< Jeremia 10 >

1 Hörer hvad Herren säger till eder, I af Israels hus.
Inu Aisraeli, imvani zimene Yehova akunena.
2 Detta säger Herren: I skolen icke lära Hedningarnas sätt, och skolen intet frukta eder för himmelens tecken, såsom Hedningarna frukta.
Yehova akuti, “Musatsatire makhalidwe a anthu a mitundu ina kapena kuchita mantha ndi zizindikiro zamlengalenga, ngakhale anthu a mitundu ina amachita nazo mantha.
3 Ty Hedningarnas gudar äro icke utan fåfängelighet; de hugga ett trä i skogenom, och mästaren gör det till med en yxa;
Pakuti miyambo ya mitundu inayo ndiyachabechabe. Iwo amakadula mtengo ku nkhalango ndipo mmisiri amawusema ndi sompho.
4 Och pryder det med silf och guld, och fäster det vid, med naglar och hamrar, att det icke omkullfalla skall.
Amakongoletsa chosemacho ndi siliva ndi golide; kenaka amachikhomerera ndi misomali kuti chisagwedezeke.
5 Sådant är nu intet annat, än öfverdragna stodar; de kunna intet tala; så måste man ock bära dem; ty de kunna intet gå. Derföre skolen I intet frukta eder för dem; förty de kunna hvarken hjelpa eller stjelpa.
Mafano awo ali ngati mtengo wakanjedza woopsezera mbalame mʼmunda wa minkhaka. Mafanowo sangathe nʼkuyankhula komwe ndipo ayenera kunyamulidwa popeza sangathe nʼkuyenda komwe. Musachite nawo mantha popeza sangathe kukuchitani choyipa ndiponso alibe mphamvu yochitira chabwino chilichonse.”
6 Men dig, Herre, är ingen lik; du äst stor, och ditt Namn är stort, och du kan det bevisa med gerningarna.
Palibe wofanana nanu, Inu Yehova; Inu ndinu wamkulu, ndipo dzina lanu lili ndi mphamvu yayikulu.
7 Ho skulle icke frukta dig, du Hedningarnas Konung? Dig skall man ju lyda; ty ibland alla Hedningarnas visa, och i all Konungarike, är ingen din like.
Ndani amene angaleke kukuopani, inu Mfumu ya mitundu ya anthu? Chimenechi ndicho chokuyenerani. Pakati pa anthu anzeru onse komanso mafumu onse a mitundu ya anthu, palibe wina wofanana nanu.
8 De äro allesamman dårar och galne; ty ett trä måste ju vara en platt fåfäng Gudstjenst.
Onsewo ndi opusa ndi opanda nzeru; malangizo awo amawatenga kuchokera kwa mafano achabechabe opanga ndi mitengo.
9 Silfskifvor förer man till på hafvet; guld ifrån Uphas, af mästare och guldsmeder beredt; gult silke och purpur kläder man uppå dem, och äro alltsammans slöga, mäns verk.
Siliva wosula amabwera naye kuchokera ku Tarisisi ndipo golide amachokera naye ku Ufazi. Mafanowo ndi ntchito ya anthu aluso ndi odziwa kuzokota golide. Tsono mafanowo amawaveka zovala za mtundu wamtambo ndi pepo. Yonseyo ndi ntchito ya anthu a luso.
10 Men Herren är en rätt Gud, en lefvandes Gud, en evig Konung; för hans vrede bäfvar jorden, och Hedningarna kunna icke fördraga hans trug.
Koma Yehova ndiye Mulungu woona; Iyeyo ndiye Mulungu wamoyo, Mfumu yamuyaya. Akakwiya, dziko limagwedezeka; anthu a mitundu ina sangathe kupirira ukali wakewo.
11 Så säger nu alltså till dem: De gudar, som himmel och jord icke gjort hafva, förgånge af jorden, och under himmelen.
“Awuze anthu awa kuti, ‘Milungu iyi, imene sinalenge dziko lakumwamba ndi dziko lapansi, idzawonongeka pa dziko lapansi ndi pansi pa thambo.’”
12 Men han hafver gjort jordena genom sina kraft, och verldenes krets beredt genom sina vishet; och utsträckt himmelen genom sitt förstånd.
