< Jesaja 63 >

1 Ho är den som ifrån Edom kommer, med färgad kläder ifrå Bozra; den så beprydd är i sin kläder, och går i sine stora kraft? Jag är den som rättfärdighet lärer, och är en mästare till att hjelpa.
Kodi ndani uyo akubwera kuchokera ku Edomu, atavala zovala za ku Bozira za madontho ofiira? Kodi uyu ndani, amene wavala zovala zokongola, akuyenda mwa mphamvu zake? “Ndi Ineyo, woyankhula zachilungamo ndiponso wamphamvu zopulumutsa.”
2 Hvi är då din klädnad så röd, och din kläder såsom en vintrampares?
Nanga bwanji zovala zanu zili psuu, ngati za munthu wofinya mphesa?
3 Jag trampar vinpressen allena, och ingen af folken är med mig; jag hafver trampat dem i mine vrede, och nedertrådat dem i mine grymhet; deraf hafver deras blod stänkt min kläder, och jag hafver besmittat all min kläder.
“Ndapondereza ndekha anthu a mitundu ina ngati mphesa, palibe ndi mmodzi yemwe anali nane. Ndinawapondereza ndili wokwiya ndipo ndinawapondereza ndili ndi ukali; magazi awo anadothera pa zovala zanga, ndipo zovala zanga zonse zinathimbirira.
4 Ty jag hafver tagit mig en hämndadag före; året till att förlossa de mina är kommet.
Pakuti ndinatsimikiza mu mtima mwanga kuti lafika tsiku lolipsira anthu anga; ndipo chaka cha kuwomboledwa kwanga chafika.
5 Ty jag såg mig om, och der var ingen hjelpare; och jag var i förskräckelse, och ingen uppehöll mig; utan min arm måste hjelpa mig, och min vrede uppehöll mig.
Ndinayangʼana ndipo panalibe munthu wondithandiza. Ndinadabwa kwambiri kuti panalibe wondichirikiza; choncho ndinapambana ndi mphamvu zanga, ndipo mkwiyo wanga unandilimbitsa.
6 Derföre hafver jag förtrampat folken uti mine vrede, och gjort dem druckna uti mine grymhet, och stött deras seger till markena.
Ndinapondereza mitundu ya anthu ndili wokwiya; ndipo ndinawasakaza ndipo ndinathira magazi awo pansi.”
7 Herrans barmhertighet vill jag ihågkomma, och Herrans lof, i allt det Herren oss gjort hafver, och det myckna goda med Israels hus, som han dem gjort hafver, genom sina barmhertighet och stora mildhet.
Ndidzafotokoza za kukoma mtima kwa Yehova, ntchito zimene Iye ayenera kutamandidwa. Ndidzatamanda Yehova chifukwa cha zonse zimene watichitira. Inde, mwa chifundo ndi kukoma mtima kwake Yehova wachitira nyumba ya Israeli zinthu zabwino zambiri.
8 Ty han sade: De äro ju mitt folk, barn som icke falsk äro; derföre var han deras Frälsare.
Yehova anati, “Ndithu awa ndi anthu anga, ana anga amene sadzandinyenga Ine.” Choncho anawapulumutsa.
9 Den som dem bedröfvade, han bedröfvade ock honom; och Ängelen, som för honom är, halp dem; han förlossade dem, derföre att han älskade dem, och skonade dem; han tog dem upp, och bar dem alltid af ålder.
Iyenso anasautsidwa mʼmasautso awo onse, ndipo mngelo wochokera kwa Iye anawapulumutsa. Mwa chikondi ndi chifundo chake iye anawapulumutsa, anawanyamula ndikuwatenga kuyambira kale lomwe.
10 Men de förbittrade och bedröfvade hans Helga Anda; derföre blef han deras fiende, och stridde emot dem.
Komabe iwo anawukira ndi kumvetsa chisoni Mzimu Woyera. Motero Yehova anatembenuka nakhala mdani wawo ndipo Iye mwini anamenyana nawo.
11 Och han tänkte åter på de förledna tider, på Mose som i hans folk var: Hvar är då nu den som förde dem utu hafvet, samt med sins hjords herda? Hvar är den som sin Helga Anda i dem gaf?
Pamenepo anthu ake anakumbukira masiku amakedzana, masiku a Mose mtumiki wake; ndipo anafunsa kuti, “Ali kuti Yehova amene anawawolotsa pa nyanja, pamodzi ndi Mose mʼbusa wawo? Ali kuti Iye amene anayika Mzimu Woyera pakati pawo?
12 Den Mose ledde vid högra handena, genom sin härliga arm; den der vattnet skiljde för dem, på det han skulle göra sig ett evigt namn;
Ali kuti amene anachita zinthu zodabwitsa ndi mphamvu zake zazikulu kudzera mwa Mose? Ali kuti amene anagawa madzi pa nyanja anthu ake akuona, kuti dzina lake limveke mpaka muyaya,
13 Den der förde dem igenom djupen, såsom hästar i öknene, de der intet snafva.
amene anawayendetsa pa nyanja yozama? Monga kavalo woyendayenda mʼchipululu, iwo sanapunthwe;
14 Såsom fä, det der nedergår på markene, det Herrans Ande drifver; alltså hafver du ock fört ditt folk, på det du skulle göra dig ett härligit namn.
Mzimu Woyera unawapumulitsa ngati mmene ngʼombe zimapumulira. Umu ndi mmene Inu munatsogolera anthu anu kuti dzina lanu lilemekezeke.”
15 Så se nu af himmelen, och skåda neder af dine helga och härliga boning; hvar är nu ditt nit, din magt? Din stora hjerteliga barmhertighet håller sig hårdeliga emot mig.
Inu Yehova amene muli kumwambako, pa mpando wanu wolemekezeka, wopatulika ndi waulemerero, tiyangʼaneni ife. Kodi changu chanu ndi mphamvu zanu zili kuti? Simukutionetsanso kukoma mtima kwanu ndi chifundo chanu.
16 Äst du dock vår fader; ty Abraham vet intet af oss, och Israel känner oss intet; men du, Herre, äst vår fader, och vår förlossare, af ålder är det ditt Namn.
Koma Inu ndinu Atate athu, ngakhale Abrahamu satidziwa kapena Israeli kutivomereza ife; Inu Yehova, ndinu Atate athu, kuyambira kale dzina lanu ndinu Mpulumutsi wathu.
17 Hvi låter du oss, Herre, ville fara ifrå dina vägar, och vårt hjerta förstockas, så att vi icke frukte dig? Vänd om för dina tjenares skull, för ditt arfs slägtes skull.
Chifukwa chiyani, Inu Yehova, mukutisocheretsa pa njira zanu? Bwanji mukutilola kuti tikhale owuma mitima kotero kuti sitikukuopaninso? Bwererani chifukwa cha atumiki anu; mafuko a anthu amene ali cholowa chanu.
18 De besitta ditt helga folk snart alltsamman; våre motståndare nedertrampa din helgedom.
Anthu anu atangokhala pa malo anu opatulika pa kanthawi kochepa, adani athu anasakaza malo anu opatulika.
19 Vi äre såsom tillförene, då du icke rådde öfver oss, och då vi efter ditt Namn icke nämnde vorom.
Ife tili ngati anthu amene simunawalamulirepo ngati iwo amene sanakhalepo anthu anu.

< Jesaja 63 >