< Jesaja 9 >

1 Ty det varder väl ett annat mörker, det dem bekymrar, än i förtiden var, då det lätteliga tillgick i Sebulons land, och i Naphthalims land, och derefter svårare vardt vid hafsvägen, på denna sidone Jordanen, vid Hedningarnas Galilea.
Anthu amene anali ndi nkhawa, sadzakhalanso otaya mtima. Masiku amakedzana Mulungu ananyozetsa dziko la Zebuloni ndi dziko la Nafutali, koma kutsogolo kuno dera lonse la Galileya, limene lili dziko la anthu a mitundu ina, kuyambira ku nyanja yayikulu, mʼmbali mwa Yorodani, adzalisandutsa laulemu.
2 Det folket, som i mörkret vandrar, ser ett stort ljus; och öfver dem, som bo i mörko lande, skin det klarliga.
Anthu oyenda mu mdima awona kuwala kwakukulu; kwa iwo okhala mʼdziko la mdima wandiweyani kuwunika kwawafikira.
3 Du gör folket mycket, dermed gör du icke glädjena, myckna; men för dig varder man sig glädjandes, såsom man glädes i skördandene, såsom man glad är, när man utskifter byte.
Inu mwauchulukitsa mtundu wanu ndipo mwawonjezera chimwemwe chawo. Iwo akukondwa pamaso panu, ngati mmene anthu amakondwera nthawi yokolola, ngatinso mmene anthu amakondwera pamene akugawana zolanda ku nkhondo.
4 Ty du hafver sönderbrutit deras bördos ok, och deras skuldrors ris, och deras plågares staf, lika som i Midians tid.
Monga munachitira pogonjetsa Amidiyani, inu mwathyola goli limene limawalemera, ndodo zimene amamenyera mapewa awo, ndiponso mikwapulo ya anthu owazunza.
5 Ty allt krig, med storm och blodig klädnad, skall uppbrännas, och af eld förtärdt varda.
Nsapato iliyonse ya munthu wankhondo, ndiponso chovala chilichonse chodonthekera magazi zidzatenthedwa pa moto ngati nkhuni.
6 Ty oss är födt ett barn, en Son är oss gifven, hvilkens herradöme är uppå hans axlar; och han heter Underlig, Råd, Gud, Hjelte, Evig Fader, Fridförste;
Chifukwa mwana watibadwira, mwana wamwamuna wapatsidwa kwa ife, ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake. Ndipo adzamutcha dzina lake lakuti Phungu Wodabwitsa, Mulungu Wamphamvu, Atate Amuyaya, ndi Mfumu ya Mtendere.
7 På det hans herradöme skall stort varda, och på friden ingen ände, på Davids säte och hans rike, att han det bereda, och stärka skall med dom och rättfärdighet, ifrå nu allt intill evighet; detta skall Herrans Zebaoths nitälskan göra.
Ulamuliro ndi mtendere wake zidzakhala zopanda malire. Iye adzalamulira ufumu wake ali pa mpando waufumu wa Davide, ndipo adzawukhazikitsa ndi kuwuchirikiza mwa chiweruzo cholungama ndi pochita zachilungamo kuyambira nthawi imeneyo mpaka muyaya. Ndi mtima wake wonse, Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza kuchita zimenezi.
8 Herren hafver sändt ett ord i Jacob, och det är fallet i Israel;
Ambuye atumiza mawu otsutsa Yakobo; ndipo mawuwo agwera pa Israeli.
9 Att allt Ephraims folk och Samarie inbyggare skola det få veta, hvilke i högmod och stolt sinne säga:
Anthu onse okhala mu Efereimu ndi okhala mu Samariya, adzadziwa zimenezi. Iwo amayankhula modzikuza kuti,
10 Tegelstenar äro fallne; men vi vilje bygga det upp igen med huggen sten; man hafver afhuggit mulbärsträ, så vilje vi sätta i samma staden cedreträ.
