< Jeremia 23 >

1 Ve eder, herdar, I som förderfven och förskingren min fosterhjord, säger Herren.
“Tsoka kwa abusa amene akuwononga ndi kubalalitsa nkhosa za pabusa panga!” akutero Yehova.
2 Derföre säger Herren, Israels Gud, om de herdar, som mitt folk regera: I hafven förskingrat min hjord, och bortdrifvit, och icke besökt honom; si, jag skall hemsöka eder, för edart onda väsendes skull, säger Herren.
Nʼchifukwa chake Yehova, Mulungu wa Israeli, ponena za abusa amene akuweta anthu anga akuti, “Mwabalalitsa ndi kumwaza nkhosa zanga. Komanso simunazisamale bwino. Choncho ndidzakulangani chifukwa cha machimo anu,” akutero Yehova.
3 Och jag skall församla, det qvart är af minom hjord, utur all land, dit jag dem utdrifvit hafver, och skall hafva dem hem igen till deras hus, att de skola växa och förökas.
“Pambuyo pake Ine mwini wakene ndidzasonkhanitsa nkhosa zanga zotsala, kuzichotsa ku mayiko onse kumene ndinazibalalitsira ndi kuzibweretsanso ku msipu wawo. Kumeneko zidzaswana ndi kuchulukana.
4 Och jag skall sätta herdar öfver dem, som dem sköta skola, att de icke mer skola frukta sig eller förskräckas, eller hemsökte varda, säger Herren.
Ndidzazipatsa abusa amene adzaziweta, ndipo sizidzaopanso kapena kuchita mantha, ndipo palibe imene idzasochera,” akutero Yehova.
5 Si, den tiden kommer, säger Herren, att jag skall uppväcka David rättfärdighetenes frukt; och det skall vara en Konung, den väl regera skall, och skall upprätta rätt och rättfärdighet på jordene.
Yehova akuti, “Masiku akubwera, pamene ndidzaphukitsira Davide Nthambi yowongoka. Imeneyi ndiye mfumu imene idzalamulira mwanzeru, mwachilungamo ndi mosakondera mʼdziko.
6 På den tiden skall Juda hulpen varda, och Israel säker bo; och detta skall vara hans namn, det man honom kalla skall: Herren vår rättfärdighet.
Pa masiku a ulamuliro wake Yuda adzapulumuka ndipo Israeli adzakhala pamtendere. Dzina limene adzamutcha ndi ili: Yehova ndiye Chilungamo Chathu.
7 Derföre, si, den tid skall komma, säger Herren, då man nu intet mer skall säga: Så sant som Herren lefver, som Israels barn utur Egypti land fört hafver;
Choncho, masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene anthu sadzanenanso polumbira kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli ku Igupto,’
8 Utan: Så sant som Herren lefver, som Israels hus säd utförde, och hade af nordlanden, och utur all land, dit jag dem fördrifvit hafver, så att de skola nu bo i sitt land.
koma adzanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa zidzukulu za Israeli ku dziko lakumpoto ndi ku mayiko konse kumene anawabalalitsira.’ Ndipo iwo adzawabweretsa ku dziko lawolawo.”
9 Emot Propheterna: Mitt hjerta vill mig brista i mino lifve, all min ben darra; mig är lika som enom drucknom manne, och lika som enom den af vin ragar, för Herranom, och för hans heliga ordom;
Kunena za aneneri awa: Mtima wanga wasweka; mʼnkhongono mwati zii. Ndakhala ngati munthu woledzera, ngati munthu amene wasokonezeka ndi vinyo, chifukwa cha Yehova ndi mawu ake opatulika.
10 Att landet så fullt med horkarlar är, att landet så jämmerliga står, att det så förbannadt är, och ängarna i öknene förtorkas; och deras lefverne är ondt, och deras regemente doger intet.
