iwe nʼkudzakufunsa kuti, ‘Tiwuze zimene unanena kwa mfumu ndi zimene mfumu inanena kwa iwe; usatibisire, ukatero tidzakupha,’
26 Så säg till dem: Jag hafver bedit Konungen, att han icke skall låta mig åter komma uti Jonathans hus igen, att jag icke blifver der död.
udzawawuze kuti, ‘Ine ndimapempha mfumu kuti isandibwezerenso ku nyumba ya Yonatani kuti ndikafere kumeneko.’”
27 Då kommo alle Förstarna till Jeremia, och frågade honom; och han sade dem, såsom Konungen honom befallt hade. Så öfvergåfvo de honom, efter de intet kunde förfara af honom.
Akuluakulu onse anabweradi kwa Yeremiya kudzamufunsa. Iye anawayankha monga momwe mfumu inamulamula. Choncho palibe amene ananenanso kanthu, pakuti palibe amene anamva zomwe anakambirana ndi mfumu.
28 Och Jeremia blef uti gårdenom för fångahuset, allt intill den dagen då Jerusalem vunnet vardt; och der var han, då Jerusalem vardt vunnet.
Ndipo Yeremiya anakhalabe mʼbwalo la alonda mpaka tsiku limene mzinda wa Yerusalemu unalandidwa.