< Jeremia 35 >

1 Detta är det ord, som af Herranom skedde till Jeremia, i Jojakims, Josia sons, Juda Konungs, tid, och sade:
Yehova anayankhula ndi Yeremiya nthawi ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, kuti:
2 Gack bort uti de Rechabiters hus, och tala med dem, och haf dem in uti Herrans hus uti en kammar, och skänk dem vin.
“Pita ku banja la Arekabu ndipo ukawayitane kuti abwere mʼchipinda chimodzi cha Nyumba ya Yehova ndipo akafika uwapatse vinyo kuti amwe.”
3 Då tog jag Jaasanja, Jeremia son, Habazinia sons, samt med hans bröder, och alla hans söner, och hela de Rechabiters hus;
Choncho ndinakatenga Yaazaniya (mwana wa Yeremiya winanso amene anali mwana wa Habaziniya), abale ake, ana ake onse aamuna ndi banja lonse la Arekabu.
4 Och hade dem in uti Herrans hus, uti Hanans barnas, Jigdalja sons, den Guds mansens, kammar, hvilken vid Förstarnas kammar är, ofvanför Maaseja, Sallums sons, dörravaktarens kammar.
Ndinabwera nawo ku Nyumba ya Yehova, ku chipinda cha ophunzira a mneneri Hanani mwana wa Igidaliya, munthu wa Mulungu. Chipinda chimenechi chinali pafupi ndi chipinda cha akuluakulu, chimene chinali pamwamba pa chipinda cha Maaseya mwana wa Salumu, mlonda wa pa khomo.
5 Och jag satte de Rechabiters hus barnom kannor före, fulla med vin, och skålar, och sade till dem: Dricker vin.
Kenaka ndinayika mabotolo odzaza ndi vinyo ndi zikho zake pamaso pa Arekabu ndipo ndinawawuza kuti, “Imwani vinyoyu.”
6 Men de svarade: Vi dricke intet vin; ty vår fader Jonadab, Rechabs son, hafver budit oss, och sagt: I och edor barn skolen aldrig något vin dricka;
Koma iwo anayankha kuti, “Ife sitimwa vinyo, chifukwa kholo lathu Yehonadabu mwana wa Rekabu anatilamula kuti, ‘Inuyo ngakhale zidzukulu zanu, musadzamwe vinyo mpaka kalekale.
7 Och intet hus bygga, ingen säd så, ingen vingård plantera, eller hafva; utan skolen bo i tjäll i alla edra lifsdagar; på det I mågen länge lefva i landena, der I uti vandren.
Musadzamange nyumba kapena kufesa mbewu, kapena kulima minda ya mpesa; musadzakhale ndi zinthu zimenezi. Mʼmalo mwake muzidzakhale mʼmatenti. Mukadzatero mudzakhala nthawi yayitali mʼdziko limene mukukhalamo.’
8 Alltså lydom vi vår faders röst, Jonadabs, Rechabs sons, i allt det han oss budit hafver, så att vi intet vin dricke i våra lifsdagar, hvarken vi eller våra hustrur, eller söner, eller döttrar;
Ife takhala tikumvera zonse zimene kholo lathu Yehonadabu mwana wa Rekabu anatilamula. Ife ngakhale akazi athu kapena ana athu aamuna ndi aakazi sitinamwepo vinyo
9 Och byggom ej heller någor hus, der vi uti bo, och hafvom hvarken vingårdar, eller åkrar, eller säd;
kapena kumanga nyumba kuti tizikhalamo kapenanso kukhala ndi minda ya mpesa, minda ina iliyonse kapena mbewu.
10 Utan bom uti tjäll, och lydom, och görom all ting, såsom vår fader Jonadab oss budit hafver.
Koma takhala mʼmatenti ndipo tamvera kwathunthu chilichonse chimene kholo lathu Yehonadabu anatilamula.
11 Men då NebuchadNezar, Konungen i Babel, drog hitupp i landet, sade vi: Kommer, låter oss draga till Jerusalem, för de Chaldeers och Syrers här; och så hafve vi sedan blifvit här i Jerusalem.
