< 1 Mosebok 29 >

1 Då hof Jacob sin fot upp, och gick in i det land, som öster ut ligger.
Yakobo anapitiriza ulendo wake kupita ku dziko la anthu a kummawa.
2 Och såg sig om, och si, der var en brunn på markene; och si, tre hjordar med får der när; förty hjordarne måste dricka af brunnenom; och låg en stor sten för hålet på brunnenom.
Atafika kumeneko anaona chitsime ku busa ndipo panali magulu atatu a nkhosa zitagona pafupi ndi chitsimecho chifukwa nkhosazo zimamwetsedwa madzi ochokera mʼchitsimecho. Pamwamba pa chitsimecho panali mwala waukulu.
3 Och de plägade der församla alla hjordarna, och vältra stenen ifrå brunnshålet, och vattna fåren, och lade så åter stenen för hålet i sitt rum igen.
Amati nkhosa zonse zikasonkhana, abusawo ankagudubuza mwalawo, kuwuchotsa ndi kumwetsa madzi nkhosazo. Kenaka ankawubwezera mwalawo pamalo pake, pakamwa pa chitsimepo.
4 Och Jacob sade till dem: Mine bröder, hvadan ären I? De svarade: Vi äre af Haran.
Yakobo anafunsa abusawo kuti, “Abale anga, mwachokera kuti?” Iwo anayankha, “Tachokera ku Harani.”
5 Han sade till dem: Kännen I ock Laban Nahors son? De svarade: Vi känne honom väl.
Iye anawafunsanso kuti, “Kodi Labani, mdzukulu wa Nahori mukumudziwa?” Iwo anayankha, “Inde tikumudziwa?”
6 Han sade: Går honom ock väl i hand? De svarade: Honom går väl i hand: Och si, der kommer hans dotter Rachel med fåren.
Ndipo Yakobo anawafunsanso, “Kodi ali bwino?” Iwo anati, “Inde ali bwino. Nayu Rakele mwana wake akubwera apoyu ndi nkhosa.”
7 Han sade: Det är ännu bittida dags, och är icke ännu tid drifva boskapen hem; vattner fåren, och går bort med dem i bet.
Iye anati, “Taonani, dzuwa likanalipo ndipo nthawi yosonkhanitsa nkhosa sinakwane. Bwanji osazimwetsa madzi nkhosazi.”
8 De svarade: Vi kunne icke, förra än du alle hjordarne komma tillsamman, och vi vältre stenen ifrå brunnshålet, och vattne så fåren.
Iwo anayankha, “Ayi sitingatero. Tidikira mpaka nkhosa zonse zisonkhane. Zikatero, tigubuduza mwalawu kuwuchotsa pamwamba pa chitsimepo, kenaka nʼkuzimwetsa madzi nkhosazo.”
9 Medan han ännu talade med dem, kom Rachel med sins faders får; förty hon vaktade fåren.
Ali chiyankhulire nawo, Rakele anafika ndi nkhosa za abambo ake popeza ndiye amene ankaweta nkhosazo.
10 Då Jacob såg Rachel, Labans sins moderbroders dotter, och Labans sins moderbroders får, gick han till, och vältrade stenen ifrå hålet på brunnenom, och vattnade Labans sins moderbroders får.
Yakobo ataona Rakele mwana wa Labani, mlongo wa amayi ake, ali ndi nkhosa za Labani, anapita nawugudubuza mwala uja nazimwetsa madzi nkhosa za amalume akezo.
11 Och kysste Rachel; hof upp sina röst, och gret.
Kenaka Yakobo anapsompsona Rakele nayamba kulira mokweza.
12 Och kungjorde henne, att han var hennes faderbroders och Rebeckas son. Då lopp hon, och kungjorde det sinom fader.
Kenaka Yakobo anawuza Rakele kuti iye ndi mwana wa Rebeka, mlongo wa abambo a Rakele uja. Choncho Rakele anathamanga nakawuza abambo ake.
13 Då nu Laban hörde om Jacob sin systerson, lopp han emot honom, och tog honom i famn, och kyssten, och hade honom in i sitt hus. Då förtäljde han honom allt, huru tillgått var.
Labani atamva za Yakobo, mwana wa mlongo wake, anafulumira kukakumana naye. Anamukupatira napsompsona, napita naye ku nyumba kwake. Yakobo anafotokozera Labani zonse zinachitika.
14 Då sade Laban till honom: Nu väl, du äst mitt ben och mitt kött: Och när han nu en månad långt hade varit när honom,
Ndipo, Labani anati kwa iye, “Iwe ndiwe ndithu fupa ndi mnofu wanga.” Yakobo anakhala ndi Labani mwezi umodzi.
15 Sade Laban till Jacob: Ändock du äst min broder, skulle du fördenskull tjena mig för intet? Säg, hvad skall vara din lön?
Tsono Labani anawuza Yakobo kuti, “Zoona iwe ndi ife ndi abale. Koma suyenera kundigwirira ntchito popanda malipiro. Ndiwuze kuti malipiro ako azikhala wotani?”
16 Och Laban hade två döttrar; den äldsta het Lea, och den yngsta het Rachel.
Tsono Labani anali ndi ana aakazi awiri; dzina la wamkulu linali Leya, ndipo dzina la wamngʼono linali Rakele.
17 Men Lea var klenögd; Rachel var väl skapad, och hade ett dägeligit ansigte.
Leya anali ndi maonekedwe wofowoka koma Rakele anali wa maonekedwe wokongola kwambiri.
