< 1 Mosebok 6 >

1 Då menniskorna begynte förökas på jordene, och födde sig döttrar:
Anthu atayamba kuchuluka pa dziko lapansi ndi kubereka ana aakazi,
2 Då sågo Guds söner menniskornas döttrar, att de voro dägeliga, och togo till hustrur hvilka de helst ville.
ana aamuna a Mulungu anaona kuti ana aakazi a anthuwo anali okongola. Ndipo anakwatira aliyense amene anamusankha.
3 Då sade Herren: Menniskorna vilja icke mer låta min Anda straffa sig, ty de äro kött. Jag vill ännu gifva dem hundrade och tjugu års dag.
Tsono Yehova anati, “Sindilola kuti chipwirikiti chikuchitikachi chipitirire mpaka muyaya, pakuti iye ndi munthu; masiku a moyo wake adzakhala zaka 120.”
4 På den tiden voro ock tyranner på jordene, förty, sedan Guds söner ingingo till menniskors döttrar, och de födde barn, vordo deraf väldige och fast beryktade män i verldene.
Masiku amenewo komanso pambuyo pake, pa dziko lapansi panali Anefili, anthu amphamvu ndiponso otchuka. Anthuwa ndi amene ankabadwa ana a Mulungu aja atakwatira ana aakazi a anthu.
5 Men då Herren såg, att menniskones ondska var stor på jordene, och all hennes hjertas uppsåt och tanke var alltid benägen till det ondt var:
Pamene Yehova anaona kuti kuyipa kwa munthu pa dziko lapansi kunali kwakukulu ndi kuti nthawi zonse amalingalira ndi kukhumbira kuchita zoyipa zokhazokha,
6 Då ångrade Herranom, att han hade gjort menniskona på jordene, och det bekymrade honom i hans hjerta.
Yehova anamva chisoni kuti analenga munthu ndi kumuyika pa dziko lapansi, ndipo anawawidwa mtima.
7 Och Herren sade: Menniskona, som jag skapade, skall jag förgöra utaf jordene, ifrå mennisko allt intill fänaden, och intill matkar, och intill foglarna under himmelen; förty det ångrar mig, att jag dem gjort hafver.
Choncho Yehova anati, “Ndidzafafaniza munthu, nyama, zonse zokwawa, ndi mbalame za mu mlengalenga pa dziko lapansi, pakuti ndikumva chisoni kuti ndinazilenga zimenezi.”
8 Men Noah fann nåde för Herranom.
Koma Yehova anamukomera mtima Nowa.
9 Detta är Noahs slägt: Noah var en from man och fullkomlig, och förde ett gudeligit lefverne i sin tid.
Mbiri ya Nowa inali yotere: Nowa anali munthu wolungama ndi wopanda tchimo pakati pa anthu a mʼbado wake. Ndipo anayenda ndi Mulungu.
10 Och födde tre söner, Sem, Ham, Japhet.
Nowa anabereka ana aamuna atatu: Semu, Hamu ndi Yafeti.
11 Men jorden var förderfvad för Guds åsyn, och full med orätt.
Chiwawa chinadzaza pa dziko lapansi kotero kuti dziko linakhala lowonongeka pamaso pa Mulungu.
12 Då såg Gud på jordena, och si, hon var förderfvad, ty allt kött hade förderfvat sin väg på jordene.
Mulungu atayangʼana, anaona kuti dziko layipadi chifukwa cha makhalidwe oyipa a anthu onse pa dziko lapansi.
13 Då sade Gud till Noah: Allt kötts ändalykt är kommen för mig, ty jorden är full med orätt af dem, och si, jag vill förderfva dem med jordene.
Ndipo Mulungu anati kwa Nowa, “Ndatsimikiza mtima kuti ndiwononge anthu onse, pakuti dziko lapansi ladzaza ndi ntchito zawo zoyipa. Ndithudi ndiwawononga pamodzi ndi zonse za pa dziko.
14 Gör dig en ark utaf furuträ, och gör kamrar derinne, och becka honom utan och innan.
Tsono udzipangire chombo cha matabwa a mtengo wanjale; mʼkati mwake upange zipinda ndipo upake phula mʼkati ndi kunja.
15 Och gör honom alltså: Trehundrade alnar skall vara längden, femtio alnar bredden, och tretio alnar höjden.
Uchipange motere: Chombo chikhale mamita 140 mulitali, mamita 23 mulifupi ndi mamita 13 mu msinkhu wake.
16 Ett fenster skall du göra der ofvan uppå, en aln stort. Dörrena skall du sätta midt på sidone; och skall han hafva tre bottnar, en nederst, den andra midt uti, den tredje öfverst.
Uchipangire denga ndi kuchimaliza ndi zenera la masentimita makumi asanu. Uyike khomo mʼmbali mwa chombocho ndi kupanga zipinda zosanjikana; chapansi, chapakati ndi chapamwamba.
17 Ty si, jag skall låta komma en vattuflod öfver jordena, till att förderfva allt kött, der en lefvande ande uti är, under himmelen, och allt det på jordene är skall förgås.
Ndidzagwetsa mvula ya chigumula pa dziko lapansi kuti ndiwononge zamoyo zonse za pansi pa thambo ndipo chilichonse cha pa dziko lapansi chidzafa.
18 Men med dig vill jag göra ett förbund, och du skall gå in i arken med dina söner, med dine hustru, och med dina söners hustrur.
Koma ndidzachita pangano langa ndi iwe. Iwe, ana ako aamuna, mkazi wako ndi akazi a ana ako nonse mudzalowa mʼchombocho.
19 Och du skall låta komma in i arken allahanda djur af allt kött, ju ett par, mankön och qvinkön, att de måga blifva lefvande när dig.
Iwe udzalowa mʼchombocho ndi zolengedwa zamoyo zonse ziwiriziwiri, chachimuna ndi chachikazi, kuti zisungike ndi moyo pamodzi ndi iwe.
20 Af foglarna efter deras slag, af fänadenom efter sitt slag, och af allahanda kräkande djur på jordene efter deras slag. Af allo desso skall ju ett par ingå till dig, på det att de skola blifva lefvande.
Udzatenga ziwiriziwiri za mitundu yonse ya mbalame, mitundu yonse ya nyama, ndi mitundu yonse ya zokwawa kuti zikhale ndi moyo.
21 Och du skall till dig taga allahanda mat, som man tärer, och skall samka honom till dig, att han varder dig och dem till födo.
Udzatengenso chakudya cha mtundu uliwonse ndi kuchisunga kuti inu ndi nyamazo muzidzadya.”
22 Och Noah gjorde allt det Gud böd honom.
Nowa anachita zonse monga Mulungu anamulamulira.

< 1 Mosebok 6 >

The World is Destroyed by Water
The World is Destroyed by Water