< Jesaja 53 >
1 Men ho tror vår predikan, och hvem varder Herrans arm uppenbarad?
Ndani wakhulupirira zimene tanenazi; kapena ndani amene Yehova wamuzindikiritsa mphamvu zake?
2 Ty han rinner upp för honom såsom en vidja, och såsom en rot utu torro jord; han hafver ingen skapnad eller dägelighet. Vi såge honom; men der var ingen den skapnad, som oss kunde behaga.
Iye anakula ngati mphukira pamaso pake, ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma. Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira, analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.
3 Han var den aldraföraktadaste och vanvördaste, full med värk och krankhet; han var så föraktad, att man gömde bort ansigtet för honom; derföre aktade vi honom intet.
Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu, munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa, ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona. Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.
4 Sannerliga han bar våra krankhet, och lade uppå sig vår sveda; men vi hölle honom för den som plågad och af Gudi slagen och pinter var.
Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife; ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu. Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga, kumukantha ndi kumusautsa.
5 Men han är sargad för våra missgerningars skull, och slagen för våra synders skull; näpsten ligger uppå honom, på det att vi skulle frid hafva, och genom hans sår äre vi helade.
Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu; iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere, ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.
6 Vi ginge alle uti villfarelse, såsom får; hvar och en såg uppå sin väg; men Herren kastade allas våra synder uppå honom.
Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera, aliyense mwa ife akungodziyendera; ndipo Yehova wamusenzetsa zoyipa zathu zonse.
7 Då han näpst och plågad vardt, lät han icke upp sin mun; såsom ett lamb, det till slagtning ledes, och såsom ett får, det stilla tiger för sinom klippare, och låter icke upp sin mun.
Anthu anamuzunza ndi kumusautsa, koma sanayankhule kanthu. Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira, kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta, momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
8 Men han är tagen utur ångest och dom. Ho kan uttala hans lifslängd? Ty han är bortryckt utaf de lefvandes land, då han för mins folks missgerningar plågad var.
Atatha kumugwira mwankhanza ndikumuyimba mlandu, kenaka anapita naye kukamupha. Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake, poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo? Ndani anaganizirapo poona kuti iye anakanthidwa chifukwa cha zolakwa za anthu anga?
9 Och han är begrafven såsom de ogudaktige, och döder såsom en rik; ändock han ingom orätt gjort hade, ej heller något svek uti hans mun var.
Anamukonzera manda ake pamodzi ndi anthu oyipa ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi anthu achuma, ngakhale kuti iye sanachite za chiwawa, kapena kuyankhula za chinyengo.
10 Men Herren ville alltså slå honom med krankhet. När han sitt lif till skuldoffer gifvit hafver, så skall han få säd, och länge lefva, och Herrans uppsåt skall uti hans hand framgång hafva.
Komatu ndi Yehova amene anafuna kuti amuzunze ndi kumusautsa. Yehova anapereka moyo wa mtumiki wake kuti ukhale nsembe yoperekedwa chifukwa cha zolakwa. Tsono iye adzaona zidzukulu zake ndipo adzakhala ndi moyo wautali, ndipo chifuniro cha Yehova chidzachitika mwa iye.
11 Derföre, att hans själ arbetat hafver, skall han få se sina lust, och nog hafva, och genom sin kunskap skall han, min tjenare, den rättfärdige, många rättfärdiga göra; ty han bär deras synder.
Atatha mazunzo a moyo wake, adzaona kuwala, ndipo adzakhutira. Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo adzalungamitsa anthu ambiri, popeza adzasenza zolakwa zawo.
12 Derföre vill jag gifva honom ganska mycket till byte, och han skall hafva de starka till rof; derföre att han gifvit sitt lif i döden, och vardt ogerningsmannom lik räknad, och mångas synder bar, och bad för öfverträdarena.
Motero Ine ndidzamupatsa ulemu pamodzi ndi akuluakulu, adzagawana zofunkha ndi ankhondo amphamvu, popeza anapereka moyo wake mpaka kufa, ndipo anamuyika mʼgulu la anthu olakwa kuti akhululukidwe. Pakuti iye anasenza machimo a anthu ambiri, ndipo anawapempherera anthu olakwa.