< Jesaja 14 >

1 Ty Herren skall förbarma sig öfver Jacob, och ännu utkora Israel, och sätta dem uti sitt land: och främlingar skola gifva sig till dem, och hålla sig intill Jacobs hus;
Yehova adzachitira chifundo Yakobo; adzasankhanso Israeli ndi kuwalola kuti akhalenso mʼdziko lawo. Alendo adzabwera kudzakhala nawo ndi kudziphatika okha kukhala ngati a mʼnyumba ya Yakobo.
2 Och folk skola, dem till sig taga, och hafva dem in till sitt rum, så att Israels hus skall äga dem uti Herrans land till tjenare och tjenarinnor; och skola hålla dem fångna, af hvilkom de fångne voro, och skola råda öfver sina plågare.
Anthu a mitundu ina adzaperekeza a Israeli ku dziko lawo. Tsono Aisraeli adzasandutsa anthu a mitundu ina aja kukhala antchito awo aamuna ndi aakazi mʼdziko la Yehova. Ndiye kuti Aisraeli adzasandutsa akapolo anthu amene kale anali ambuye awo. Iwo adzasandutsa akapolo anthu amene kale ankawalamulira ndi kuwazunza.
3 Och på den tiden, då Herren varder dig ro gifvandes ifrå din jämmer och vedermöda, och ifrå den hårda träldom, der du uti varit hafver;
Yehova akadzakupumitsani ku zowawa ndi mavuto, ndiponso kuntchito yakalavulagaga imene ankakugwiritsani,
4 Så skall du föra ett sådant ordspråk emot Konungen af Babel, och säga: Huru är det nu ute med plågarenom, och beskattningen hafver en ända?
mudzayankhula monyogodola mfumu ya Babuloni kuti, Wopsinja uja watha! Ukali wake uja watha!
5 Herren hafver sönderbrutit de ogudaktigas ris, de väldigas ris;
Yehova wathyola chikwapu cha anthu oyipa, Iye waphwanya ndodo ya olamulira.
6 Den som folk slog i grymhet utan återvändo, och med stränghet rådandes var öfver Hedningarna, och förföljde dem utan barmhertighet.
Mfumu ya ku Babuloni inkakantha mitundu ya anthu mwaukali powamenya kosalekeza, Iyo inkagonjetsa anthu a mitundu ina mwaukali ndikuwazunza kosalekeza.
7 Nu hafver dock hela verlden ro, och är stilla, och fröjdar sig i glädje.
Koma tsopano mayiko onse ali pa mpumulo ndi pa mtendere; ndipo akuyimba mokondwa.
8 Ock fröjda sig furoträn öfver dig, och de cedreträ i Libanon ( och säga ): Efter du ligger, så kommer ingen upp, som oss afhugger.
Ngakhale mitengo ya payini ndi mikungudza ya ku Lebanoni ikuyimba za iwe mokondwa ndipo ikuti, “Chigwetsedwere chako pansi, palibe wina anabwera kudzatigwetsa.”
9 Helvetet dernedre bäfvade för dig, emot din tillkommelse; det uppväcker dig de döda, alla verldenes bockar, och bad alla Hedningarnas Konungar uppstå utaf sina stolar; (Sheol h7585)
Ku manda kwatekeseka kuti akulandire ukamabwera; mizimu ya anthu akufa, aja amene anali atsogoleri a dziko lapansi, yadzutsidwa. Onse amene anali mafumu a mitundu ya anthu ayimiritsidwa pa mipando yawo. (Sheol h7585)
10 Att de skulle, en efter den andra, tala, och säga till dig: Du äst ock slagen lika som vi, och dig går lika som oss.
Onse adzayankha; adzanena kwa iwe kuti, “Iwenso watheratu mphamvu ngati ife; Iwe wafanana ndi ife.”
11 Ditt prål är neder till helvete faret, samt med dina harpors klingande; mal skall vara din säng, och matkar ditt öfvertäckelse. (Sheol h7585)
Ulemerero wako wonse walowa mʼmanda, pamodzi ndi nyimbo za azeze ako; mphutsi zayalana pogona pako ndipo chofunda chako ndi nyongolotsi. (Sheol h7585)
12 Huru äst du af himmelen fallen, du sköna morgonstjerna? Huru äst du till jordena fallen, du som försvagade Hedningarna?
Wagwa pansi bwanji kuchoka kumwamba, iwe nthanda, mwana wa mʼbandakucha! Wagwetsedwa pansi pa dziko lapansi, Iwe amene unagonjetsapo mitundu ya anthu!
13 Tänkte du dock uti ditt hjerta: Jag vill stiga upp i himmelen, och förhöja min stol upp öfver Guds stjernor. Jag vill sätta mig på vittnesbördsens berg, på den sidon norrut.
Mu mtima mwako unkanena kuti, “Ndidzakwera mpaka kumwamba; ndidzakhazika mpando wanga waufumu pamwamba pa nyenyezi za Mulungu; ndidzakhala pa mpando waufumu pa phiri losonkhanirako, pamwamba penipeni pa phiri la kumpoto.
14 Jag vill fara öfver de höga skyar, och vara den Aldrahögsta lik.
Ndidzakwera pamwamba pa mitambo; ndidzafanana ndi Wammwambamwamba.”
15 Ja, till helvetes far du, vid kulones sida. (Sheol h7585)
Koma watsitsidwa mʼmanda pansi penipeni pa dzenje. (Sheol h7585)
16 Den dig ser, han skall skåda dig, och se uppå dig ( och säga ): Är det den man, som verldena skälfvande gjorde, och Konungariken bäfvande;
Anthu akufa adzakupenyetsetsa nadzamalingalira za iwe nʼkumati, “Kodi uyu ndi munthu uja anagwedeza dziko lapansi ndi kunjenjemeretsa maufumu,
17 Den der jordenes krets ödelade, och städerna derinne nederslog, och gaf icke sina fångar lösa?
munthu amene anasandutsa dziko lonse chipululu, amene anagwetsa mizinda yake ndipo sankalola kuti anthu ogwidwa abwerere kwawo?”
