< 1 Mosebok 21 >

1 Och Herren sökte Sara, såsom han sagt hade, och Herren gjorde med henne såsom han talat hade.
Yehova anakomera mtima Sara monga ananenera, ndipo Yehovayo anachita monga momwe analonjezera.
2 Och Sara vardt hafvande, och födde Abraham en son i sinom ålderdom, vid den tiden, som Gud honom föresagt hade.
Sara anakhala ndi pathupi ndipo anamuberekera Abrahamu mwana wamwamuna mu ukalamba wake, pa nyengo imene Mulungu anamulonjeza.
3 Och Abraham nämnde sin son, som honom född var, Isaac, den honom Sara födt hade.
Abrahamu anapereka dzina loti Isake kwa mwana wamwamuna amene Sara anamuberekera.
4 Och omskar honom på åttonde dagen, som Gud honom budit hade.
Isake atakwanitsa masiku asanu ndi atatu, Abrahamu anamuchita mdulidwe monga Mulungu anamulamulira.
5 Hundrade år gammal var Abraham, då honom hans son Isaac födder var.
Abrahamu anali ndi 100 pamene mwana wake Isake anabadwa.
6 Och Sara sade: Gud hafver gjort mig ett löje; ty hvilken det får höra, han får le åt mig.
Sara anati, “Mulungu wandibweretsera mseko, ndipo aliyense amene adzamva zimenezi adzaseka nane pamodzi.”
7 Och sade ytterligare: Ho torde ock säga Abraham sjelfvom, att Sara däggde barn, och hade födt honom en son i sinom ålderdom?
Ndipo anawonjezera kuti, “Ndani akanamuwuza Abrahamu kuti Sara nʼkudzayamwitsako ana? Chonsecho ndamubalira mwana wamwamuna kuwukalamba wake.”
8 Och barnet växte, och vardt afvandt. Och Abraham gjorde ett stort gästabud den dagen, då Isaac afvandes.
Mwana uja anakula mpaka kumuletsa kuyamwa. Tsiku lomuletsa Isake kuyamwa, Abrahamu anakonza phwando lalikulu.
9 Och Sara fick se den Egyptiska qvinnones Hagars son, den hon Abraham födt hade, att han var en bespottare.
Koma Sara anaona kuti mwana wamwamuna amene Hagara Mwigupto anamuberekera Abrahamu amamuseka,
10 Och sade till Abraham: Drif denna tjensteqvinnona ut med hennes son; ty denne tjensteqvinnones son skall icke ärfva med min son Isaac.
ndipo anati kwa Abrahamu, “Muchotse mdzakazi ndi mwana wake wamwamunayu, pakuti mwana wa kapolo sadzagawana chuma ndi mwana wanga Isake.”
11 Detta ordet behagade Abraham ganska illa för sin sons skull.
Nkhaniyi inamumvetsa chisoni kwambiri Abrahamu chifukwa imakhudza mwana wake.
12 Men Gud sade till honom: Låt dig icke tycka hårdt vara om pilten och tjensteqvinnone; allt det Sara dig sagt hafver, så lyd henne; förty i Isaac skall säden dig nämnd varda.
Koma Mulungu anamuwuza Abrahamu kuti, “Usamve chisoni motero ndi mnyamatayu ndi mdzakazi wakoyu. Mvetsera chilichonse chomwe Sara akukuwuza, chifukwa zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake.
13 Jag skall ock göra tjensteqvinnones son till folk, derföre att han din säd är.
Mwana wa mdzakazi wakoyu ndidzamusandutsa mtundu wa anthu chifukwa ndi mwana wako.”
14 Då stod Abraham bittida upp om morgonen, och tog bröd och en flaska med vatten, och lade på Hagars rygg, och pilten med, och lät gå henne. Hon gick sin väg, och for vill i öknene, vid BerSaba.
Mmamawa wake, Abrahamu anatenga chakudya ndi botolo la madzi nazipereka kwa Hagara. Anasenzetsa Hagara nawaperekeza pangʼono ndi mnyamatayo. Hagara ananyamuka nayendayenda mʼchipululu cha Beeriseba.
15 Då nu vattnet i flaskone var förtärdt, kastade hon pilten under en buska.
Madzi atatha mʼbotolo muja, anamuyika mnyamatayo pansi pa zitsamba.
16 Och gick bort och satte sig tvärs öfver långt ifrå, vid ett armborst skott; ty hon sade: Jag gitter icke se uppå att pilten dör. Och vid hon satt tvärs öfver, hof hon upp sina röst, och gret.
Kenaka Hagara anachoka nakakhala pansi cha pakatalipo, pafupifupi mamita makumi asanu ndi anayi, popeza mʼmaganizo mwake amati, “Sindingaonerere mwanayu akufa.” Ndipo anakhala pansi cha poteropo nʼkumalira.
17 Då hörde Gud piltens röst, och Guds Ängel kallade Hagar af himmelen, sägandes: Hvad skadar dig, Hagar? Frukta dig intet; förty Gud hafver hört piltens röst, der han ligger.
