< Jesaja 2 >

1 Detta är det Esaia, Amos son, såg om Juda och Jerusalem:
Nazi zinthu zokhudza Yuda ndi Yerusalemu, zimene Yesaya mwana wa Amozi anaziona mʼmasomphenya:
2 Uti yttersta tiden skall det berget, der Herrans hus är, tillredt varda, högre än all berg, och öfver all berg upphöjdt varda; och alle Hedningar skola löpa dertill;
Mʼmasiku otsiriza, phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse, lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse, ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.
3 Och mycket folk gå dit, och säga: Kommer, och låter oss gå upp på Herrans berg, till Jacobs Guds hus, att han lärer oss sina vägar, och vi vandrom på hans stigar; ty af Zion skall lagen utgå, och Herrans ord af Jerusalem.
Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti, “Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.” Malangizo adzachokera ku Ziyoni, mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
4 Och han skall döma ibland Hedningarna, och straffa mång folk; då skola de göra sin svärd till plogbillar, och sin spjut till liar; ty intet folk skall upplyfta svärd emot det andra, och skola nu intet lära mer att örliga.
Iye adzaweruza pakati pa mayiko, ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri. Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera. Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina, kapena kuphunziranso za nkhondo.
5 Kommer, I af Jacobs hus, låt oss vandra uti Herrans ljus.
Inu nyumba ya Yakobo, bwerani, tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.
6 Men du hafver låtit fara ditt folk, Jacobs hus; ty de bedrifvat mer än de österländningar, och äro dagaväljare såsom de Philisteer; och låta de främmande barn varda mång.
Inu Yehova mwawakana anthu anu, nyumba ya Yakobo. Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa; amawombeza mawula ngati Afilisti, ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.
7 Deras land är fullt med silfver och guld, och på deras rikedom är ingen ände; deras land är fullt med hästar, och på deras vagnar är ingen ände.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide; ndipo chuma chawo ndi chosatha. Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo; ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.
8 Deras land är också fullt med afgudar, och de tillbedja sitt handaverk, det deras finger gjort hafva.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano; iwo amapembedza ntchito ya manja awo, amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.
9 Der bugar den menige man, der ödmjuka sig de myndige; det varder du icke förlåtandes dem.
Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa ndi kutsitsidwa. Inu Yehova musawakhululukire.
10 Gack in uti bergen, och bortgöm dig uti jordene, för Herrans fruktan, och för hans härliga majestät.
Lowani mʼmatanthwe, bisalani mʼmaenje, kuthawa kuopsa kwa Yehova ndi ulemerero wa ufumu wake!
11 Förty all hög ögon skola förnedrad varda, och hvad högt är ibland menniskor, det måste bocka sig; men Herren skall på den tid allena hög vara.
Kudzikuza kwa anthu kudzatha, ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa; Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.
12 Ty Herrans Zebaoths dag skall gå öfver allt högfärdigt och högt, och öfver allt upphäfvet, att det skall förnedradt varda;
Yehova Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku limene adzatsitse onse onyada ndi odzitama, ndipo adzagonjetsa onse amphamvu,
13 Och öfver all hög och upphäfven cedreträ i Libanon, och öfver alla ekar i Basan;
tsiku la mikungudza yonse ya ku Lebanoni, yayitali ndi yoonekera patali, ndiponso la mitengo yonse ya thundu ya ku Basani,
14 Öfver all hög berg, och öfver alla upphöjda backar;
tsiku la mapiri onse ataliatali ndiponso la zitunda zonse zazitali,
15 Öfver all hög torn, och öfver alla fasta murar;
tsiku la nsanja zonse zazitali ndiponso malinga onse olimba,
16 Öfver all skepp i hafvet, och öfver all kostelig skepps baner;
tsiku la sitima zapamadzi zonse za ku Tarisisi ndiponso la mabwato onse okongola.
17 Att sig böja måste all höghet, och sig ödmjuka hvad högt är ibland menniskorna; och Herren allena hög vara på den tiden.
Kudzikuza kwa munthu kudzatha ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa, Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo,
18 Och afgudarna skola platt förgås.
ndipo mafano onse adzatheratu.
19 Så skall man gå in uti bergskrefvor, och uti jordkulor, för Herrans fruktan, och för hans härliga majestät, då han tager till att förskräcka jordena.
Anthu adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndi mʼmaenje a nthaka, kuthawa mkwiyo wa Yehova, ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
20 På den tiden skall hvar och en bortkasta sina silfverafgudar, och gyldene afgudar, som han sig hafver göra låtit till att tillbedja, och till att ära mullvärplar och flädermöss;
Tsiku limenelo anthu adzatayira mfuko ndi mileme mafano awo asiliva ndi mafano awo agolide, amene anawapanga kuti aziwapembedza.
21 På det han må krypa in uti stenklyftor, och i bergskrefvor, för Herrans fruktan, och för hans härliga majestät, då han tager till att förskräcka jordena.
Adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndiponso mʼmingʼalu ya nthaka kuthawa mkwiyo wa Yehova ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
22 Så befatter eder intet med menniskone, som anda hafver i näsone; ty I veten icke, huru högt han är aktad.
Lekani kudalira munthu, amene moyo wake sukhalira kutha. Iye angathandize bwanji wina aliyense?

< Jesaja 2 >