Dziko ladzaza ndi anthu achigololo; lili pansi pa matemberero. Dziko lasanduka chipululu ndipo msipu wawuma. Aneneri akuchita zoyipa ndipo akugwiritsa ntchito mphamvu zawo molakwika.
11 Ty både Propheter och Prester äro skalkar; och jag finner också deras ondska i mino huse, säger Herren.
“Mneneri ngakhale wansembe onse sapembedza Yehova. Amachita zoyipa ngakhale mʼnyumba yanga,” akutero Yehova.
12 Derföre är deras väg lika som en slipper väg i mörkrena, der de uppå falla; ty Jag skall låta komma olycko öfver dem, deras hemsökningsår, säger Herren.
“Nʼchifukwa chake njira zawo zidzakhala zoterera; adzawapirikitsira ku mdima ndipo adzagwera kumeneko. Adzaona zosaona mʼnthawi ya chilango chawo,” akutero Yehova.
13 Med de Propheter i Samarien hafver jag sett galenskap, att de propheterade i Baal och förförde mitt folk Israel;
“Pakati pa aneneri a ku Samariya ndinaona chonyansa ichi: Ankanenera mʼdzina la Baala ndipo anasocheretsa anthu anga, Aisraeli.
14 Men med de Propheter i Jerusalem ser jag en styggelse; huru de bedrifva hor, och fara med lögn, och styrka de onda, på det att ju ingen skall omvända sig af sine ondsko. De äro alle för mig lika som Sodoma, och dess inbyggare lika som Gomorra.
Ndipo pakati pa aneneri a ku Yerusalemu ndaonapo chinthu choopsa kwambiri: amachita chigololo, amanena bodza ndipo amalimbitsa mtima anthu ochita zoyipa. Choncho palibe amene amasiya zoyipa zake. Kwa Ine anthu onsewa ali ngati a ku Sodomu ndi Gomora.”
15 Derföre säger Herren Zebaoth om Propheterna alltså: Si, jag skall spisa dem med malört, och gifva dem galla dricka; ty ifrå Propheterna i Jerusalem kommer ut skrymteri öfver hela landet.
Choncho ponena za aneneriwa Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndidzawadyetsa zakudya zowawa ndi kuwamwetsa madzi a ndulu, chifukwa uchimo umene wafalikira mʼdziko lonse ndi wochokera kwa aneneri a ku Yerusalemuwa.”
16 Detta säger Herren Zebaoth: Hörer intet Propheternas ord, de eder prophetera; de bedraga eder, ty de predika sins hjertas syner, och icke utaf Herrans mun.
Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Musamvere zimene aneneri amenewa akulosera kwa inu; zomwe aloserazo nʼzachabechabe. Iwo akungoyankhula za masomphenya a mʼmitima mwawo basi, osati zochokera kwa Yehova.
17 De säga dem som mig försmäda: Herren hafver det sagt: Eder varder väl gångandes; och allom dem som vandra efter sins hjertas tycko, säga de: Det kommer ingen olycka öfver eder.
Iwo amapita ndi kumakawuza amene amandinyoza Ine kuti, ‘zinthu zidzakuyenderani bwino.’ Kwa iwo amene amawumirira kutsata zofuna za mitima yawo amakawawuza kuti, ‘palibe choyipa chimene chidzakugwereni.’”
18 Ty ho hafver varit i Herrans råd, den hans ord sett och hört hafver? Ho hafver förmärkt och hört hans ord?
Ine ndikuti, “Koma ndani wa iwo amene anakhalapo mu msonkhano wa Yehova? Ndani anaonapo kapena kumvapo mawu ake? Ndani mwa iwo analabadirako za mawu ake ndi kuwamvera?
19 Si, ett Herrans väder skall komma med grymhet, och ett förskräckeligit oväder falla de ogudaktiga öfver hufvudet.
Taonani ukali wa Yehova uli ngati chimphepo chamkuntho, inde ngati namondwe. Ndipo adzakantha mitu ya anthu oyipa.
