< 1 Mosebok 15 >

1 Sedan detta så skedt var, begaf sig, att Herrans ord i en syn kom till Abram, sägandes: Frukta dig intet, Abram, jag är ditt beskärm och din ganska stora lön.
Zitatha izi, Yehova anayankhula ndi Abramu mʼmasomphenya nati: “Usaope Abramu. Ine ndili ngati chishango chokutchinjiriza. Mphotho yako idzakhala yayikulu.”
2 Men Abram sade: Herre, Herre, hvad vill du mig gifva? Jag går barnlös, och min redesven, denne Eleasar af Damasco, hafver en son.
Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, mukhoza kundipatsa chiyani popeza ndikanali wopanda mwana ndipo amene adzatenge chuma changa ndi Eliezara wa ku Damasiko?
3 Och Abram sade ytterligare: Men mig hafver du ingen säd gifvit. Och si, mins tjenares son skall vara min arfvinge.
Inu simunandipatse ana kotero kuti wantchito wa ku nyumba kwanga ndiye amene adzalowe mʼmalo mwanga.”
4 Och si, Herrans ord kom till honom, sägandes: Han skall icke vara din arfvinge, utan den, som utaf ditt lif komma skall, han skall vara din arfvinge.
Yehova anayankhula naye nati: “Munthu uyu sadzalowa mʼmalo mwako, koma mwana wako weniweni wamwamuna, wobereka wekha ndiye adzalowe mʼmalo mwako.”
5 Och han hade honom ut, och sade: Se upp till himmelen, och räkna stjernorna, om du kan räkna dem. Och sade till honom: Så skall din säd vara.
Yehova anapita naye Abramu panja nati, “Tayangʼana kumwambaku, ndipo chifukwa cha chimenechi uwerenge nyenyezi ngati ungathe kuziwerenga.” Ndipo anamuwuza kuti, “Ndi mmene adzakhalire ana ako ndi zidzukulu zako.”
6 Abram trodde Herranom, och han räknade honom det till rättfärdighet.
Abramu anakhulupirira Yehova, ndipo ichi chinamuchititsa kukhala wolungama.
7 Och han sade till honom: Jag är Herren, som dig utfört hafver ifrån Ur utu Chaldeen, att jag dig detta land gifva skall till besittning.
Ndipo anamuwuza kuti, “Ine ndine Yehova amene ndinakuchotsa iwe ku mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kuti ndikupatse dziko ili kuti likhale lako.”
8 Abram sade: Herre, Herre, hvaruppå skall jag märka, att jag skall besitta det?
Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, kodi ndingadziwe bwanji kuti lidzakhaladi langa?”
9 Och han sade till honom: Tag mig ena treåra ko, och ena treåra get, och en treåra vädur, och ena turturdufvo, och ena unga dufvo.
Kotero Yehova anati kwa iye, “Kanditengere kamsoti kangʼombe ka zaka zitatu, kamsoti ka mbuzi ka zaka zitatu, ndi nkhosa yayimuna ya zaka zitatu pamodzi ndi nkhunda ndi kamwana ka njiwa.”
10 Och han tog allt detta, och delade det midt i tu ifrå hvart annat, och lade hvar delen tvärt emot den andra; men foglarne delade han intet.
Abramu anabweretsadi zonsezi nadula chilichonse pakati nʼkuzindandalika, chidutswa chilichonse kuyangʼanana ndi chinzake; koma njiwa ndi nkhunda sanazidule pakati.
11 Och foglarne kommo neder på kropparna, och Abram dref bort dem.
Pamene miphamba inabwera kuti itole nyama ija, Abramu anayipirikitsa.
12 Då solen nedergången var, föll en svår sömn på Abram, och si, en förskräckelse och ett stort mörker kom öfver honom.
Pamene dzuwa limalowa Abramu anagona tulo tofa nato ndipo mdima wandiweyani ndi wochititsa mantha unamuphimba.
13 Då sade han till Abram: Detta skall du veta, att din säd skall varda främmande uti ett land, det dem icke tillhörer, och man skall der göra dem till trälar och fara illa med dem i fyrahundrade år.
Tsono Yehova anati kwa iye, “Uyenera kudziwa mosakayika kuti zidzukulu zako zidzakhala alendo mʼdziko lachilendo ndipo zidzakhala akapolo ndi kuzunzidwa zaka 400.
14 Men öfver det folk, som de tjenande varda, skall jag domare vara; sedan skola de draga ut med stora håfvor.
Koma ndidzalanga dziko limene zidzukulu zako zidzagwireko ukapolo ndipo pambuyo pake iwo adzatulukamo ndi chuma chambiri.
15 Och du skall fara till dina fäder med frid, och i en god ålder begrafven varda.
Komabe iweyo udzamwalira mu mtendere ndi kuyikidwa mʼmanda utakalamba bwino.
16 Men de skola i fjerde mans ålder komma hit igen; förty de Amoreers ondska är icke ännu all fullkomnad.
Patapita mibado inayi, adzukulu ako adzabwereranso kuno popeza tchimo la Aamori silinafike pachimake kuti alangidwe.”
17 Då nu solen var nedergången, och mörker vordet, si, då rök en ugn, och en eld for emellan stycken.
Dzuwa litalowa ndipo mdima utagwa, panaoneka mʼphika wofuka nthunzi ya moto ndi sakali yoyaka ndipo zinadutsa pakati pa zidutswa za nyama zija.
18 På den dagen gjorde Herren ett förbund med Abram, och sade: Dine säd skall jag gifva detta landet, ifrå den älfvene i Egypten, allt intill den stora älfven Phrath:
Pa tsiku limenelo, Yehova anachita pangano ndi Abramu nati, “Ndikulonjeza kuti ndidzapereka dziko ili kwa zidzukulu zako, kuchokera ku mtsinje wa ku Igupto mpaka ku mtsinje waukulu wa Yufurate.
19 De Keneer, de Keniseer, de Kadmoneer,
Ndidzakupatsani dziko la Akeni, Akenizi, Akadimoni,
20 De Hetheer, de Phereseer, de Reser,
Ahiti, Aperezi, Arefaimu,
21 De Amoreer, de Cananeer, de Girgaseer, de Jebuseer.
Aamori, Akanaani, Agirigasi ndi Ayebusi.”

< 1 Mosebok 15 >