< 1 Mosebok 30 >

1 Då Rachel såg, att hon födde Jacob intet, afundades hon vid sina syster, och sade till Jacob: Skaffa mig ock barn, eljest dör jag.
Rakele ataona kuti sakumuberekera Yakobo ana, anayamba kumuchitira nsanje mʼbale wake. Choncho anati kwa Yakobo, “Undipatse ana kapena apo ayi ndingofa!”
2 Jacob vardt ganska vred på Rachel, och sade: Icke är jag Gud, som dig förmenar dins lifs frukt?
Yakobo anapsera mtima Rakele ndipo nati, “Kodi ine ndalowa mʼmalo mwa Mulungu amene wakulepheretsa iwe kukhala ndi ana?”
3 Men hon sade: Si, der är min tjenstepiga Bilha: lägg dig när henne, att hon må föda i mitt sköt, och jag varder dock uppbyggd genom henne.
Pamenepo Rakele anati kwa Yakobo, “Mdzakazi wanga Biliha nayu. Lowana naye kuti mwina nʼkundibalira mwana, ndipo kudzera mwa iyeyu nanenso nʼkukhala ndi ana.”
4 Och gaf honom så Bilha, sina tjenstepigo, till hustru, och Jacob lade sig när henne.
Ndipo anamupatsa Yakobo wantchito wake Biliha kuti alowane naye. Choncho Yakobo analowana ndi Biliha,
5 Och så vardt Bilha hafvande, och födde Jacob en son.
ndipo Bilihayo anatenga pathupi namubalira Yakobo mwana wamwamuna.
6 Då sade Rachel: Gud hafver dömt mina sak, och hört mina röst, och gifvit mig en son: Derföre kallade hon honom Dan.
Pamenepo Rakele anati, “Mulungu waweruza mondikomera mtima, wamva kupempha kwanga ndipo wandipatsa mwana wa mwamuna.” Choncho anamutcha Dani.
7 Åter vardt Bilha, Rachels tjensteqvinna, hafvande, och födde Jacob den andra sonen.
Biliha, wantchito wa Rakele, anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri.
8 Då sade Rachel: Gud hafver omvändt det med mig och mine syster, och jag får öfverhandena: Och hon kallade honom Naphthali.
Pamenepo Rakele anati, “Ndakhala ndikulimbana kwambiri ndi mʼbale wanga ndipo ndapambana.” Choncho anamutcha Nafutali.
9 Då nu Lea såg, att hon hade vändt igen att föda, tog hon sina tjenstepigo Silpa, och gaf henne Jacob till hustru.
Pamene Leya anaona kuti waleka kubereka ana, iye anatenga wantchito wake Zilipa namupereka kwa Yakobo kuti alowane naye.
10 Så födde Silpa, Leas tjensteqvinna, Jacob en son.
Zilipa, wantchito wa Leya, anaberekera Yakobo mwana wamwamuna.
11 Då sade Lea: Rustig; och kallade honom Gad.
Pamenepo Leya anati, “Mwayi wangawo!” Choncho anamutcha Gadi.
12 Derefter födde Silpa, Leas tjensteqvinna, Jacob den andra sonen.
Zilipa, wantchito wa Leya anamubalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri.
13 Då sade Lea: Väl mig; förty döttrarna skola säga mig saliga: Och hon kallade honom Asser.
Pamenepo Leya anati, “Ndakondwa bwanji! Amayi adzanditcha ine wokondwa.” Choncho anamutcha Aseri.
14 Ruben gick ut om hveteandena, och fann liljor på markene, och hade dem hem till sina moder Lea. Då sade Rachel till Lea: Gif mig en del af din sons liljor.
Pa nthawi yokolola tirigu, Rubeni anapita ku munda ndipo anapezako zipatso za mankhwala wobereketsa. Tsono anatengerako mayi wake Leya. Rakele anati kwa Leya, “Chonde patseko mankhwala wakupezera mwana wakowo.”
15 Hon svarade: Hafver du icke nog, att du hafver tagit min man bort, och vill desslikes taga min sons liljor? Rachel sade: Nu väl, låt honom denna nattena sofva när dig, för dins sons liljor.
Koma iye anati kwa Rakele, “Kodi sizinakukwanire kulanda mwamuna wanga? Ukuti utengenso mankhwala a mwana wangawa.” Iye anati, “Chabwino, agone ndi iwe usiku uno kuti tisinthane ndi mankhwala a mwana wakowo.”
16 Då nu Jacob kom om aftonen af markene, gick Lea ut emot honom, och sade: När mig skall du ligga; förty jag hafver köpt dig för mins sons liljor: Och han låg när henne de nattena.