“Ngakhale njerwa zagumuka, koma ife tidzamanga ndi miyala yosema. Mitanda ya mkuyu yagwetsedwa, koma ife tidzayika mitanda ya mkungudza mʼmalo mwake.”
11 Ty Herren skall uppresa Rezins krigsfolk emot dem, och gadda deras fiendar tillhopa;
Koma Yehova wadzutsa adani kuti alimbane nawo ndipo wawafulumiza adani awo kuti amenyane nawo.
12 De Syrer före, och de Philisteer efter, att de skola uppfräta Israel med fullom mun. Uti allt detta stillas icke ännu hans vrede; hans hand är ännu uträckt.
Asiriya ochokera kummawa ndi Afilisti ochokera kumadzulo ndipo ayasama pakamwa kuti adye a Israeli. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
13 Så vänder sig ej heller folket till honom, som dem slår, och fråga intet efter Herran Zebaoth.
Koma anthu sanabwerere kwa amene anawakantha uja, ngakhale kufunafuna Yehova Wamphamvuzonse.
14 Derföre skall Herren afhugga af Israel både hufvud och stjert, både qvist och stubbs, på en dag.
Choncho Yehova adzadula mutu wa Israeli pamodzi ndi mchira womwe, nthambi ya kanjedza ndi bango lomwe tsiku limodzi;
15 De gamle och ärlige äro hufvudet; men Propheterna, som falskt lära, äro stjerten;
mutuwo ndiye akuluakulu ndi olemekezeka, mchira ndiye aneneri ophunzitsa zabodza.
16 Ty detta folks ledare äro förförare; och de som sig leda låta, äro förtappade.
Amene amatsogolera anthuwa ndiwo amawasocheretsa, ndipo otsogoleredwa amatayika.
17 Derföre kan Herren intet glädja sig öfver deras unga män, eller förbarma, sig öfver deras faderlösa och enkor; ty de äro allesammans skrymtare och onde, och hvar och en mun talar galenskap. Uti allt detta stillas icke ännu hans vrede; hans hand är ännu uträckt.
Nʼchifukwa chake Ambuye adzakondwera nawo achinyamata, ngakhale kuwachitira chifundo ana amasiye ndi akazi amasiye, pakuti aliyense ndi wosapembedza Mulungu ndiponso ndi wochimwa ndipo aliyense amayankhula zopusa. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
18 Ty det ogudaktiga väsendet är upptändt såsom en eld, och förtärer törne och tistlar, och brinner såsom uti en tjock skog, och gifver högan rök.
Ndithu kuyipa kwa anthuwo kumayaka ngati moto; moto wake umanyeketsa mkandankhuku ndi minga, umayatsa nkhalango yowirira, ndipo utsi wake umachita kuti toloo ngati mtambo.
19 Förty uti Herrans Zebaoths vrede är landet förmörkradt, så att folket är lika, som en eldsmat; ingen skonar den andra.
Dziko lidzatenthedwa ndi ukali wa Yehova Wamphamvuzonse, dziko lidzatenthedwa ndipo anthu adzakhala ngati nkhuni zosonkhera moto; palibe munthu amene adzachitire chifundo mʼbale wake.
20 Röfva de på högra sidone, så lida de hunger; äta de på venstra sidone, så varda, de icke mätte; hvar och en äter sins arms kött;
Kudzanja lamanja adzapeza chakudya nʼkudya, koma adzakhalabe ndi njala; kudzanja lamanzere adzapeza chakudya nʼkudya, koma sadzakhuta. Aliyense azidzadya ana ake omwe.
21 Manasse Ephraim, Ephraim Manasse, och de båda, tillsammans emot Juda. Uti allt detta stillas icke ännu hans vrede; hans hand är ännu uträckt.
Manase adzadya Efereimu ndipo Efereimu adzadya Manase; onsewa pamodzi adzadya Yuda. Komabe pa zonsezi, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.

< Jesaja 9 >