18 Allesamman Hedningarnas Konungar ligga dock med äro, hvar och en i sitt hus;
Mafumu onse a mitundu ya anthu akugona mwaulemu aliyense mʼmanda akeake.
19 Men du äst förkastad utu dine graf, såsom en förderfvad gren, såsom de slagnas klädnad, som med svärd ihjälstungne äro, hvilke nederfara till helvetes stenar, såsom ett förtrampadt as. (questioned)
Koma iwe watayidwa kunja kwa manda ako, ngati nthambi yowola ndi yonyansa. Mtembo wako waphimbidwa ndi anthu ophedwa; amene anabayidwa ndi lupanga, anatsikira mʼdzenje lamiyala ngati mtembo woponderezedwa.
20 Du skall icke såsom de begrafven varda; ty du hafver förderfvat ditt land, och slagit ditt folk; ty man skall aldrig tänka på den ondskofulla sädena.
Sudzayikidwa nawo mʼmanda mwaulemu, chifukwa unawononga dziko lako ndi kupha anthu ako. Zidzukulu za anthu oyipa sizidzakumbukika nʼpangʼono pomwe.
21 Reder till, att man må slagta hans barn, för deras fäders missgerningars skull, att de icke uppkomma eller ärfva landet, eller göra jordenes krets fullan med fiendar.
Konzani malo woti muphere ana ake aamuna chifukwa cha machimo a makolo awo; kuti angadzuke ndi kulanda dziko lapansi ndi kulidzaza dziko lonselo ndi mizinda yawo.
22 Och jag skall öfver dem komma säger Herren Zebaoth, och i Babel utrota hans åminnelse, hans igenlefda, affödo och efterkommande, säger Herren;
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzathira nkhondo mzinda wa Babuloni. Ndidzachotseratu mu Babuloni dzina lake ndi onse otsaliramo. Ndiye kuti sipadzakhala ana kapena zidzukulu,” akutero Yehova.
23 Och skall göra honom igelkottom till arfs, och till en vattusjö, och skall sopa honom med förderfvelsens qvast, säger Herren Zebaoth.
“Ndidzawusandutsa mzindawo malo okhalamo anungu ndiponso dambo lamatope; ndidzawusesa ndi tsache lowononga,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
24 Herren Zebaoth hafver svorit, och sagt: Hvad gäller, att det skall så ske som jag tänker, och skall så blifva, som jag i sinnet hafver;
Yehova Wamphamvuzonse walumbira kuti, “Ndithudi, monga ndaganizira ndidzachitadi choncho, ndipo monga momwe ndatsimikizira zidzakhala momwemo ndithu.
25 Att Assur nederlagd varder i mitt land, och jag förtrampar honom på min berg; på det hans ok skall af dem taget varda, och hans börda af deras hals komma.
Ndidzawawononga Asiriya mʼdziko langa; ndidzawapondereza ndi mapazi pa mapiri anga; ndidzachotsa goli lawo pa anthu anga, ndipo ndidzachotsa katundu wawo pa mapewa awo.”
26 Detta äro de anslag, som han hafver öfver all land, och det är den uträckta hand öfver alla Hedningar.
Izi ndizo ndakonza kuti zichitike pa dziko lonse lapansi, ndatambasula dzanja pa anthu a mitundu yonse.
27 Ty Herren Zebaoth hafver det beslutit; ho vill förmenat? Och hans hand är uträckt; ho kan afvända henne?
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza, ndipo ndani angamuletse? Dzanja lake latambasulidwa ndipo ndani angalibweze?
28 I det året, då Konung Ahas blef död, vardt denne tungen sedd.
Uthenga uwu unabwera chaka chimene mfumu Ahazi anamwalira:
29 Fröjda dig icke så fast, du Philistea, att det ris, som dig slog, sönderbrutet är; ty utaf ormsens rot skall komma en basilisk, och hans frukt skall vara en brinnande flygande drake.
Musakondwere inu Afilisti nonse kuti Asiriya amene anali ngati ndodo yokukanthani anathedwa; chifukwa kuchokera ku njoka yomweyi (mfumu ya Aasiriya) mudzatuluka mphiri, ndipo chipatso chake chidzakhala njoka yaliwiro ndiponso yaululu.
30 Ty de torftigas förstfödingar skola berga sig, och de fattige tryggeliga hvila sig; men dina rot vill jag dräpa med hunger, och skall han förgöra dina igenlefda.
Osaukitsitsa adzapeza chakudya ndipo amphawi adzakhala mwamtendere. Koma anthu ako ndidzawawononga ndi njala, ndipo njalayo idzapha ngakhale opulumuka ako.
31 Jämra dig, du port, ropa, du stad, hela Philistea är förtviflad; ty nordanefter kommer en rök, och ingen ensam är uti hans tjäll.
Lirani kwambiri, anthu a pa chipata! Fuwulani kwambiri, anthu a mu mzinda! Njenjemerani ndi mantha, inu Afilisti nonse! Mtambo wa utsi ukuchokera kumpoto, ndipo palibe wamantha pakati pa ankhondo ake.
32 Och hvad varda Hedningarnas båd sägande? Nämliga att Herren hafver grundat Zion, och der skola hans folks elände hafva tillflykt.
Kodi tidzawayankha chiyani amithenga a ku Filisitiya? “Yehova wakhazikitsa Ziyoni, ndipo mu mzinda wakewu, anthu ozunzika apeza populumukira.”

< Jesaja 14 >