< Jesaja 22 >

1 Detta är tungen öfver synedalen: Hvad är eder, att I så alle löpen på taken?
Uthenga wonena za Chigwa cha Masomphenya: Kodi chachitika nʼchiyani, kuti nonsenu mukwere pa madenga?
2 Du vast full med gny, en stad full med folk, en glad stad; dine slagne äro icke med svärd slagne, och icke döde blefne i strid;
Iwe mzinda wodzaza ndi chisangalalo chodzaza tsaya, iwe mzinda waphokoso ndi wosokonekera? Anthu ako ophedwa aja sanaphedwe ndi lupanga, kapena kufera pa nkhondo.
3 Utan alle dine höfvitsmän äro tillika bortvekne för båga, och fångne; alle de, Som man uti dig funnit hafver, äro fångne, och långt bortflydde.
Atsogoleri ako onse ngakhale anathawa limodzi; koma anagwidwa osadziteteza nʼkomwe. Inu munapezeka ndipo nonse pamodzi munatengedwa ukapolo, ngakhale munathawa pamene mdani akanali patali.
4 Derföre säger jag: Går ifrå mig, låter mig bitterliga gråta; farer icke efter att hugsvala mig öfver mins folks dotters förstöring.
Nʼchifukwa chake Ine ndinati, “Chokani pamaso panga; ndilekeni ndilire ndi mtima wowawa. Musayesere kunditonthoza chifukwa cha kuwonongeka kwa anthu anga.”
5 Ty det är en bullers, förtryckelses och bekymmers dag af Herranom Zebaoth, i synedalenom, för murarnas undergrafnings skull, och för ropets skull på berget.
Lero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse walola kuti tione mavuto ndi kugonjetsedwa ndiponso chisokonezo mʼChigwa cha Masomphenya. Malinga agumuka, komanso anthu akanalira mofuwula ku mapiri.
6 Ty Elam drager med koger, vagnar, folk och resenärar, och Kir glimmar af sköldar.
Ankhondo a ku Elamu anadza pa magaleta ndi akavalo ali ndi mivi mʼmanja. Ankhondo a ku Kiri anakonzeka ndi zishango.
7 Och skall ske, att dina utkorade dalar skola med vagnar fulle varda, och resenärer skola lägga sig för portarna.
Zigwa zanu zachonde ndi zodzaza ndi magaleta, ndipo asilikali okwera pa akavalo ayikidwa pa zipata za mzinda;
8 Då skall Juda förlåt öppnad varda, att man skall kunna se, på den tiden, tygen uti skogshuset.
zonse zoteteza Yuda zachotsedwa. Ndipo tsiku limenelo munayangʼanayangʼana zida zankhondo zomwe zinali mʼnyumba yaufumu ya nkhalango;
9 Och I skolen se refvorna många vara på Davids stad, och skolen församla vatten uti dem nedra dammenom.
inu munaona kuti makoma ambiri a mzinda wa Davide anali ndi malo ambiri ogumuka; munasunga madzi mu chidziwe chakumunsi.
10 I skolen ock räkna, husen i Jerusalem, ja, I skolen afbryta husen, till att befästa murarna.
Munawerenga nyumba zonse za mu Yerusalemu ndipo munagwetsa nyumba zina kuti mulimbitse linga logumuka lija.
11 Och I skolen göra ena vattugraf, emellan båda murarna af den gamla dammens vatten; likväl sen I icke uppå den som detta gör, och skåden icke på den som sådant beställt hafver fjerranefter.
Pakati pa makoma awiri munamanga chitsime chosungiramo madzi ochokera ku dziwe lakale, koma inu simunadalire Mulungu amene anapanga zimenezi, kapena kusamalako za Iye amene anazilenga kale lomwe.
12 Derföre skall Herren, Herren Zebaoth på den tiden låta utropa, att man skall gråta och jämra sig, och kulla sig, och draga säck uppå;
Pa tsiku limenelo, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse anakuyitanani kuti mulire ndi kukhetsa misozi; kumeta mutu wanu mpala ndi kuvala ziguduli.
13 Ändock nu, si; intet annat är än glädje, slagta oxar, dräpa får, äta kött, dricka vin, och säga: Låt oss äta och dricka, vi måste dock i morgon dö.
