< Haggai 1 >

1 Uti andra årena Konungs Darios, uti sjette månadenom, på första dagen i månadenom, skedde Herrans ord, genom den Propheten Haggai, till Serubbabel, Sealthiels son, Juda Första, och till Jehosua, Jozadaks son, den öfversta Presten, och sade:
Chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo, tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chimodzi, Yehova anapatsa mneneri Hagai uthenga wopita kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, ndiponso kwa mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki:
2 Så säger Herren Zebaoth: Detta folket säger: Tiden är ännu icke kommen, att man Herrans hus bygga skall.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu awa amanena kuti, ‘Nthawi sinafike yoti nʼkumanga Nyumba ya Yehova.’”
3 Och Herrans ord skedde genom den Propheten Haggai sägandes:
Tsono Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti,
4 Månn då edar tid vara kommen, att I bo skolen uti hvälfdom husom, och detta huset måste öde stå?
“Kodi ino ndi nthawi yoti inuyo muzikhala mʼnyumba zomanga bwino, pamene Nyumba yangayi ikanali bwinja?”
5 Nu, så säger Herren Zebaoth: Ser, huru det går eder.
Tsono zimene Yehova Wamphamvuzonse akunena ndi izi, “Ganizirani bwino njira zanu.
6 I sån mycket, och fören litet in; I äten, och varden dock icke mätte; I dricken, och varden dock intet otörstige; I kläden eder, och kunnen dock intet värma eder; och den der penningar förtjenar, han lägger dem uti hålogan pung.
Mwadzala zambiri, koma mwakolola zochepa. Mumadya, koma simukhuta. Mumamwa, koma ludzu lanu silitha. Mumavala, koma simumva kutentha. Mumalandira malipiro, koma ndalama zanu zimatha ngati mwaziyika mʼthumba lobowoka.”
7 Så säger Herren Zebaoth: Ser, huru det går eder.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ganizirani bwino njira zanu.
8 Går upp på berget, och hemter trä, och bygger huset; det skall vara mig tacknämligt och jag skall bevisa mina äro, säger Herren.
Pitani ku mapiri ndipo mukatenge matabwa oti mudzamangire Nyumba yanga, kuti ndikondwere nayo ndi kulandiramo ulemu,” akutero Yehova.
9 Ty I vänten väl efter mycket, och si, det varder litet; och om I än fören det hem, så blås jag dock det bort. Hvi så? säger Herren Zebaoth. Derföre, att mitt hus så öde står, och hvar och en hastar med sino huse;
“Mumayembekezera zambiri, koma taonani mwapeza pangʼono pokha. Zimene munazibweretsa ku nyumba, Ine ndinazimwaza. Nʼchifukwa chiyani?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Chifukwa Nyumba yanga ikanali bwinja, pamene aliyense wa inu watanganidwa kumanga nyumba yake.
10 Derföre hafver himmelen förhållit daggena öfver eder, och jorden sina frukt.
Choncho, chifukwa cha inu, mitambo yaleka kugwetsa mvula ndipo dziko lapansi laleka kutulutsa zomera.
11 Och jag hafver kallat torko, både öfver land och berg, öfver korn, vin, oljo, och öfver allt det utaf jordene kommer; och öfver folk och fä, och öfver allt händers arbete.
Ndabweretsa chilala pa minda ndi pa mapiri, chilala chawumitsa tirigu, mphesa, mafuta a olivi ndi chilichonse chimene chimamera pa nthaka, pa anthu ndi pa ngʼombe, ndi pa ntchito zonse za manja anu.”
12 Då hörde Serubbabel, Sealthiels son, och Jehosua, Jozadaks son, den öfverste Presten, och alle öfverblefne af folket, sådana Herrans, deras Guds, röst, och Prophetens Haggai ord; såsom Herren, deras Gud, honom sändt hade; och folket fruktade sig för Herranom.
Pamenepo Zerubabeli mwana wa Sealatieli, mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki, ndi anthu onse otsala anamvera mawu a Yehova Mulungu wawo ndi uthenga wa Hagai, chifukwa anatumidwa ndi Yehova Mulungu wawo. Ndipo anthuwo anaopa Yehova.
13 Då sade Haggai, Herrans Ängel, som Herrans bådskap hade till folket: Jag är med eder, säger Herren.
Tsono Hagai, mthenga wa Yehova, anapereka kwa anthuwo uthenga uwu wa Yehova: “Ine ndili nanu,” akutero Yehova.
14 Och Herren uppväckte Serubbabels anda, Sealthiels sons, Juda Förstas, och Jehosua anda, Jozadaks sons, dens öfversta Prestens, och allt igenlefda folkens anda; så att de kommo, och arbetade uppå Herrans Zebaoths, deras Guds, hus.
Kotero Yehova anakhudza mtima wa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, mtima wa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndiponso mitima ya anthu onse otsala. Iwo anabwera ndi kuyamba ntchito yomanga Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wawo,
15 På fjerde och tjugonde dagen i sjette månadenom, uti andro årena Konungs Darios;
pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chimodzi, wa chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo.

< Haggai 1 >