Koma pamene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anathira nkhondo dziko lino, ife tinati, ‘Tiyeni tichoke, tipite ku Yerusalemu kuti tithawe magulu ankhondo a Akasidi ndi Aaramu.’ Kotero ife takhala tikukhala mu Yerusalemu.”
12 Då skedde Herrans ord till Jeremia, och sade:
Yehova anayankhulanso ndi Yeremiya kuti,
13 Detta säger Herren Zebaoth, Israels Gud: Gack bort, och säg till dem i Juda, och till de inbyggare i Jerusalem: Viljen I då icke bättra eder, så att I lyden min ord? säger Herren.
“Iyeyu, Yehova Mulungu wa Israeli anawuza Yeremiya kuti: Pita ukawawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Kodi simungatengeko phunziro ndi kumvera mawu anga?’ akutero Yehova.
14 Jonadabs ord, Rechabs sons, som han sinom barnom budit hafver, att de intet vin dricka skulle, de varda hållen, så att de dricka intet vin intill denna dag, derföre att de lyda deras faders bud; men jag hafver tidigt låtit predika eder, likväl hören I mig intet.
‘Yehonadabu mwana wa Rekabu analamula ana ake kuti asamwe vinyo ndipo lamulo limeneli alisunga. Mpaka lero lino iwo samwa vinyo, chifukwa akumvera lamulo la kholo lawo. Koma Ine ndakhala ndikuyankhula nanu kawirikawiri kukuchenjezani, koma inu simunandimvere Ine.
15 Så hafver jag ock tidigt sändt till eder alla mina tjenare Propheterna, och låtit säga: Vänder eder om, hvar och en ifrå sitt onda väsende, och bättrer edart lefverne, och efterföljer icke andra gudar, till att tjena dem, så skolen I blifva i landena, som jag eder och edra fäder gifvit hafver; men I villen icke böja edor öron dertill, eller höra mig;
Kawirikawiri ndakhala ndikutumiza atumiki anga, aneneri, kwa inu. Iwo akhala akukuwuzani kuti, ‘Aliyense wa inu asiye ntchito zake zoyipa ndi kukonza makhalidwe ake; musatsatire milungu ina ndi kumayitumikira. Pamenepo mudzakhala mʼdziko limene ndinakupatsani ndi makolo anu.’ Komabe inu simunasamale zimenezi kapena kundimvera Ine.
16 Ändock Jonadabs barn, Rechabs sons, sins faders bud hållit hafva, som han dem budit hafver; men detta, folket hörer mig Intet.
Zidzukulu za Yehonadabu mwana wa Rekabu zakhala zikumvera lamulo limene kholo lawo anazilamula, koma inuyo simunandimvere Ine.
17 Derföre så säger Herren Gud Zebaoth, och Israels Gud: Si, jag skall låta komma öfver Juda, och alla Jerusalems inbyggare, all den olycko, som jag emot dem talat hafver; derföre, att jag hafver talat till dem, och de ville intet höra; jag hafver ropat, men de ville intet svara mig.
“Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndidzagwetsera pa Yuda ndi pa onse okhala mu Yerusalemu masautso onse amene ndinakonza chifukwa sanandimvere. Ndinawayitana koma iwo sanayankhe.’”
18 Och till de Rechabiters hus sade Jeremia: Detta säger Herren Zebaoth, Israels Gud; derföre att I edars faders Jonadabs bud lydt hafven, och hållit all hans bud, och allt det gjort, som han eder budit hafver;
Yeremiya anawuza banja la Arekabu mawu onse a Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, kuti, “Munamvera lamulo la kholo lanu Yehonadabu ndipo mwatsatira malangizo ake onse ndi kuchita chilichonse chimene anakulamulani.”
19 Derföre säger Herren Zebaoth, Israels Gud, alltså: Det skall aldrig fela Jonadab, Rechabs sone, att ju någor af hans säd alltid för mig stå skall.
Tsono Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Yehonadabu mwana wa Rekabu sadzasowa munthu wonditumikira Ine nthawi zonse.”

< Jeremia 35 >