Choncho pamene Yakobo ankabwera kuchokera ku munda madzulo, Leya anapita kukakumana naye nati, “Lero mukagona ku nyumba chifukwa ndakubwerekani ndi mankhwala wobereketsa a mwana wanga.” Choncho usiku umenewo Yakobo anakalowa kwa Leya.
17 Och Gud hörde Lea, och hon vardt hafvande, och födde Jacob den femte sonen.
Mulungu anamva pemphero la Leya ndipo anatenga pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu.
18 Och sade: Gud hafver lönt mig, för det jag gaf minom manne mina tjenstepigo; och hon kallade honom Isaschar.
Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphotho chifukwa chopereka wantchito wanga kwa mwamuna wanga.” Choncho anamutcha Isakara.
19 Åter vardt Lea hafvande, och födde Jacob den sjette sonen.
Leya anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu ndi chimodzi.
20 Och sade: Gud hafver väl försett mig: Nu varder åter min man boendes när mig, ty jag hafver födt honom sex söner: Och kallade honom Sebulon.
Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphatso yapamwamba. Tsopano mwamuna wanga adzandilemekeza chifukwa ndamubalira ana aamuna asanu ndi mmodzi.” Choncho anamutcha Zebuloni.
21 Derefter födde hon ena dotter, och kallade henne Dina.
Patapita nthawi Leya anabereka mwana wamkazi ndipo anamutcha Dina.
22 Men Gud tänkte på Rachel, och hörde henne, och gjorde henne fruktsamma.
Kenaka, Mulungu anakumbukira Rakele namva pemphero lake ndi kulola kuti akhale ndi mwana.
23 Då vardt hon hafvande, och födde en son, och sade: Gud hafver min smälek ifrå mig tagit.
Rakele anatenga pathupi nabala mwana wamwamuna ndipo anati, “Mulungu wandichotsera manyazi anga.”
24 Och kallade honom Joseph, och sade: Herren gifve mig ännu en son härtill.
Iye anamutcha mwanayo Yosefe, ndipo anati, “Mulungu andipatsenso mwana wina.”
25 Då nu Rachel hade födt Joseph, sade Jacob till Laban: Låt mig färdas, och resa hem till mitt, och i mitt land.
Rakele atabereka Yosefe, Yakobo anati kwa Labani, “Ndimasuleni kuti ndizipita ku dziko la kwathu.
26 Gif mig mina hustrur och min barn, som jag hafver tjent dig före, att jag må färdas; förty du vetst, hvad jag hafver gjort dig för en tjenst.
Patseni akazi anga ndi ana anga, amene ndinakugwirirani ntchito, ndipo ndidzanyamuka ulendo. Inu mukudziwa ntchito imene ndakugwirirani.”
27 Laban sade till honom: Kan jag icke finna nåd för din ögon? Jag förnimmer, att Herren hafver välsignat mig för dina skull.
Koma Labani anati kwa iye, “Chonde, ngati mungandikomere mtima musapite chifukwa ndadziwa kudzera mwa kuwombeza kwanga kuti Yehova wandidalitsa chifukwa cha inu.”
28 Säg, hvad lön jag skall gifva dig?
Anapitiriza kunena kuti, “Tchula malipiro ako ndipo ndidzakupatsa.”
29 Men han sade till honom: Du vetst, huru jag hafver tjent dig, och hvad boskap du hafver under mig.
Koma Yakobo anati kwa iye, “Inu mukudziwa mmene ine ndakugwirirani ntchito ndi mmene ziweto zanu zaswanira pamene ine ndimazisamalira.
30 Du hade litet, förra än jag kom, men nu äst du riker vorden; och Herren hafver välsignat dig för mina skull: Och nu, när skall jag ock något bestyra till mitt hus?
Poyamba munali nazo zochepa ine ndisanabwere, koma tsopano zachuluka. Yehova wakudalitsani chifukwa cha ine. Ndi nthawi tsopano kuti nane ndisamalire banja langa.”
31 Laban sade: Hvad skall jag då gifva dig? Jacob sade: Du skall allsintet gifva mig; utan om du vill göra mig det jag säger, så skall jag ännu beta och vakta din får.
Labani anafunsa, “Ndikupatse chiyani?” Yakobo anayankha, “Musandipatse kanthu. Koma mungondichitira izi ndipo ndidzapitiriza kusamalira nkhosa zanu ndi kuziyangʼanira:
32 Jag vill i dag gå igenom alla dina hjordar, och skilj du derifrån all fläckot och brokot får, och all svart får ibland lamben och kiden: Hvad nu sedan brokot och fläckot blifver, det skall vara min lön.