Mulungu anamva mnyamatayo akulira ndipo mngelo wa Mulungu anayankhula kwa Hagara kuchokera kumwamba nati, “Chavuta nʼchiyani Hagara? Usachite mantha; Mulungu wamva kulira kwa mnyamatayo pamene wagonapo.
18 Statt upp, tag pilten, och håll honom med dina händer; ty jag skall göra honom till stort folk.
Munyamule mnyamatayo ndipo umugwire dzanja pakuti ndidzamupanga kukhala mtundu waukulu.”
19 Och Gud öppnade hennes ögon, att hon fick se en vattubrunn. Då gick hon till och fyllde sina flasko med vatten, och gaf piltenom dricka.
Kenaka Mulungu anatsekula maso a Hagara ndipo anaona chitsime cha madzi. Choncho anapita nadzaza botolo lija ndi madzi ndi kumupatsa mnyamatayo kuti amwe.
20 Och Gud var med piltenom; han växte, och bodde i öknene, och vardt en god skytte.
Mulungu anali ndi mnyamatayo pamene ankakula. Anakhala ku chipululu nakhala katswiri wolasa uta.
21 Och bodde i den öknene Pharan: Och hans moder tog honom hustru utur Egypti land.
Akukhala ku chipululu cha Parani, mayi ake anamupezera mkazi wochokera ku Igupto.
22 På samma tiden talade Abimelech och Phicol, hans härhöfvitsman, med Abraham, och sade: Gud är med dig uti allt det du gör.
Pa nthawiyo, Abimeleki ndi Fikolo wamkulu wankhondo wake anati kwa Abrahamu, “Mulungu ali nawe pa chilichonse umachita.
23 Så svär mig nu vid Gud, att du är mig icke arg, eller minom barnom, eller minom barnabarnom: Utan den barmhertighet, som jag hafver gjort med dig, den gör ock med mig, och landena, der du en främling uti äst.
Tsopano undilumbirire ine pano pamaso pa Mulungu kuti sudzachita mwa chinyengo ndi ine kapena ana anga kapena zidzukulu zanga. Undionetse ine pamodzi ndi dziko limene ukukhalamo ngati mlendo, kukoma mtima kokhala ngati kumene ndinakuonetsa ine.”
24 Då sade Abraham: Jag vill svärja.
Abrahamu anati, “Ine ndikulumbira.”
25 Och Abraham straffade Abimelech för den vattubrunnens skull, som Abimelechs tjenare hade tagit med våld.
Kenaka Abrahamu anadandaula kwa Abimeleki pa za chitsime chimene antchito a Abimeleki analanda.
26 Då svarade Abimelech: Jag hafver icke vist, ho det gjorde; ej heller sade du mig det; dertill hafver jag icke hört det förra än i dag.
Koma Abimeleki anati, “Ine sindikudziwa amene anachita zimenezi. Iwe sunandiwuze, ndipo ndazimva lero zimenezi.”
27 Då tog Abraham får och fä, och gaf Abimelech: Och gjorde båda ett förbund med hvarannan.
Choncho Abrahamu anabweretsa nkhosa ndi ngʼombe nazipereka kwa Abimeleki, ndipo anthu awiriwo anachita pangano.
28 Och Abraham ställde sju lamb afsides.
Abrahamu anapatulako ana ankhosa aakazi asanu ndi awiri kuchoka pagulu la nkhosa zina,
29 Sade Abimelech till Abraham: Hvad skola de sju lamb, som du hafver ställt der afsides?
ndipo Abimeleki anafunsa Abrahamu, “Kodi tanthauzo lake la ana ankhosa aakazi asanu ndi awiri amene wawapatula pawokhawa nʼchiyani?”
30 Han svarade: Sju lamb skall du taga af mine hand, att de skola vara mig till ett vittnesbörd, att jag denna brunn grafvit hafver.
Iye anayankha kuti, “Landirani ana ankhosa aakazi kuchokera mʼdzanja langa ngati umboni kuti ndinakumba chitsime ichi.”
31 Deraf heter det rummet BerSaba, att de båda med hvarannan der så svoro.
Kotero malo amenewo anatchedwa Beeriseba, chifukwa anthu awiriwo analumbirirapo malumbiro.
32 Och alltså gjorde de det förbund i BerSaba. Då stodo Abimelech och hans härhöfvitsman Phicol upp, och drogo in i de Philisteers land igen.
Atatha kuchita pangano pa Beeriseba, Abimeleki ndi Fikolo mkulu wankhondo wake anabwerera ku dziko la Afilisti.
33 Och Abraham plantade trä i BerSaba; och predikade der om Herrans eviga Guds namn;
Abrahamu anadzala mtengo wa bwemba ku Beeriseba, ndipo anapemphera pamenepo mʼdzina la Yehova, Mulungu Wamuyaya.
34 Och var en främling uti de Philisteers land i långan tid.
Ndipo Abrahamu anakhala mʼdziko la Afilisti kwa nthawi yayitali.

< 1 Mosebok 21 >