Koma Mulungu analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake; Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake ndipo anayala thambo mwaluso lake.
13 Då han dundrar, så är mycket vatten under himmelen, och drager upp dimbona ifrå jordenes anda; han gör ljungelden i regnet, och låter vädret kommer ifrå hemlig rum.
Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba; Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene osungirako.
14 Alla menniskor äro dårar med sine konst, och alle guldsmeder stå med skam med sin beläte; ty deras beläte äro bedrägeri, och hafva intet lif.
Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru; mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake. Mafano akewo ndi abodza; alibe moyo mʼkati mwawo.
15 Det är alltsammans ett fåfängt och bedrägeligit verk; de måste förgås, då de hemsökte varda.
Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo. Pamene anthuwo azidzaweruzidwa, mafanowo adzawonongedwa.
16 Men sådan är icke han, som Jacobs lott är; utan han är den som all ting skapat hafver, och Israel är hans arfvedel; han heter Herren Zebaoth.
Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo. Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse kuphatikizapo Israeli, mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
17 Tag din handel bort utu landena, du som bor i den fasta ( staden ).
Sonkhanitsani katundu wanu, inu amene mukukhala mʼlinga la ankhondo.
18 Ty så säger Herren: Si, jag skall i denna resone bortslunga landsens inbyggare, och så plåga dem, att de det känna skola.
Pakuti Yehova akuti, “Tsopano Ine ndidzachotsa anthu onse amene akukhala mʼdziko lino; adzakhala pa mavuto mpaka adzamvetsa.”
19 Ack! min jämmer och hjertans sorg; men jag tänker, att det är min plåga; jag måste lida henne.
Aliyense ankangoti, “Mayo ine, chifukwa cha kupweteka kwanga! Chilonda changa nʼchachikulu!” Koma ine ndinkaganiza kuti, “Ndithu, ili ndi vuto langa basi, choncho ndingolipirira.”
20 Mitt tjäll är förstördt, och all min tåg äro sönder; min barn äro borto, och icke mer för handene; ingen upprättar min hyddo igen, och mitt tjäll slår ingen upp igen.
Tenti yanga yawonongeka, zingwe zake zonse zaduka. Ana anga andisiya ndipo kulibenso. Palibenso amene adzandimangire tenti, kapena kufunyulula nsalu yake.
21 Ty herdarna äro till dårar vordne, och fråga intet efter Herran; derföre kunna de ock intet rätt lära, utan förskingra hjorden.
Abusa ndi opusa ndipo sanapemphe nzeru kwa Yehova; choncho palibe chimene anapindula ndipo nkhosa zawo zonse zabalalika.
22 Si, ett rykte kommer, och ett stort bäfvande af det landet norrut, att Juda städer skola ödeläggas, och till drakaboningar varda.
Tamvani! kukubwera mphekesera, phokoso lalikulu la gulu la a ankhondo likumveka kuchokera kumpoto! Lidzasandutsa bwinja mizinda ya ku Yuda, malo okhala nkhandwe.
23 Jag vet, Herre, att menniskones väg står icke till henne; och det står i ingens mans magt, huru han vandra eller sin gång styra skall.
Inu Yehova, ndikudziwa kuti moyo umene munthu ali nawo si wake; munthuyo sangathe kuwongolera mayendedwe ake.
24 Näps mig, Herre, dock med måttelighet, och icke uti dine grymhet; på det du icke skall platt göra mig till intet.
Inu Yehova, langizeni, komatu mwachilungamo, osati ndi mkwiyo wanu, mungandiwononge kotheratu.
25 Men gjut dina vrede ut öfver Hedningarna som intet känna dig, och öfver de slägte som intet åkalla ditt Namn: ty de hafva uppfrätit och uppsvulgit Jacob; de hafva gjort en ända med honom, och hans boning förödt.
Tsanulirani ukali wanu pa mitundu ya anthu amene sakudziwani, ndiye kuti mitundu ya anthu amene satama pa dzina lanu mopemba. Iwo aja anasakaza Yakobo; amusakaza kotheratu ndipo awononga dziko lake.

< Jeremia 10 >