Koma mʼmalo mwake inu munakondwa ndi kusangalala; munapha ngʼombe ndi nkhosa; munadya nyama ndi kumwa vinyo. Inu mumati, “Tiyeni tidye ndi kumwa pakuti mawa tifa!”
14 Detta är för Herrans Zebaoths öron uppenbart. Hvad gäller, om eder denna missgerningen förlåtas skall, tilldess I dön, säger Herren, Herren Zebaoth.
Yehova Wamphamvuzonse wandiwululira mondinongʼoneza kuti, “Tchimo limeneli sindidzakhululuka mpaka tsiku la kufa kwanu,” akutero Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse.
15 Så säger Herren, Herren Zebaoth: Gack in till räntomästaren Sebna, hofmästaren, och säg till honom:
Chimene Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pita, ukanene kwa Sabina kapitawo, amene amayangʼanira nyumba yaufumu:
16 Hvad hafver du här? Hvem hörer du till? att du låter dig hugga en graf, såsom den der låter sig hugga en graf i höjdene, och såsom den der låter sig göra en boning i bergklippone?
Kodi ukuchita chiyani kuno, nanga ndani anakupatsa chilolezo kuti udzikumbire manda kuno, kudzikumbira manda pa phiri ndi kudzisemera malo opumulira mʼthanthwe?
17 Si, Herren skall förkasta dig, såsom en stark man någon bortkastar, och nederkrafsa dig;
“Samalira, Yehova watsala pangʼono kukugwira zolimba ndi kukuponya mwamphamvu, iwe munthu wamphamvu.
18 Och skall omdrifva dig, såsom ett klot på vida mark; der skall du dö, der skola dina kosteliga vagnar blifva med dins herras hus försmädelse.
Iye adzakukulunga kwambiri ngati mpira ndipo adzakuponyera mʼdziko lalikulu. Kumeneko ndiko ukafere ndipo kumeneko ndiko kudzatsalire magaleta ako. Ndipo udzasanduka wochititsa manyazi nyumba ya mbuye wako.
19 Och jag skall störta dig ifrå ditt stånd, och sätta dig af ditt ämbete.
Ine ndidzakuchotsa pa ukapitawo wako ndipo ndidzakutsitsa pa udindo wako.
20 Och på den tiden vill jag kalla min tjenare Eliakim, Hilkia son;
“Tsiku limenelo ndidzayitanitsa mtumiki wanga, Eliyakimu mwana wa Hilikiya.
21 Och draga din kjortel uppå honom, och omgjorda honom med ditt bälte, och gifva ditt välde uti hans hand, att han skall vara deras fader, som i Jerusalem och Juda hus bo;
Ndidzamuveka mkanjo wako ndi kumangira lamba wako mʼchiwuno mwake ndi kumupatsa ulamuliro wako. Iye adzakhala kholo la amene amakhala mu Yerusalemu ndiponso a fuko la Yuda.
22 Och skall lägga Davids hus nyckel uppå hans axlar, att han skall upplåta, och ingen skall tillsluta; att han skall tillsluta, och ingen upplåta.
Ndidzamupatsa ulamuliro wa banja la Davide. Adzatsekula ndipo palibe adzatseke, adzatseka popanda wina kutsekula.
23 Och jag vill inslå honom för en nagla på ett fast rum, och han skall hafva ärones stol uti sins faders hus;
Ufumu wake udzakhala wokhazikika ngati chikhomo chokhomedwa pa malo olimba. Anthu adzalemekeza nyumba ya abale ake chifukwa cha iye.
24 Att man skall hänga uppå honom all hans faders hus härlighet, barn och barnabarn, all små tyg, både dryckekar och allahanda strängaspel.
Ana ndi abale a nyumba ya abambo ake adzakhala ngati katundu pa iye ngati ziwiya zopanda ntchito zimene zapachikidwa pa chikhomo.
25 På den tiden, säger Herren Zebaoth, skall nagelen borttagen varda, den på det fasta rummet står, så att han skall söndergå och falla, och hans börda förgås; ty Herren säger det.
“Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Tsiku limeneli chikhomo chokhomedwa kwambiri chija sichidzalimbanso; chidzazuka ndipo chidzagwa ndipo zonse zopachikidwa zidzawonongedwa.’” Yehova wayankhula chomwechi.

< Jesaja 22 >