< 1 Mosebok 48 >
1 Derefter vardt Joseph sagdt: Si, din fader är sjuk. Och han tog båda sina söner med sig, Manasse och Ephraim.
Patapita kanthawi Yosefe anawuzidwa kuti, “Abambo ako akudwala.” Choncho anatenga ana ake awiri aja Manase ndi Efereimu ndi kupita nawo kwa Yakobo.
2 Då vardt Jacob sagdt: Si, din son Joseph kommer till dig. Och Israel tog styrko till sig, och satte sig upp i sängene.
Yakobo atawuzidwa kuti, “Mwana wanu Yosefe wabwera,” Israeli anadzilimbitsa nadzuka kukhala tsonga pa bedi pake.
3 Och sade till Joseph: Den allsmägtige Gud syntes mig i Lus i Canaans land, och välsignade mig,
Yakobo anati kwa Yosefe, “Mulungu Wamphamvuzonse anandionekera ku Luzi mʼdziko la Kanaani, ndipo anandidalitsa,
4 Och sade till mig: Si, jag skall låta dig växa och förökas, och göra dig till mycket folk, och skall gifva dine säd efter dig detta landet till egendom evinnerliga.
nati kwa ine, ‘Ndidzakupatsa ana ambiri ndipo zidzukulu zako zidzasanduka mitundu yambiri ya anthu. Ndidzapereka dziko ili kwa zidzukulu zako zobwera pambuyo pako kuti likhale lawo mpaka muyaya.’
5 Så skola nu dine två söner, Ephraim och Manasse, som dig i Egypten födde äro, förra än jag kom hit in till dig, vara mine, lika som Ruben och Simeon.
“Tsopano ana ako aamuna awiri amene anabadwa ine ndisanabwere kuno adzakhala ana anga. Efereimu ndi Manase adzakhala anga monga mmene alili Rubeni ndi Simeoni.
6 Men de, som du föder efter dem, skola vara dine: men desse skola vara nämnde med deras bröders namn i deras arfvedel.
Koma amene ati adzabadwe pambuyo pa iwowa adzakhala ako ndipo cholowa chawo chidzadziwika ndi mayina a abale awo.
7 Och då jag kom utaf Mesopotamien, dödde mig Rachel i Canaans lande på vägenom, då ännu ett litet stycke vägs var till Ephrath; Och jag begrof henne på vägenom till Ephrath, det nu heter BethLehem.
Pamene ndimabwerera kuchoka ku Parani, mwachisoni Rakele, amayi ako anamwalira mʼdziko la Kanaani, tikanali mʼnjira, mtunda wokafika ku Efurata ukanalipo. Ndipo ndinawayika kumeneko mʼmphepete mwa msewu wa ku Efurata” (amene ndi Betelehemu).
8 Och Israel såg Josephs söner, och sade: Ho äro desse?
Israeli ataona ana a Yosefe anafunsa kuti, “Anyamatawa ndi a yani?”
9 Joseph svarade sinom fader: Det äro mine söner, som Gud hafver mig här gifvit. Han sade: Haf dem hit till mig, att jag välsignar dem.
Yosefe anati kwa abambo ake, “Awa ndi ana anga amene Mulungu wandipatsa kuno.” Ndipo Israeli anati, “Bwera nawo kuno kuti ndiwadalitse.”
10 Ty Israels ögon voro mörk vorden för ålders skull, och kunde icke väl se. Och han hade dem till honom: Och han kysste dem, och tog dem i famn.
Koma maso a Israeli anali ofowoka chifukwa cha kukalamba moti sankaona nʼkomwe. Tsono Yosefe anabwera nawo ana ake aja pafupi ndi abambo ake ndipo abambo ake anawapsompsona nawakumbatira.
11 Och sade till Joseph: Si, jag hafver sett ditt ansigte, det jag icke förmodat hade: Och si, Gud hafver ock låtit mig se dina säd.
Israeli anati kwa Yosefe, “Ine sindinali kuyembekeza kuti nʼkudzaonanso nkhope yako, ndipo tsopano Mulungu wandilola kuti ndionenso ngakhale ana ako.”
12 Och Joseph tog dem utaf hans sköte, och han böjde sig ned på jordena för hans ansigte.
Tsono Yosefe anawachotsa ana aja pa mawondo a Israeli ndipo anamuweramira nkhope pansi.
