< Jesaja 21 >

1 Detta är tungen öfver öknena vid hafvet: Såsom ett väder kommer ifrå sunnan, det all ting omvänder, så kommer det utur öknene, utur ett grufveligit land.
Uthenga wonena za chipululu cha mʼmbali mwa Nyanja. Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya adzabwera ngati kamvuluvulu amene akuwomba modutsa mʼmbali ya nyanja, kuchokera ku chipululu, dziko lochititsa mantha.
2 Ty mig är betedd en hård syn: En föraktare kommer emot den andra; och en förstörare emot den andra; drag upp, Elam, belägg dem, Madai; jag skall göra en ända uppå allt hans suckande.
Ine ndaona zinthu zoopsa mʼmasomphenya: Wonyenga akunyenga, wofunkha akufunkha komanso owononga akuwononga. Elamu, yambani nkhondo! Mediya, zingani mzinda! Ine ndidzathetsa mavuto onse amene anayambitsa Ababuloni.
3 Derföre äro mina länder fulla mes värk, och ångest hafver begripit mig, såsom ena barnafödersko; jag kröker mig, när jag hörer det, och förskräckes, när jag ser deruppå.
Chifukwa cha zimenezi thupi langa likunjenjemera ndi mantha, ndikumva ululu ngati wa mayi amene akubereka; ndikuvutika kwambiri ndi zimene ndikumva, ndathedwa nzeru ndi zimene ndikuziona.
4 Mitt hjerta bäfvar; grufvelse hafver mig förskräckt; jag hafver derföre uti den ljufva nattene ingen ro haft.
Mtima wanga ukugunda, ndipo ndikunjenjemera ndi mantha; chisisira chimene ndakhala ndikuchifuna chasanduka chinthu choopsa kwa ine.
5 Ja, tillred ett bord, låt vaka på vaktene, äter, dricker; står upp, I Förstar, smörjer skölden.
Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya akukonza matebulo, akuyala mphasa, akudya komanso kumwa! Mwadzidzidzi anamva mawu akuti, “Dzukani inu ankhondo, pakani mafuta zishango zanu!”
6 Ty Herren säger till mig alltså: Gack bort och beställ en väktare, den som tillser och tillsäger.
Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi; “Pita, kayike mlonda kuti azinena zimene akuziona.
7 Men han ser resenärer rida och fara med hästar, åsnar, och camelar, och hafver granneliga akt deruppå.
Taonani, anthu akubwera ali pa akavalo ndipo akuyenda awiriawiri, okwera pa bulu kapena okwera pa ngamira, mlondayo akhale tcheru kwambiri.”
8 Och ett lejon ropade: Herre, jag står på vaktene alltjemt om dagen, och står i mine vakt alla nätter.
Ndipo mlondayo anafuwula kuti, “Ambuye anga, tsiku ndi tsiku ndimakhala pa nsanja yolondera; Usiku uliwonse ndimakhala pa malo anga olondera.
9 Och si, der kommer en på enom vagn, han svarar, och säger: Babel är fallet; det är fallet, och all dess gudars beläte äro slagne ned till markena.
Taonani, uyo munthu akubwera atakwera pa galeta ali ndi gulu la akavalo. Mmodzi wa iwo akuti, ‘Babuloni wagwa, wagwa! Mafano onse a milungu yake agwa pansi ndipo aphwanyika!’”
10 O! min loge, der jag på tröskar; hvad jag af Herranom Zebaoth Israels Gudi hört hafver, det förkunnar jag eder.
Inu anthu anga opunthidwa ndi kupetedwa ngati tirigu, ine ndikukuwuzani zimene ndamva ndikukuwuzani Uthenga wochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli.
11 Detta är tungen öfver Duma: Man ropar till mig utaf Seir: Väktare, hvad lider natten? Väktare, hvad lider natten?
Uthenga wonena za Duma: Munthu wina akundiyitana kuchokera ku Seiri kuti, “Iwe mlonda, usikuwu utha liti? Iwe mlonda, utha liti kodi usikuwu?”
12 Väktaren sade: Då morgonen än kommer, så skall det ändå vara natt; om I än frågen, så skolen I likväl igenkomma och åter fråga.
Mlonda akuyankha kuti, “Kukucha, koma kudanso. Ngati ukufuna kufunsa, funsa tsopano; ndipo ubwerenso udzafunse.”
13 Detta är tungen öfver Arabien: I skolen bo uti skogenom i Arabien, på den vägen åt Dedanim.
Uthenga wonena za Arabiya: Inu anthu amalonda a ku Dedani, amene usiku mumagona mʼzithukuluzi za ku Arabiya,
14 Bärer vatten emot den törstiga, I som bon uti Thema land; bjuder dem flyktigom bröd;
perekani madzi kwa anthu aludzu. Inu anthu a ku Tema perekani chakudya kwa anthu othawa nkhondo.
15 Förty de flyr för svärd, ja, för draget svärd, för spändom båga, för storo strid.
Iwo akuthawa malupanga, lupanga losololedwa, akuthawa uta wokokakoka ndiponso nkhondo yoopsa.
16 Ty alltså, säger Herren till mig: Ännu innan ett år, såsom legodrängers år äro, skall all Kedars härlighet förgås;
Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi: “Chaka chimodzi chisanathe, potsata mmene amawerengera munthu waganyu, ulemerero wonse wa Kedara udzatheratu.
17 Och de qvarblefne skyttar af hjeltarna i Kedar skola mindre varda; ty Herren Israels Gud hafver det så sagt.
Mwa anthu okoka uta, ankhondo a ku Kedara opulumuka adzakhala owerengeka.” Wayankhula ndi Yehova Mulungu wa Israeli.

< Jesaja 21 >