< Jeremia 1 >

1 Detta är Jeremia ord, Hilkia sons, af de Prester i Anathoth, i BenJamins land;
Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini.
2 Till hvilken skedde Herrans ord i Josia tid, Amons sons, Juda Konungs, uti trettonde årena af hans rike;
Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda.
3 Och sedan intill Jojakims tid, Josia sons, Juda Konungs, allt intill ändan på ellofte årena Zedekia, Josia sons, Juda Konungs, intill Jerusalems fängelse, i femte månadenom.
Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.
4 Och Herrans ord skedde till mig, och sade:
Yehova anayankhula nane kuti,
5 Jag kände dig, förr än jag tillredde dig i moderlifvet, och utkorade dig, förr än du af modrene född vardt, och satte dig till en Prophet ibland mång folk.
“Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale, iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale; ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”
6 Men jag sade: Ack! Herre Herre, jag doger intet till att predika, ty jag är för ung.
Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”
7 Då sade Herren till mig: Säg icke: Jag är för ung; utan du skall gå dit jag sänder dig, och predika hvad jag befaller dig.
Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira.
8 Frukta dig intet för dem; ty jag är när dig, och vill frälsa dig, säger Herren.
Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
9 Och Herren räckte ut sina hand, och tog uppå min mun; och Herren sade till mig: Si, jag sätter min ord i din mun.
Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako.
10 Si, jag sätter dig i dag öfver folk och rike, att du skall upprycka, nederbryta, förstöra och förderfva, och bygga, och plantera.
Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”
11 Och Herrans ord skedde till mig, och sade: Jeremia, hvad ser du? Jag sade: Jag ser en vakande staf.
Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”
12 Och Herren sade till mig: Rätt hafver du sett; ty jag vill vaka öfver mitt ord, att jag det göra skall.
Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”
13 Och Herrans ord skedde annan gången till mig, och sade: Hvad ser du? Jag sade: Jag ser en het sjudande gryto nordanefter.
Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”
14 Och Herren sade till mig: Nordanefter skall ondt komma öfver alla de som i landena bo.
Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto.
15 Ty si, jag vill kalla alla Förstar uti de rike norrut, säger Herren, att de skola komma och sätta sin säte inför portarna i Jerusalem, och allt omkring murarna, och för alla Juda städer.
Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova. “Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu polowera pa zipata za Yerusalemu; iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.
16 Och jag skall låta rätten gå öfver dem, för alla deras ondskos skull, att de öfvergifva mig, och röka androm gudom, och tillbedja sina händers verk.
Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine. Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina, ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.
17 Så begjorda nu dina länder, och statt upp, och predika dem allt det jag bjuder dig; frukta dig intet för dem, lika som jag skulle afskräcka dig.
“Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona.
18 Ty jag vill i denna dag göra dig till en fast stad, till en jernpelare, och till en kopparmur i hela landena, emot Juda Konungar, emot hans Förstar, emot hans Prester, emot folket i landena;
Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo.
19 Så att, om de än strida emot dig, skola de likväl intet öfvervinna dig; ty jag är när dig, säger Herren, att jag skall frälsa dig.
Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.

< Jeremia 1 >