< Jeremia 14 >

1 Detta är det ord, som Herren till Jeremia sade, om den dyra tiden:
Awa ndi mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya onena za chilala:
2 Juda ligger jämmerliga, hans portar stå i en ömkelig måtto; det står klageliga till i landena, och i Jerusalem är ett stort rop.
“Yuda akulira, mizinda yake ikuvutika; anthu ake adzigwetsa pansi mwachisoni, kulira kwa Yerusalemu kwakula.
3 De store sända de små efter vatten; men då de komma till brunnen, så finna de intet vatten, och bära sina käril tom hem igen; de gå sorgse och bedröfvade, och omsvepa sin hufvud;
Anthu awo wolemekezeka akutuma antchito awo kuti akatunge madzi. Apita ku zitsime osapezako madzi. Choncho amabwerera ndi mitsuko yopanda madzi. Amanyazi ndi othedwa nzeru adziphimba kumaso.
4 Derföre, att jorden refnar, efter intet regnar på jordena; åkermännerna, gå sorgse, och omsvepa sin hufvud.
Popeza pansi pawumiratu chifukwa kulibe madzi, alimi ali ndi manyazi ndipo amphimba nkhope zawo.
5 Ty ock hinderna, som på markena kalfva, öfvergifva sina kalfvar, efter intet gräs växer.
Ngakhale mbawala yayikazi ikusiya mwana wake wakhanda ku thengo chifukwa kulibe msipu.
6 Vildåsnarna stå på bergen, och lukta efter vädret, lika som drakar, och försmäkta, efter ingen ört växer.
Mbidzi zikuyima pa zitunda zopanda kanthu nʼkumapuma wefuwefu ngati nkhandwe; maso awo achita chidima chifukwa chosowa msipu.”
7 Ack! Herre, våra missgerningar hafva det ju förtjent; men hjelp dock för ditt Namns skull; ty vår ohörighet är stor, der vi emot dig med syndat hafve.
Anthu akuti, “Ngakhale machimo athu akutitsutsa, koma Inu Yehova chitanipo kanthu chifukwa cha dzina lanu. Pakuti kusakhulupirika kwathu nʼkwakukulu; ife takuchimwirani.
8 Du äst Israels tröst, och hans nödhjelpare; hvi skickar du dig, lika som du vore främmande i landena, och såsom en gäst, den icke mer än ena natt derinne ligger?
Inu Yehova amene Aisraeli amakukhulupirirani ndi amene mumawapulumutsa pa nthawi ya masautso, chifukwa chiyani mukukhala ngati mlendo mʼdziko muno? Chifukwa chiyani muli ngati wapaulendo amene akungogona tsiku limodzi?
9 Hvi hafver du dig såsom en hjelte, som förtviflad är; och som en kämpe, den intet hjelpa kan? Du äst ju dock ibland oss, Herre, och vi nämnes efter ditt Namn; öfvergif oss icke.
Chifukwa chiyani muli ngati munthu amene wadzidzimutsidwa, kapena ngati wankhondo amene alibe mphamvu yopulumutsa? Komabe Inu Yehova, muli pakati pathu, ndipo tikudziwika ndi dzina lanu; musatitaye ife!”
10 Så säger Herren om detta folket: De löpa gerna hit och dit, och blifva icke gerna hemma; derföre hafver Herren ingen vilja till dem; utan han tänker nu uppå deras missgerningar, och vill hemsöka deras synder.
Zimene Yehova akunena za anthuwa ndi izi: “Iwo amakonda kuyendayenda kwambiri; samatha kudziretsa. Nʼchifukwa chake Ine Yehova sindingawalandire, ndipo tsopano ndidzakumbukira zoyipa zawo ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo.”
11 Och Herren sade till mig: Du skall intet bedja för detta folk om nåde.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Usawapempherere anthu awa kuti zinthu ziwayendere bwino.
12 Ty om de än fastade, så vill jag dock intet höra deras bön; och om de än hade bränneoffer och spisoffer fram, så behaga de mig dock intet; utan jag vill göra en ända uppå dem med svärd, hunger och pestilentie.
Ngakhale asale zakudya, Ine sindidzamva kulira kwawo; ngakhale apereke nsembe zopsereza ndi chopereka cha chakudya, sindidzazilandira. Mʼmalo mwake, ndidzawapha ndi lupanga, njala ndi mliri.”
13 Då sade jag: Ack Herre Herre! Si, Propheterna säga dem: I skolen intet svärd se, och ingen dyr tid få när eder; men jag skall gifva eder en god frid i detta rummet.
Koma ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova, aneneri amawawuza anthuwo kuti, sadzaphedwa ndi lupanga kapena kuvutika ndi njala. Koma kuti Inu mudzawapatsa mtendere wokhawokha pamalo pano.”