13 Då tog Joseph dem båda, Ephraim i sin högra hand, emot Israels venstra hand, och Manasse i sina venstra hand, emot Israels högra hand, och dem till honom.
Yosefe anawagwira ana onse awiri padzanja, Efereimu ku dzanja lake lamanja kulunjika dzanja lamanzere la Israeli ndipo Manase ku dzanja lamanzere kulunjikitsa dzanja lamanja la Israeli, ndipo anawayandikiza kwa Yakobo.
14 Men Israel räckte ut sina högra hand, och lade henne på Ephraims dens yngstes hufvud, och sina venstra hand på Manasse hufvud, och omskifte händerna med vilja; ty Manasse var den förstfödde.
Koma Israeli anapinganitsa mikono motero kuti anayika dzanja lake lamanja pamutu pa Efereimu ngakhale kuti iyeyo anali wamngʼono ndi dzanja lake lakumanzere analisanjika pamutu pa Manase ngakhale kuti iyeyu ndiye anali mwana woyamba.
15 Och han välsignade Joseph, och sade: Gud, för hvilkom mine fäder Abraham och Isaac vandrat hafva; Gud, som mig födt hafver utaf min ungdom allt intill denna dag.
Kenaka anadalitsa Yosefe nati, “Mulungu amene makolo anga Abrahamu ndi Isake anamutumikira, Mulungu amene wakhala ali mʼbusa wanga moyo wanga wonse kufikira lero,
16 Ängelen, som mig frälst hafver af allo ondo, han välsigne dessa piltarna, att de må efter mitt, och mina fäders, Abrahams och Isaacs, namn nämnde varda, så att de må växa och förökas på jordene.
mngelo amene wandipulumutsa ine ku zovuta zonse, ameneyo adalitse anyamata awa. Kudzera mwa iwowa dzina langa ndi mayina a makolo anga, Abrahamu ndi Isake, adzamveka. Iwowa adzakhala ndi ana ambiri nadzasanduka mtundu waukulu pa dziko lapansi.”
17 Men då Joseph såg, att hans fader lade sina högra hand på Ephraims hufvud, behagade det honom illa, och fattade uti sins faders hand, att han skulle vända sina hand af Ephraims hufvud in på Manasse hufvud;
Yosefe ataona kuti abambo ake ayika dzanja lamanja pa Efereimu, sanakondwere. Choncho anagwira dzanja la abambo ake kuti alichotse pamutu pa Efereimu ndi kuliyika pamutu pa Manase,
18 Och sade till honom: Icke så, min fader; denne är den förstfödde, lägg dina högra hand på hans hufvud.
nati kwa abambo ake, “Ayi, abambo anga, uyu ndiye woyamba kubadwa, ikani dzanja lanu lamanja pamutu pake.”
19 Men hans fader nekade det, och sade: Jag vet väl, min son, jag vet det väl; denne skall ock varda till folk, och skall varda stor, men hans yngre broder skall varda större än han, och hans säd skall varda till ett stort folk.
Koma abambo ake anakana nati, “Ndikudziwa, mwana wanga, ndikudziwa. Adzukulu a iyeyunso adzakhala mtundu waukulu. Komabe mʼbale wake wamngʼonoyu adzakhala wamkulu kuposa iye, ndipo zidzukulu zake zidzakhala mitundu yayikulu ya anthu.”
20 Så välsignade han dem i den dagen och sade: Varde Israel välsignad efter ditt sätt, så att man må säga: Gud sätte dig såsom Ephraim och Manasse: Och så satte han Ephraim för Manasse.
Tsono iye anawadalitsa tsiku limenelo nati, “Aisraeli adzagwiritsa ntchito dzina lanu podalitsa nadzati: Mulungu akudalitseni monga Efereimu ndi Manase.” Choncho anayika Efereimu patsogolo pa Manase.
21 Och Israel sade till Joseph: Si, jag dör, och Gud skall vara med eder, och skall föra eder åter i edra fäders land.
Kenaka Israeli anati kwa Yosefe, “Ine ndatsala pangʼono kufa, koma Mulungu adzakhala ndipo adzakutenganinso kubwerera nanu ku dziko la makolo anu.
22 Jag hafver gifvit dig ett stycke land utan dina bröder, som jag med mitt svärd och båga utaf de Amoreers hand tagit hafver.
Ndiponso iwe wekha ndikupatsa moposera abale ako, malo woonjezera, Sekemu, malo amene ndinalanda kwa Aamori ndi lupanga ndi uta wanga.”