18 Till henne fick Jacob kärlek, och sade: Jag vill tjena dig i sju år för Rachel dina yngsta dotter.
Yakobo anakonda Rakele ndipo anati, “Ndidzakugwirirani ntchito kwa zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha mwana wanu wamngʼono, Rakele.”
19 Laban svarade: Det är bättre jag gifver dig henne, än enom androm; blif när mig.
Labani anati, “Kuli bwino kuti ndimupereke kwa iwe ameneyu kusiyana ndi munthu wina. Khala ndi ine kuno.”
20 Så tjente Jacob i sju år för Rachel; och tyckte honom det vara få dagar, så kär hade han henne.
Choncho Yakobo anagwira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele. Koma kwa iye zaka zonsezi zinakhala ngati masiku wochepa chifukwa anamukonda Rakele.
21 Och Jacob sade till Laban: Få mig mina hustru; ty nu är tid, att jag kommer i säng med henne.
Kenaka Yakobo anati kwa Labani, “Nthawi yanga ndakwanitsa, ndipatseni mwana wanu kuti ndimukwatire.”
22 Då böd Laban allt folket der omkring, och gjorde bröllop.
Pamenepo Labani anakonza phwando la ukwati, nayitana anthu onse a pamalopo.
23 Men om aftonen tog han Lea sina dotter, och hade henne in till honom: Och han låg när henne.
Koma pokwana usiku, Labani anatenga mwana wake wamkazi Leya namupatsa Yakobo, ndipo Yakobo anagona naye.
24 Och Laban fick sine dotter Lea Silpa till ena tjenstepigo.
Ndipo Labani anapereka wantchito wake wamkazi Zilipa kwa Leya kuti akhale wantchito wake.
25 Om morgonen, si, då var det Lea: Och han sade till Laban: Hvi hafver du det gjort mig? Hafver jag icke tjent dig för Rachel? Hvi hafver du bedragit mig?
Pakucha mmawa, Yakobo anaona kuti anagona ndi Leya. Choncho Yakobo anafunsa Labani, “Nʼchiyani mwandichitirachi? Kodi ine sindinakugwirireni ntchito chifukwa cha Rakele? Bwanji mwandinyenga?”
26 Laban svarade: Man gör icke så i våro lande, att man gifver ut den yngsta förr än den äldsta.
Labani anayankha, “Si mwambo wathu kuno kupereka wamngʼono ku banja, wamkulu asanakwatiwe.
27 Håll dessa veckona ut, så vill jag ock gifva dig denna med, för den tjenst, som du ännu skall tjena mig i androm sju år.
Yamba watsiriza sabata ya chikondwerero cha ukwati wa Leya; kenaka ndidzakupatsanso Rakele. Koma udzayenera kundigwirira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri.”
28 Jacob gjorde så, och höll de veckona ut; då gaf han honom Rachel sina dotter till hustru.
Yakobo anachitadi momwemo. Anamaliza sabata ya chikondwerero cha Leya, ndipo Labani anamupatsa Rakele kuti akhale mkazi wake.
29 Och Laban gaf Rachel sine dotter Bilha till ena tjenstepigo.
Labani anapereka wantchito wake wamkazi Biliha kwa Rakele kuti akhale wantchito wake.
30 Så låg han ock när Rachel, och hade Rachel kärare än Lea; och tjente honom framdeles i de andra sju åren.
Yakobo analowana ndi mkazi wake Rakele, ndipo Yakobo anakonda Rakele kuposa Leya. Ndipo anamugwirira ntchito Labani zaka zina zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele.
31 Men då Herren såg, att Lea vardt vanvörd, gjorde han henne fruktsamma, och Rachel ofruktsamma.
Pamene Mulungu anaona kuti Yakobo sankamukonda Leya kwambiri, Iye analola kuti Leya uja akhale ndi ana, ndi kuti Rakele akhale wosabala.
32 Och Lea vardt hafvande, och födde en son, den kallade hon Ruben, och sade: Herren hafver sett till min förtryckelse; nu varder min man hafvandes mig kär.
Leya anakhala ndi pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha Rubeni pakuti anati, “Yehova waona kusauka kwanga. Zoonadi, mwamuna wanga adzandikonda tsopano.”
33 Och vardt åter hafvande, och födde en son, och sade: Herren hafver hört, att jag är vanvörd, och hafver desslikes denna gifvit mig; och kallade honom Simeon.
Anakhalanso ndi pathupi ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Yehova anamva kuti mwamuna wanga sakundikonda, choncho wandipatsanso mwana winayu.” Ndipo anamutcha dzina lake Simeoni.
34 Åter vardt hon hafvande, och födde en son, och sade: Nu varder min man åter hållandes sig till mig, ty jag hafver födt honom tre söner; derföre kallade hon honom Levi.
Anatenganso pathupi kachitatu, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Pano pokha tidzaphatikana kwambiri ndi mwamuna wanga, chifukwa ndamubalira ana aamuna atatu.” Kotero anamutcha dzina lake Levi.
35 Fjerde reso vardt hon hafvande, och födde en son, och sade: Nu vill jag tacka Herranom; derföre kallade hon honom Juda, och vände så igen att föda.
Anatenganso pathupi pena, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna, iye anati, “Nthawi ino ndidzalemekeza Yehova.” Choncho anamutcha Yuda. Kenaka analeka kubereka.

< 1 Mosebok 29 >