< Jesaja 34 >

1 Kommer, I Hedningar, och hörer; I folk, akter uppå; jorden höre till, och hvad derinne är, verldenes krets med sin växt.
Inu anthu a mitundu yonse, bwerani pafupi kuti mumve: tcherani khutu, inu anthu a mitundu ina yonse: Limvetsere dziko lapansi pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse pamodzi ndi zonse zochokera mʼmenemo!
2 Ty Herren är vred uppå alla Hedningar; och förtörnad uppå alla deras härar. Han skall gifva dem tillspillo, och öfverantvarda, dem till slagning.
Yehova wayipidwa ndi anthu a mitundu yonse; wapsera mtima magulu awo onse ankhondo. Iye adzawawononga kotheratu, nawapereka kuti aphedwe.
3 Deras slagne skola bortkastade varda, att stanken af deras kroppar skall uppgå, och bergen flyta i deras blod.
Anthu awo ophedwa adzatayidwa kunja, mitembo yawo idzawola ndi kununkha; mapiri adzafiira ndi magazi awo.
4 Och all himmelens här skall förruttna, och himmelen skall varda sammanlagd såsom ett bref; och all hans här skall förfalna, såsom ett löf förfalnar på vinträ, och såsom ett torrt löf på fikonaträ.
Dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zidzasungunuka ndipo mlengalenga mudzakulungidwa ngati chipepala; nyenyezi zonse zidzayoyoka ngati masamba ofota a mphesa, ngati masamba onyala a mtengo wa mkuyu.
5 Ty mitt svärd är drucket i himmelen, och si, det skall fara neder på Edom, och öfver det spillgifna folket till straff.
Yehova akuti, “Lupanga langa lakhutiratu magazi kumwamba; taonani, likutsika kudzalanga anthu a ku Edomu, anthu amene ndawawononga kotheratu.”
6 Herrans svärd är fullt med blod, och är fett af fetma, af lambablod och bockablod, af vädrars njuratalg; ty Herren håller ett offer i Bozra, och en stor slagtning i Edoms land.
Lupanga la Yehova lakhuta magazi, lakutidwa ndi mafuta; magazi a ana ankhosa onenepa ndi ambuzi, mafuta a ku impsyo za nkhosa zazimuna. Pakuti Yehova ali ndi nsembe mu Bozira ndiko kuphedwa kwa anthu ambiri mʼdziko la Edomu.
7 De enhörningar måste ock fara neder med dem, och stutarna med de gödda oxar; ty deras land måste drucket varda af blod, och deras jord fet varda af fetma.
Pamodzi ndi anthuwo zidzaphedwanso njati, ngʼombe zazimuna zazingʼono ndi zazikulu zomwe. Dziko lawo lidzakhala magazi okhaokha, ndipo nthaka idzakutidwa ndi mafuta.
8 Ty det är Herrans hämndadagar, och ett vedergälloår, till att hämnas Zion.
Iyi ndi nthawi imene Yehova adzalipsira ndi kulanga adani a Ziyoni.
9 Då skola dess bäck er varda till tjäro, och dess jord till svafvel; ja, dess land skall varda till brinnande tjäro;
Madzi a mʼmitsinje ya Edomu adzasanduka phula, ndipo fumbi lake lidzasanduka sulufule; dziko lake lidzasanduka phula lamoto!
10 Den hvarken dag eller natt utslockna skall; utan evinnerliga skall rök uppgå deraf, och skall öde blifva utan ända, så att ingen skall gå derigenom i evig tid;
Motowo sudzazimitsidwa usiku ndi usana; utsi wake udzafuka kosalekeza. Dzikolo lidzakhala chipululu pa mibado ndi mibado; palibe ndi mmodzi yemwe amene adzadutsemo.
11 Utan rördrommar och ufvar skola hafva det inne; nattugglor och korpar skola der bo; ty han skall draga ett snöre deröfver, att det skall öde varda, och ett murlod, att det skall tomt blifva;
Mʼdzikomo mudzakhala akabawi ndi anungu; amantchichi ndi akhwangwala adzapanga zisa zawo mʼmenemo. Mulungu adzatambalitsa pa Edomu chingwe choyezera cha chisokonezo ndi chingwe chowongolera cha chiwonongeko.
12 Så att dess herrar skola heta herrar utan land, och alle dess Förstar få en ända.
Anthu olemekezeka ake sadzatchedwanso mfumu kumeneko; akalonga ake onse adzachotsedwa.
13 Och skola törne växa uti dess palats, nässlor och tistlar uti dess borger; och skola varda en drakaboning, och bet för strutsar.
Minga idzamera mʼnyumba zake zankhondo zotetezedwa, khwisa ndi mitungwi zidzamera mʼmalinga ake. Ankhandwe azidzadya mʼmenemo; malo okhalamo akadzidzi.
14 Då skola der troll och spökelse löpa hvar om annan, och en gast skall möta den andra; elfvor skola ock hafva der herberge, och finna der ro.
Avumbwe adzakumana ndi afisi, ndipo zirombo za mʼchipululu zizidzayitanizana. Kumeneko kudzafikanso mizimu yoyipa ndi kupeza malo opumulirako.
15 Ufven skall ock hafva der sitt näste, och värpa der, ligga der, och utkläcka der, under dess skugga; och glador skola komma der tillsammans.
Kadzidzi adzamangako chisa chake nʼkuyikirako mazira, adzaswa ana ake ndi kusamalira ana ake mu mthunzi wa mapiko ake; akamtema adzasonkhananso kumeneko, awiriawiri.
16 Söker nu uti Herrans bok, och läser: Icke ett af dessa stycken skall fela; man skall ej sakna deraf antingen ett eller annat; ty han är den der igenom min mun bjuder, och hans Ande är den det tillhopahemtar.
Funafunani mʼbuku la Yehova ndi kuwerenga: mwa zolengedwazi palibe chimene chidzasowa; sipadzakhala nʼchimodzi chomwe chopanda chinzake. Pakuti Yehova walamula kuti zitero, ndipo Mzimu wake udzawasonkhanitsa pamodzi.
17 Han kastar lott öfver dem, och hans hand delar ut måttet ibland dem, att de skola hafva der arfvedel inne evinnerliga, och blifva deruti utan ända.
Yehova wagawa dziko lawo; wapatsa chilichonse chigawo chake. Dziko lidzakhala lawo mpaka muyaya ndipo zidzakhala mʼmenemo pa mibado yonse.

< Jesaja 34 >