20 Och Herrans vrede skall icke upphålla, tilldess han gör och uträttar det han i sinnet hafver. Härefter skolen I väl förvarat.
Mkwiyo wa Yehova sudzaleka mpaka atachita zonse zimene anatsimikiza mu mtima mwake. Mudzazizindikira bwino zimenezi masiku akubwerawa.”
21 Jag sände intet Propheterna, likväl lupo de; jag talade intet med dem, likväl propheterade de.
Yehova anati, “Ine sindinatume aneneri amenewa, komabe iwo athamanga uku ndi uku kulalikira uthenga wawo; Ine sindinawayankhule, komabe iwo ananenera.
22 Ty om de hade blifvit vid mitt råd och hade predikat mino folke min ord, så hade de omvändt dem ifrå deras onda väsende, och ifrå deras onda lefverne.
Iwo akanakhala pa msonkhano wanga ndiye kuti akanamayankhula mawu anga kwa anthu anga. Komanso bwenzi atawachotsa anthu anga mʼnjira zawo zoyipa kuti aleke machimo awo.”
23 Är jag icke en Gud, den hardt när är, säger Herren, och icke en Gud, den fjerran är?
Yehova akuti, “Kodi ndimakhala Mulungu pokhapokha ndikakhala pafupi, ndiye sindine Mulungu?
24 Menar du, att någor kan så hemliga fördölja sig, att jag icke kan se honom? säger Herren. Är icke jag den som uppfyller himmel och jord? säger Herren.
Kodi wina angathe kubisala Ine osamuona?” “Kodi Ine sindili ponseponse kumwamba ndi dziko lapansi?” Akutero Yehova.
25 Jag hörer väl, att Propheterna predika, och prophetera lögn i mitt Namn, och säga: Mig hafver drömt, mig hafver drömt.
“Ndamva zimene aneneri akuyankhula. Iwo amalosera zabodza mʼdzina langa nʼkumati, ‘Ndalota! Ndalota!’
26 När vilja nu Propheterna igenvända? de der lögn prophetera, och prophetera sins hjertas bedrägeri;
Kodi zabodzazi zidzakhalabe mʼmitima ya aneneriwa mpaka liti? Iwotu amalosera zonyenga za mʼmitima yawo.
27 Och vilja, att mitt folk skall förgäta mitt Namn, för deras drömmars skull, som den ene för den andra predikar, såsom deras fäder förgåto mitt Namn för Baals skull.
Aneneriwa amakhulupirira kuti anthu anga adzayiwala mawu anga akamamva za maloto awo amene amayankhulana ngati mmene anachitira makolo awo popembedza Baala.
28 En Prophet, som drömmar hafver, han predike drömmar; men den som mitt ord hafver, han predike mitt ord rätt. Huru när kommer agnar och hvete tillhopa? säger Herren.
Mneneri amene ali ndi maloto afotokoze malotowo. Koma iye amene ali ndi mawu anga alalikire mawuwo mokhulupirika. Kodi phesi lingafanane ndi chimanga?
29 Är icke mitt ord lika som en eld, säger Herren, och såsom en hammar, den berg sönderslår?
Kodi suja mawu anga amatentha ngati moto? Suja mawu anga amaphwanya monga ichitira nyundo kuphwanya miyala?” Akutero Yehova.
30 Derföre, si: Jag vill till de Propheter, säger Herren, som min ord stjäla den ene dem andra.
Yehova akuti, “Nʼchifukwa chake, Ine ndikudana nawo aneneri amene amaberana okhaokha mawu nʼkumati mawuwo ndi a Yehova.”
31 Si, jag vill till de Propheter, säger Herren, som sitt eget ord föra, och säga: Han hafver det sagt.
Yehova akuti, “Inde, Ine ndikudana ndi aneneri amene amakonda kuyankhula zabodza nʼkumanena kuti, ‘Amenewa ndi mawu a Yehova.’”