14 Och Herren sade till mig: Propheterna, spå lögn i mitt Namn; jag hafver intet sändt dem, och intet befallt dem, och intet talat med dem; de predika eder falska syner, spådom, afguderi, och sins hjertans bedrägeri.
Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Ndi zabodza kuti aneneriwa akunenera mʼdzina langa. Ine sindinawatume kapena kuwasankha kapenanso kuyankhula nawo. Iwo amakuwuzani zinthu zabodza zomwe amati anaziona mʼmasomphenya, kapena pogwiritsa ntchito mawula achabechabe. Zimene amayankhula ndi zongopeka mʼmutu mwawo.
15 Derföre säger Herren om de Propheter, som i mitt Namn prophetera, ändock jag dem intet sändt hafver, och de likväl predika, att intet svärd eller dyr tid skall komma i detta land: Sådana Propheter skola dö genom svärd och hunger.
Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti aneneri amenewa akulosera mʼdzina langa pamene Ine sindinawatume. Iwo amati simudzafa pa nkhondo kapena ndi njala mʼdziko muno. Koma tsono ndi iwowo, aneneriwa amene adzafe pa nkhondo kapena ndi njala.
16 Och folket, hvilko de prophetera, skola af svärd och hunger ligga här och der på gatomen i Jerusalem, att ingen skall begrafva dem; sammalunda ock deras hustrur, söner och döttrar; och jag skall gjuta deras ondsko uppå dem.
Ndipo anthu amene anawaloserawo adzaponyedwa mʼmisewu ya mu Yerusalemu atafa ndi njala ndi lupanga. Sipadzapezeka wowayika mʼmanda popeza iwowo, akazi awo, ana awo aamuna, onse adzakhala atafa. Ine ndidzawagwetsera chilango chowayenera.
17 Och du skall säga till dem detta ordet: Min ögon flyta med tårar dag och natt, och vända intet åter; ty jungfrun, mins folks dotter, är grufveliga plågad, och jämmerliga slagen.
“Awuze mawu awa: “‘Maso anga akugwetsa misozi kosalekeza usana ndi usiku; chifukwa anthu anga okondedwa apwetekeka kwambiri, akanthidwa kwambiri.
18 Går jag ut på markena, si, så ligga der de slagne med svärd; kommer jag in uti staden, så ligga der de försmäktade af hunger; ty ock Propheterna och Presterna måste bortdraga uti ett land, det de intet känna.
Ndikapita kuthengo, ndikuona amene aphedwa ndi lupanga; ndikapita mu mzinda, ndikuona amene asakazidwa ndi njala. Ngakhale aneneri pamodzi ndi ansembe onse atengedwa.’”
19 Hafver du då förkastat Juda? Eller hafver din själ en vämjelse till Zion? Hvi hafver du så slagit oss, att oss ingen hela kan? Vi hoppades, att det skulle frid varda, men här kommer intet godt; vi hoppades, att vi skulle helade varda, och si, här är nu mera vedermöda.
Kodi anthu a ku Yuda mwawakana kwathunthu? Kodi mtima wanu wanyansidwa nawo anthu a ku Ziyoni? Chifukwa chiyani mwatikantha chotere kuti sitingathenso kuchira? Ife tinayembekezera mtendere koma palibe chabwino chomwe chabwera, tinayembekezera kuchira koma panali kuopsezedwa kokhakokha.
20 Herre, vi kännom vårt ogudaktiga väsende, och våra fäders missgerningar; ty vi hafve syndat emot dig.
Inu Yehova, ife tikuvomereza kuyipa kwathu ndiponso kulakwa kwa makolo athu; ndithu ife tinakuchimwiranidi.
21 Men, för ditt Namns skull, låt oss icke skämde varda; låt dine härlighets säte icke begabbadt varda; kom dock ihåg, och låt icke ditt förbund med oss återvända.
Musatikane kuopa kuti dzina lanu linganyozedwe; musanyoze mpando wanu waufumu waulemerero. Kumbukirani pangano lanu ndi ife ndipo musachiphwanye.
22 Det är dock ingen ibland Hedningarnas afgudar, som regn gifva kan; himmelen kan ock icke regna. Du äst ju Herren vår Gud, uppå hvilken vi hoppas; ty du kan alltsammans detta göra.
Mwa milungu yachabechabe ya anthu a mitundu ina, kodi pali mulungu amene angagwetse mvula? Ife chikhulupiriro chathu chili pa Inu, popeza Inu nokha ndinu Yehova Mulungu wathu amene mukhoza kuchita zimenezi.

< Jeremia 14 >