< Jesaja 15 >

1 Detta är tungen öfver Moab: Om nattena kommer förstöring öfver Ar i Moab, det är sin kos; om nattena, kommer förstöring öfver Kir i Moab, det är sin kos.
Uthenga wonena za Mowabu: Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha. Mzinda wa Kiri wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
2 De gå upp till Baith och Dibon till altaren, att de skola gråta och jämra sig öfver Nebo och Medba i Moab: All hufvud är rakad, allt skägg är afskuret.
Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo, akupita ku malo awo achipembedzo kukalira; anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba. Mutu uliwonse wametedwa mpala, ndipo ndevu zonse zametedwa.
3 På deras gator gå de omsvepte i säcker; på deras tak och gatom jämra de sig alle, och gå neder gråtande.
Mʼmisewu akuvala ziguduli; pa madenga ndi mʼmabwalo aliyense akulira mofuwula, misozi ili pupupu.
4 Hesbon och Eleale ropa, så att man hörer det intill Jahaz; derföre jämra sig de väpnade i Moab, ty deras själ går illa.
Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula, mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi. Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula, ndipo ataya mtima.
5 Mitt hjerta ropar till Moab, deras flyktige fly ifrå den treggaåra kon allt intill Zoar; ty de gå upp till Luhith och gråta; och på den vägenom till Horonaim upphäfver sig ett jämmerrop.
Inenso ndikulirira Mowabu; chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari ndi Egilati-Selisiya akupita akulira ku chikweza cha Luhiti, Akulira mosweka mtima pa njira yopita ku Horonaimu; akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.
6 Ty de vatten i Nimrim torkas bort, så att höet förtorkas der, och gräset förvissnar, och växer ingen grön ört.
Madzi a ku Nimurimu aphwa ndipo udzu wauma; zomera zawonongeka ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.
7 Ty de ägodelar, som de församlat, och de folk, som de tillrustat hafva, förer man öfver pilträbäcken.
Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga, achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.
8 Ropet går omkring uti Moabs gränsor de gråta allt intill Eglaim, och gråta vid den brunnen Elim;
Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu; kulira kwawo kosweka mtima kukumveka mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.
9 Ty de vatten i Dimon äro full med blod; dertill vill jag ännu låta mer komma öfver Dimon, både öfver dem som behållne äro i Moab lejonens, och öfver dem igenlefda i landena.
Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi, komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni, mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.

< Jesaja 15 >