< Habackuk 1 >

1 Detta är den tunge, som Propheten Habacuc sett hafver.
Uthenga umene mneneri Habakuku analandira mʼmasomphenya.
2 Herre, huru länge skall jag ropa, och du vill icke höra? Huru länge skall jag ropa till dig för öfvervålds skull, och du vill icke hjelpa?
Kodi inu Yehova, ndidzakhala ndikukupemphani thandizo kwa nthawi yayitali motani, koma wosayankha? Kapena kufuwulira kwa inu kuti, “Chiwawa kuno!” koma wosatipulumutsa?
3 Hvi låter du mig se mödo och arbete? Hvi hafver du låtit mig se rof och öfvervåld? Våld går öfver rätt.
Chifukwa chiyani mukundionetsa zinthu zoyipa? Chifukwa chiyani mukundionetsa mavutowa? Ndikuona chiwonongeko ndi chiwawa; pali ndewu ndi kukangana kwambiri.
4 Derföre måste lagen blifva tillbaka, och ingen rätt kan till ända komma; ty den ogudaktige öfverfaller den rättfärdiga, derföre gå vrånga domar.
Kotero malamulo anu atha mphamvu, ndipo chilungamo sichikugwira ntchito. Anthu oyipa aposa olungama, kotero apotoza chilungamo.
5 Ser ibland Hedningarna; ser till, och förundrer eder ty jag vill något göra i edrom tid, det i icke tro skolen, då man derom talar.
“Yangʼanani pakati pa mitundu ya anthu, ndipo penyetsetsani, ndipo muthedwe nazo nzeru. Pakuti ndidzachitadi zinthu pa nthawi yanu zimene inu simudzazikhulupirira, ngakhale wina atakufotokozerani.
6 Ty si, jag vill uppväcka de Chaldeer, ett bittert och snart folk, hvilket draga skall så vidt som landet är, till att intaga de boningar som icke äro deras.
Pakuti taonani, Ine ndikuwutsa Ababuloni, anthu ankhanza ndiponso amphamvu, amene amapita pa dziko lonse lapansi kukalanda malo amene si awo.
7 Och skall vara grufveligit och förfärligit; och skall bjuda och tvinga såsom det vill.
Iwowa ndi anthu ochititsa mantha, ndipo ndi owopsa; amadzipangira okha malamulo ndi kudzipezera okha ulemu.
8 Deras hästar äro raskare än parder, så äro de ock ilsknare än ulfvar om aftonen; hans resenärer draga med storom hopom fjerranefter, lika som de flögo, såsom örnar hasta sig till ett as.
Akavalo awo ndi aliwiro kwambiri kupambana akambuku ndi owopsa kupambana mimbulu yolusa nthawi ya madzulo. Okwerapo awo akuthamanga molunjika; a pa akavalo awo ndi ochokera kutali, akuwuluka ngati chiwombankhanga chofuna kugwira nyama;
9 De komma allesamman till att göra skada ehvart de vilja; der gå de igenom, lika som ett östan väder, och samka fångar tillhopa, såsom sand.
onse akubwera atakonzekera zachiwawa. Gulu la ankhondo likubwera ngati mphepo ya mʼchipululu ndi kugwira akapolo ochuluka ngati mchenga.
10 De skola bespotta Konungar, och begabba Förstar; all fäste skola vara dem ett skämt; ty de skola göra der blåverk före, och vinna dem.
Akunyoza mafumu ndiponso kuchitira chipongwe olamulira. Akupeputsa mizinda yonse yotetezedwa; akumanga mitumbira ndi kulanda mizindayo.
11 Då skola de taga sig ett nytt mod, fara framåt och synda; och så måste då deras seger höra deras gud till.
Kenaka amasesa mofulumira ngati mphepo nʼkumangopitirirabe, anthu ochimwa, amene mphamvu zawo ndiye mulungu wawo.”
12 Men du Herre, min Gud, min Helige, du som äst af evighet, låt oss icke dö; utan låt dem, Herre, allenast vara oss till ett straff; och låt dem, o vår tröst, allenast tukta oss.
Inu Yehova, kodi sindinu wachikhalire? Mulungu wanga, Woyera wanga, ife sitidzafa. Inu Yehova, munawasankha anthuwo kuti abweretse chiweruzo; Inu Thanthwe, munawayika iwowo kuti atilange.
13 Din ögon äro ren, så att du icke orkar se det onda, och kan icke se uppå jämmer. Hvi ser du då på de öfverträdare, och tiger, att den ogudaktige uppslukar den, som frommare är än han?
Maso anu ndi oyera kwambiri safuna kuona choyipa; Inu simulekerera cholakwa. Chifukwa chiyani nanga mukulekerera anthu ochita zachinyengowa? Chifukwa chiyani muli chete pamene anthu oyipa akuwononga anthu olungama kupambana iwowo?
14 Och låter menniskorna gå, lika som fiskar i hafvet; såsom matkar, de ingen herm hafva?
Mwasandutsa anthu kukhala ngati nsomba zamʼnyanja, ngati zolengedwa zamʼnyanja zimene zilibe wolamulira.
15 De dragat allt med krok, och fuskar med sin nät, och församlat med sin garn; dess fröjda de sig, och äro glade.
Mdani wawo woyipa amakoka anthu onse ndi mbedza, amawakola mu ukonde wake, amawasonkhanitsa mu khoka lake; kotero iyeyo amakondwa ndi kusangalala.
16 Derföre offra de sinom nätom, och röka sinom garnom; efter det deras del är derigenom så fet, och deras mat så kräselig vorden.
Choncho iye amaperekera nsembe ukonde wake ndiponso kufukizira lubani khoka lake, popeza ukonde wakewo ndiye umamubweretsera moyo wapamwamba ndipo amadya chakudya chabwino kwambiri.
17 Derföre kasta de sin nät ännu alltid ut, och vilja icke återvända att dräpa folk.
Kodi iye azipitirabe kugwiritsa ntchito makoka akewo, kuwononga mitundu ya anthu mopanda chifundo?

< Habackuk 1 >