< Jeremia 29 >

1 Detta äro de ord, i de brefvena, som Propheten Jeremia sände af Jerusalem, till de igenlefda äldsta som bortförde voro, och till Presterna, och Propheterna, och till allt folket, som NebucadNezar ifrå Jerusalem till Babel bortfört hade;
Yeremiya anatumiza kalata kuchokera ku Yerusalemu kupita kwa akuluakulu amene anali ku ukapolo, ndiponso kwa ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse amene Nebukadinezara anawatenga ku Yerusalemu kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
2 Sedan Konung Jechonia och Drottningen, med kamererarena, och Förstarna i Juda och Jerusalem, samt med timbermän och smeder i Jerusalem, borto voro;
Zimenezi zinachitika mfumu Yekoniya, amayi a mfumu, nduna za mfumu ndiponso atsogoleri a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu, anthu aluso ndi amisiri atatengedwa ku Yerusalemu kupita ku ukapolo.
3 Genom Elasa, Saphans son, och Gemaria, Hilkia son, hvilka Zedekia, Juda Konung, sände till Babel, till NebucadNezar, Konungen i Babel, och sade:
Yeremiya anapatsira kalatayo Eleasa mwana wa Safani ndi Gemariya mwana wa Hilikiya, amene Zedekiya mfumu ya Yuda anawatumiza kwa Mfumu Nebukadinezara ku Babuloni. Mʼkalatamo analembamo kuti:
4 Detta säger Herren Zebaoth, Israels Gud, till alla fångar, som jag hafver låtit bortföra ifrå Jerusalem till Babel:
Anthu onse amene anatengedwa ukapolo kuchokera ku Yerusalemu kupita ku Babuloni, Yehova akuwawuza kuti,
5 Bygger hus, der I uti bo kunnen; planterer trädgårdar, der I frukt af äta mågen.
“Mangani nyumba ndipo muzikhalamo. Limani minda ndipo mudye zipatso zake.
6 Tager eder hustrur, och föder söner och döttrar; gifver edra söner hustrur, och gifver edra döttrar män, att de måga föda söner och döttrar; föröker eder der, så att I icke ären få.
Kwatirani ndipo mubereke ana aamuna ndi aakazi. Ana anu aamuna muwasankhire akazi ndipo muwasankhire amuna ana anu aakaziwo, kuti nawonso abale ana aamuna ndi aakazi. Muchulukane kumeneko. Chiwerengero chanu chisachepe.
7 Söker stadsens bästa, dit jag hafver låtit bortföra eder, och beder för honom till Herran; ty då honom väl går, så går eder ock väl.
Ndiponso muzifunafuna mtendere ndi ubwino wa mzinda umene ndinakupirikitsirani ku ukapoloko. Muzipempherera mzindawo kwa Yehova, kuti zikuyendereni bwino.”
8 Ty detta, säger Herren Zebaoth, Israels Gud: Låter icke de Propheter, som när eder äro, och de spåmän bedraga eder, och sköter intet edra drömmar som I drömmen;
Inde, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, “Musalole kuti aneneri ndi owombeza amene ali pakati panu akunyengeni. Musamvere maloto awo.
9 Ty de spå eder lögn i mitt Namn; jag hafver intet sändt dem, säger Herren.
Iwo akunenera zabodza kwa inu mʼdzina langa ngakhale Ine sindinawatume,” akutero Yehova.
10 Ty så säger Herren; När i Babel sjutio år ute äro, så skall jag besöka eder, och skall uppväcka mitt nådeliga ord öfver eder, att jag skall låta eder komma till detta rum igen.
Yehova akuti, “Zaka 70 za ku Babuloni zikadzatha, ndidzabwera kudzakuchitirani zabwino zonse zimene ndinakulonjezani zija, ndipo ndidzakubwezerani ku malo ano.
11 Ty jag vet väl, hvad tankar jag hafver om eder, säger Herren, nämliga fridsens tankar, och icke bedröfvelsens, att jag skall gifva eder den ända, som I vänten efter.
Pakuti Ine ndikudziwa zimene ndinakukonzerani,” akutero Yehova, “ndimalingalira zabwino zokhazokha za inu osati zoyipa, ayi. Ndimalingalira zinthu zokupatsani chiyembekezo chenicheni pa za mʼtsogolo.
