< Hosea 12 >

1 Men Ephraim gapar efter väder, och löper efter östanväder, och gör hvar dag mer afguderi och skada; de göra förbund med Assur, och föra balsam uti Egypten;
Efereimu amadya mpweya; tsiku lonse amasaka mphepo ya kummawa ndipo amachulukitsa mabodza ndi chiwawa. Amachita mgwirizano ndi Asiriya ndipo amatumiza mphatso za mafuta a olivi ku Igupto.
2 Derföre skall Herren beskärma Juda, och hemsöka Jacob efter hans vägar, och löna honom efter hans förtjenst.
Yehova akuyimba mlandu Yuda; Iye adzalanga Yakobo molingana ndi makhalidwe ake, adzamulanga molingana ndi ntchito zake.
3 Ja, ( säga de ) han hafver undertryckt sin broder i moderlifvena, och af allo magt kämpat med Gudi.
Akali mʼmimba mwa amayi ake, Yakobo anagwira chidendene cha mʼbale wake; iye atakula analimbana ndi Mulungu.
4 Han kämpade med Ängelen, och vann; ty han gret, och bad honom; der hafver han ju funnit honom i BethEl, och der hafver han talat med oss.
Yakobo analimbana ndi mngelo ndipo anapambana; analira napempha kuti amukomere mtima. Mulungu anakumana naye ku Beteli ndipo anayankhula naye kumeneko,
5 Men Herren är Gud Zebaoth; Herre är hans Namn.
Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Yehova ndiye dzina lake lotchuka!
6 Så omvänd dig nu till din Gud; gör barmhertighet och rätt, och hoppas allstädes uppå din Gud.
Koma inu muyenera kubwerera kwa Mulungu wanu; pitirizani chikondi ndi chiweruzo cholungama, ndipo muzidikira Mulungu wanu nthawi zonse.
7 Men köpmannen hafver en falsk våg i sine hand, och bedrager gerna.
Munthu wamalonda amagwiritsa ntchito masikelo achinyengo; iyeyo amakonda kubera anthu.
8 Ty Ephraim säger: Jag är rik, jag hafver nog; man skall intet ondt finna i allt mitt arbete, det synd är.
Efereimu amadzitama ponena kuti, “Ndine wolemera kwambiri; ndili ndi chuma chambiri. Palibe amene angandiloze chala chifukwa cha kulemera kwanga.”
9 Men jag, Herren, är din Gud, allt ifrå Egypti land, och den dig låter ännu i hyddom bo, såsom man i årstider plägar;
“Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa mu Igupto. Ndidzakukhazikaninso mʼmatenti, monga munkachitira masiku aja pa nthawi ya zikondwerero zanu.
10 Och talar till Propheterna; och jag är den som så många prophetier gifver, och förkunnar genom Propheterna, ho jag är.
Ndinayankhula ndi aneneri, ndinawaonetsa masomphenya ambiri, ndipo ndinawawuza mafanizo kudzera mwa iwo.”
11 Uti Gilead är alltsamman afguderi, och i Gilgal offra de oxar fåfängeliga, och hafva så mång altare, som skylarna på åkren stå.
Kodi Giliyadi ndi woyipa? Anthu ake ndi achabechabe! Kodi amapereka nsembe za ngʼombe zazimuna ku Giligala? Maguwa awo ansembe adzakhala ngati milu ya miyala mʼmunda molimidwa.
12 Jacob miste fly uti Syrie land, och Israel måste tjena för ena hustru; för ena hustru måste han vakta.
Yakobo anathawira ku dziko la Aramu, Israeli anagwira ntchito kuti apeze mkazi, ndipo anaweta nkhosa kuti akwatire mkaziyo.
13 Men derefter förde Herren Israel utur Egypten, genom en Prophet, och lät bevara honom genom en Prophet.
Yehova anagwiritsa ntchito mneneri kuti atulutse Israeli mu Igupto; kudzera mwa mneneriyo Iye anawasamalira.
14 Men nu förtörnar honom Ephraim genom sina afgudar; derföre skall deras blod komma öfver dem, och deras herre skall vedergälla dem deras försmädelse.
Koma Efereimu wamukwiyitsa kwambiri. Nʼchifukwa chake Yehova adzawalanga ndi imfa. Adzawalanga chifukwa anamuchititsa manyazi kwambiri.

< Hosea 12 >