Mundilole ndiyendeyende pakati pa ziweto zanu lero ndi kuchotsamo mwana wankhosa wamkazi aliyense wakuda, mbuzi iliyonse yamathothomathotho ndi yamawangamawanga. Zimenezi ndiye zikhale malipiro anga.
33 Så varder mig min rättfärdighet betygandes i dag eller morgon, när dertill kommer, att jag skall taga min lön af dig, alltså, att hvad som icke fläckot eller brokot, eller ock hvad svart är ibland lamben och kiden, det vare en tjufnad med mig.
Ndipo chilungamo changa chidzaoneka mʼtsogolo, pamene inu mudzabwere kudzaona malipiro angawo. Ngati mudzapeza mbuzi mʼgulu langa imene si yamawangamawanga, kapena mwana wankhosa wamkazi amene si wakuda ndiye kuti zimenezo zidzakhala kuti ndinakuberani.”
34 Då sade Laban: Jag är till frids, blifve som sagt hafver.
Labani anati, “Ndavomera, zikhale monga mmene wayankhuliramu.”
35 Och han skilde i den dagen ut spräcklota och brokota bockar, och all fläckot och brokot kid, der som ju något hvitt var uppå, och allt det svart var ibland lamben; och fick det sin barn i händer.
Tsiku lomwelo Labani anachotsa atonde onse ndi mbuzi zazikazi zonse zimene zinali ndi mawangamawanga kapena zamathothomathotho, ndiponso zonse zabanga loyera. Anachotsa ana onse ankhosa aakazi akuda, napereka ziweto zonsezi kwa ana ake aamuna kuti aziweta.
36 Och lät blifva tre dagsleder långe emellan sig och Jacob. Så bette Jacob det öfver var af Labans hjord.
Kenaka Labani anayenda mtunda wa masiku atatu kutalikirana ndi Yakobo koma Yakobo anapitiriza kuweta nkhosa zina zonse za Labani.
37 Men Jacob tog gröna aspekäppar, hassel och castaneen, och barkade hvita ränder deruppå;
Tsono Yakobo anatenga nthambi zaziwisi za mitengo ya mkundi, alimoni ndi puleni nazisenda kuchotsa makungwa ake mpaka mtengo woyera wamʼkati kuonekera.
38 Och lade käpparna, som han barkat hade, i dryckehoar för hjordarna, som der komma måste och vattnas, att de skulle hafvande varda, när de kommo till att dricka.
Atatero anayika nthambi zija mʼmagome omwera madzi molunjika ziweto zija kuti pakumwa madziwo ziweto zazikazi ziziyangʼana nthambi zija popeza kuti pakumwa madzi ziweto zija zinkakwerana.
39 Alltså vordo hjordarne hafvande öfver käpparna, och födde fläckot, spräcklot och brokot.
Ndiye kuti nkhosa zija zinkatenga mawere pakumwa madzi molunjika nthambi zija, ndipo zinkaswa ana a mawangamawanga kapena a mathothomathotho.
40 Då afskiljde Jacob lamben, det icke brokot, och allt det svart var, och lät dem in till Labans hjord, och gjorde sig en egen hjord, den lät han icke till Labans hjord.
Yakobo anayika padera ana a ziweto zija. Koma ziweto zina anaziyika kuti ziyangʼanane ndi za Labani, zimene zinali za mawangamawanga ndi zakuda. Motero anapeza ziweto zakezake, ndipo sanazisakanize ndi za Labani.
41 Men när den tidfödde hjorden lopp, lade han käpparna i hoar för hjordens ögon, så att de vordo hafvande öfver käpparna.
Yakobo ankayika nthambi zija momwera madzi pamene ziweto zamphamvu zazikazi zinkakweredwa pofuna kuti zitenge mawere pakumwa madzi moyangʼanana ndi nthambi zija.
42 Men när de senfödda lupo, lade han dem intet deruti. Så vordo då de senfödlingar Labans och de tidfödlingar Jacobs.
Koma sankayika nthambizo pamene ziweto zofowoka zazikazi zinkakweredwa pakumwa madzi. Choncho ziweto zofowoka zonse zinakhala za Labani, ndi ziweto zamphamvu zinakhala za Yakobo.
43 Deraf vardt mannen öfvermåttan riker, så att han hade mycken får, tjenarinnor och tjenare, camelar och åsnar.
Mwa njira imeneyi, Yakobo analemera kwambiri ndipo anali ndi ziweto zochuluka kwambiri, antchito aakazi ndi aamuna, ngamira ndi abulu.

< 1 Mosebok 30 >