12 Och I skolen åkalla mig, och gå och bedja mig, och jag skall höra eder.
Nthawi imeneyo mudzandiyitana, ndi kunditama mopemba ndipo ndidzakumverani.
13 I skolen söka mig, och finna mig; ty om I mig af allt hjerta söken,
Mudzandifunafuna ndipo mudzandipeza. Mukadzandifuna ndi mtima wanu wonse
14 Så skall jag låta mig finna af eder, säger Herren; och jag skall vända edart fängelse, och församla eder utur all folk, och utaf all rum, dit jag eder utdrifvit hafver, säger Herren; och skall låta eder återkomma till detta rum igen, dädan jag eder hafver bortföra låtit.
mudzandipezadi,” akutero Yehova, “ndipo ndidzakubwezerani zabwino zanu. Ndidzakusonkhanitsani kuchokera ku mayiko onse ndi kumalo konse kumene munali,” akutero Yehova, “ndipo ndidzakubweretsani kumalo kumene munali ndisanakuchotseni kukupititsani ku ukapolo.”
15 Ty I menen, att Herren hafver uppväckt eder Propheter i Babel.
Inu mumati, “Yehova watiwutsira aneneri athu ku Babuloni,”
16 Ty detta säger Herren om Konungen, som på Davids stol sitter, och om allt folket, som i denna stadenom bor, nämliga om edra bröder, som med eder uti fängelset icke utdragne äro;
koma zimene Yehova akunena za mfumu imene ikukhala pa mpando waufumu wa Davide pamodzi ndi anthu onse amene anatsala mu mzinda muno, abale anu amene sanapite nanu ku ukapolo ndi izi,
17 Ja, så säger Herren Zebaoth: Si, jag skall sända ibland dem svärd, hunger och pestilentie, och skall så ställa mig med dem, lika som med de onda fikon, de man vämjar vid att äta;
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndidzawapha ndi nkhondo, njala ndi mliri ndipo ndidzawasandutsa ngati nkhuyu zowola kwambiri, zosati nʼkudya.
18 Och skall förfölja dem med svärd, hunger och pestilentie, och skall icke låta dem blifva, uti något rike på jordene, så att de skola varda till bannor, till under, till hån och spott, ibland all folk, dit jag dem utdrifvandes varder;
Ndidzawalondola ndi lupanga, njala ndi mliri ndipo ndidzawasandutsa chinthu chonyansa kwa anthu amayiko onse a pa dziko lapansi. Adzakhala otembereredwa, ochititsa mantha, onyozeka ndiponso ochitidwa chipongwe pakati pa anthu a mitundu yonse kumene ndawapirikitsirako.
19 Derföre, att de icke hafva hört min ord, säger Herren, de jag städse med mina tjenare Propheterna till eder sändt hafver; men I villen intet höra, säger Herren.
Zidzatero chifukwa sanamvere mawu anga amene ndinkawatumizira kudzera mwa atumiki anga, aneneri. Ngakhale inu amene muli ku ukapolo simunamverenso,” akutero Yehova.
20 Men I alle, som fångne bortförde ären, de jag hafver ifrå Jerusalem till Babel draga låtit, hörer Herrans ord.
Choncho, imvani mawu a Yehova, inu akapolo nonse amene ndinakuchotsani mu Yerusalemu ndi kukupititsani ku Babuloni.
21 Detta säger Herren Zebaoth, Israels Gud, emot Achab, Kolaja son, och emot Zedekia, Maaseja son, hvilke eder lögn spå i mitt Namn: Si, jag skall gifva dem uti NebucadNezars händer, Konungens i Babel; han skall låta slå dem för edor ögon;
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti zokhudza Ahabu mwana wa Kolaya ndi Zedekiya mwana wa Maseya, amene akulosera zabodza kwa inu mʼdzina langa: “Taonani ndidzawapereka kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo adzawapha inu mukupenya.
