< Jesaja 46 >
1 Bel lutar fast, Nebo är fallen, deras afgudar äro vordne djurom och ökom till tunga, att de skola bära sig trötta af edra bördo.
Beli wagwada pansi, Nebo wawerama; nyama zonyamula katundu za nyamula milungu yawo. Mafano awo asanduka katundu wolemera pa msana pa ngʼombe. Asandukadi ngati katundu pa msana pa nyama zotopa.
2 Ja, de falla, och luta allesamman, och kunna icke bortbära bördona; utan deras själ måste gå i fängelse.
Nyamazo zikuwerama ndi kufuna kugwa ndi milunguyo; sizikutha kupulumutsa katunduyo, izo zomwe zikupita ku ukapolo.
3 Hörer mig, I af Jacobs hus, och alle återlefde af Israels hus; I som i lifve bärens, och i qvede liggen.
Mverani Ine, Inu nyumba ya Yakobo, inu nonse otsala a mʼnyumba ya Israeli, Ine ndakhala ndi kukusamalirani kuyambira mʼmimba ya amayi anu, ndakhala ndikukunyamulani chibadwire chanu.
4 Ja, jag skall bära eder intill åldren, och intilldess I grå varden; jag skall görat; jag skall upplyfta, och bära, och hjelpa.
Mpaka pamene mudzakalambe ndi kumera imvi ndidzakusamalirani ndithu. Ndinakulengani ndipo ndidzakunyamulani, ndidzakusamalirani ndi kukulanditsani.
5 Vid hvem viljen I likna mig, och vid hvem mäten I mig, den jag lik skulle vara?
“Kodi inu mudzandifanizira ndi yani, kapena mufananitsa ndi yani? Kodi mudzandiyerekeza kapena kundifanizitsa ndi yani?
6 De slå guld utu säcken, och väga ut silfver med vigt, och leja guldsmeden, att han gör der en gud af, för hvilkom de knäfalla och tillbedja.
Anthu ena amakhuthula golide mʼzikwama zawo ndipo amayeza siliva pa masikelo; amalemba ntchito mʼmisiri wosula kuti awapangire mulungu, kenaka iwo amagwada pansi ndikupembedza kamulunguko.
7 De taga honom uppå axlarna, och bära honom, och sätta honom på sitt rum; der står han, och kommer intet utaf sitt rum; ropar någor till honom, då svarar han intet, och hjelper honom intet af hans nöd.
Amanyamula nʼkumayenda nayo milunguyo pa mapewa awo; amayikhazika pa malo pake ndipo imakhala pomwepo. Singathe kusuntha pamalo pakepo. Ngakhale wina apemphere kwa milunguyo singathe kuyankha; kapena kumupulumutsa ku mavuto ake.
8 På sådant tänker dock, och varer faste; I öfverträdare, går till edart hjerta.
“Kumbukirani zimenezi ndipo muchite manyazi, Muzilingalire mu mtima, inu anthu owukira.
9 Tänker uppå det i förtiden af ålder varit hafver; ty jag är Gud, och ingen mer, i en Gud hvilkens like ingenstäds är;
Kumbukirani zinthu zakale zinthu zamakedzana; chifukwa Ine ndine Mulungu ndipo palibe wina ofanana nane.
10 Jag, som förkunnar tillförene, hvad härefter komma skall, och tillförene förrän det sker, och säger: Mitt råd blifver ståndandes, och jag gör allt det mig täckes.
Ndinaneneratu zakumathero kuchokera pachiyambi pomwe. Kuyambira nthawi yamakedzana ndinaloseratu zoti zidzachitike. Ndikanena zimene ndifuna kuchita ndipo zimachitikadi. Chilichonse chimene ndafuna ndimachichita.
11 Jag kallar en fogel östanefter, och en man som min anslag fullkomnar af fjerran land. Hvad jag säger, det låter jag ske; hvad jag tänker, det gör jag ock.
Ndikuyitana chiwombankhanga kuchokera kummawa. Ndikuyitana kuchokera ku dziko lakutali munthu amene adzakwaniritsa cholinga changa. Zimene ndanena ndidzazikwaniritsadi; zimene ndafuna ndidzazichitadi.
12 Hörer mig, I stolthjertade, I som långt ären ifrå rättfärdighetene.
Ndimvereni, inu anthu owuma mtima, inu amene muli kutali ndi chipulumutso.
13 Jag hafver låtit mina rättfärdighet när komma; hon är icke långt borto, och min salighet dröjer icke; ty jag vill gifva salighet I Zion, och mina härlighet i Israel.
Ndikubweretsa pafupi tsiku la chipulumutso changa; sichili kutali. Tsikulo layandikira ndipo sindidzachedwa kukupulumutsani ndi kupereka ulemerero wanga kwa Israeli.