32 Si, jag vill till de som falska drömmar prophetera, säger Herren, och predika dem, och förföra mitt folk med sine lögn och lösaktig ting; efter jag dock intet hafver sändt dem, och intet befallt dem, och de ej heller desso folkena nyttige äro, säger Herren.
Yehova akuti, “Ndithudi, Ine ndikudana ndi aneneri a maloto abodzawa. Iwo amafotokoza malotowo nʼkumasocheretsa anthu anga ndi bodza lawo losachita nalo manyazilo, chonsecho Ine sindinawatume kapena kuwalamula. Iwo sathandiza anthuwa ndi pangʼono pomwe,” akutero Yehova.
33 Om detta folk, eller en Prophet, eller en Prest varder dig frågandes, och säger: Hvilket är Herrans tunge? så skall du säga till dem, hvad den tungen är: Jag skall bortkasta eder, säger Herren.
Yehova anawuza Yeremiya kuti, “Anthu awa, kapena mneneri, kapenanso wansembe, akakufunsa kuti, ‘Kodi uthenga wolemetsa wa Yehova ukuti chiyani?’ uwawuze kuti, ‘Inuyo ndinu katundu wolemetsa Yehova, ndipo adzakutayani.’
34 Och om en Prophet, eller Prest, eller folk varder sägandes: Det är Herrans tunge; densamma skall jag hemsöka, och hans hus dertill.
Ngati mneneri kapena wansembe kapenanso munthu wina aliyense anena kuti, ‘Uthenga wolemetsa wa Yehova ndi uwu,’ Ine ndidzalanga munthu ameneyo pamodzi ndi banja lake.
35 Men så skall den ene tala med dem andra, och säga sig emellan: Hvad svarar Herren? Och hvad säger Herren?
Koma chimene aliyense wa inu azifunsa kwa mnzake kapena mʼbale wake ndi ichi: ‘Kodi Yehova wayankha chiyani?’ kapena ‘Yehova wayankhula chiyani?’
36 Och kaller det icke mer Herrans tunga; ty hvarjom och enom skall hans egen ord vara till en tunga, efter I alltså lefvandes Guds, Herrans Zebaoths, vårs Guds ord förvänden.
Koma musanenenso kuti ‘nawu uthenga wolemetsa wa Yehova,’ chifukwa mawu a munthu aliyense ndiwo uthenga wa iye mwini, kotero kuti inu mumakhotetsa mawu a Mulungu wamoyo, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wathu.
37 Derföre skolen I säga till Propheten alltså: Hvad svarar Herren dig? Och hvad säger Herren?
Tsono iwe Yeremiya udzamufunse mneneri kuti, ‘Kodi Yehova wakuyankha chiyani?’ kapena, ‘Kodi Yehova wayankhula chiyani?’
38 Nu medan I sägen Herrans tunge, derföre säger Herren alltså: Efter I kallen ordet Herrans tunga, och jag till eder sändt hafver, och hafver säga låtit, att I icke skullen kallat Herrans tunga;
Ngati mudzanena kuti, ‘Nawu uthenga wolemetsa wa Yehova,’ ndiye tsono Yehova akuti, ‘Popeza mwagwiritsa ntchito mawu akuti: Nawu uthenga wolemetsa wa Yehova, mawu amene ndinakuletsani kuti musawatchule,
39 Si, så skall jag taga eder bort, och bortkasta eder samt med stadenom, som jag eder och edra fäder gifvit hafver, ifrå mitt ansigte;
ndiye kuti Ine ndidzakunyamulani ngati katundu nʼkukuponyani kutali. Ndidzakuchotsani pamaso panga, inuyo pamodzi ndi mzinda umene ndinakupatsani inu ndi makolo anu.
40 Och skall foga eder en evig skam till, och en evig försmädelse, den aldrig förgäten skall varda.
Ndidzakunyozani mpaka muyaya. Ndidzakuchititsani manyazi osayiwalika.’”

< Jeremia 23 >