22 Så att man skall göra bannor af dem ibland alla fångar af Juda, som i Babel äro, och säga: Herren göre dig lika som Zedekia och Achab, hvilka Konungen af Babel på eld steka lät;
Chifukwa cha anthu awiriwo, akapolo onse ochokera ku Yuda amene ali ku Babuloni adzagwiritsa ntchito mawu awa potemberera: ‘Yehova achite nawe monga mmene anachitira ndi Zedekiya ndi Ahabu, amene mfumu ya ku Babuloni inawatentha.’
23 Derföre att de bedrefvo en galenskap i Israel, och bedrefvo hor med annars mans hustrur, och predikade lögn i mitt Namn, det jag dem intet befallt hade. Detta vet jag, och betygar det, säger Herren.
Pakuti anthu amenewa achita zoyipa kwambiri mu Israeli; achita chigololo ndi akazi a eni ake ndipo mʼdzina langa ankayankhula zabodza zimene sindinawawuze kuti atero. Ine ndikuzidziwa ndipo ndine mboni ya zimenezi,” akutero Yehova.
24 Och emot Semaja af Nehelam skall du säga:
Ukamuwuze Semaya wa ku Nehelamu kuti,
25 Detta säger Herren Zebaoth, Israels Gud; derföre, att du under ditt namn hafver bref sändt till allt folket, som i Jerusalem är, och till Presten Zephanja, Maaseja son, och till alla Presterna, och sagt:
“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Iwe unatumiza kalata mʼdzina lako kwa anthu onse a mu Yerusalemu, kwa Zefaniya mwana wa wansembe Maseya, ndi kwa ansembe onse. Unalemba mu kalatayo kuti,
26 Herren hafver satt dig till en Prest uti Prestens Jehojada stad, att I skolen tillsiare vara uti Herrans hus öfver alla ursinniga och spåmän, att du skall sätta dem i fångahus och i stock;
‘Yehova wakusankha kukhala wansembe mʼmalo mwa Yehoyada kuti ukhale wamkulu woyangʼanira Nyumba ya Yehova. Munthu aliyense wamisala amene akudziyesa kuti ndi mneneri uzimuponya mʼndende ndi kumuveka goli lachitsulo.
27 Och nu, hvi straffar du då icke Jeremia af Anathoth, den eder propheterar?
Nanga tsono chifukwa chiyani simunamuchitire zimenezi Yeremiya wa ku Anatoti, amene amakhala ngati mneneri pakati panu?
28 Derföre, att han till oss i Babel sändt hafver, och låtit säga: Det skall ännu länge vara; bygger hus, der I uti bon, och planterer trägårdar, att I äten der frukt af.
Yeremiyayo watitumizira uthenga uwu kuno ku Babuloni: Ukapolo wanu ukhala wa nthawi yayitali. Choncho mangani nyumba ndipo muzikhalamo; limani minda ndipo mudye zipatso zake.’”
29 Och Zephanja Presten hade läsit det samma brefvet, och låtit Jeremia Propheten höra det.
Koma wansembe Zefaniya anayiwerenga kalatayo pamaso pa mneneri Yeremiya.
30 Derföre skedde Herrans ord till Jeremia, och sade:
Ndipo Yehova anawuza Yeremiya kuti,
31 Sänd bort till alla fångarna, och låt säga dem: Detta säger Herren emot Semaja af Nehelam: Derföre, att Semaja propheterar eder, och jag hafver dock intet sändt honom, och hafver gjort, att I förlåten eder uppå lögn;
“Tumiza uthenga uwu kwa akapolo onse: ‘Yehova akuti zokhudza Semaya wa ku Nehelamu: Semaya wakuloserani, ngakhale kuti Ine sindinamutume, ndipo wakunyengani kuti muzikhulupirira bodza.
32 Derföre säger Herren alltså: Si, jag skall hemsöka Semaja af Nehelam, samt med hans säd, så att ingen af hans skall blifva ibland detta folket, och skall icke se det goda, som jag desso mino folke göra vill, säger Herren; ty han hafver med sitt tal afvändt dem ifrå Herranom.
Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti: Mʼbanja lakelo sipadzakhala munthu pakati pa mtundu uno wa anthu amene adzaone zinthu zabwino zimene ndidzachitira anthu anga chifukwa analalika zondiwukira,’” akutero Yehova.

< Jeremia 29 >