< 1 Mosebok 11 >
1 Och all verlden hade enahanda tungo och mål.
Nthawi imeneyo anthu onse a pa dziko lapansi ankayankhula chiyankhulo chimodzi ndipo mawu amene ankayankhula anali amodzi.
2 Då de nu drogo öster ut, funno de en plan uti Sinear land, och bodde der.
Pamene anthu amapita chakummawa anapeza chigwa ku dziko la Sinara nakhazikikako.
3 Och sade till hvarannan: Kommer, låter oss slå tegel och bränna. Och togo tegel för sten, och ler för kalk.
Tsono anawuzana kuti, “Tiyeni tiwumbe njerwa ndi kuziwotcha bwinobwino.” Tsono mʼmalo mwa miyala anagwiritsa ntchito njerwa zowotcha, ndipo mʼmalo mwa matope anagwiritsa ntchito phula.
4 Och sade: Kommer, låter oss bygga en stad och ett torn, hvilkets höjd skall räcka upp i himmelen, att vi måge göra oss ett namn, förty vi varde tilläfventyrs spridde ut i all land.
Kenaka anati, “Tiyeni tidzimangire mzinda wokhala ndi nsanja yoti ikafike kumwamba kuti titchuke. Kupanda kutero tibalalikana pa dziko lonse lapansi.”
5 Då steg Herren neder, att han skulle se staden och tornet, som menniskones barn byggde.
Koma Yehova anatsika kudzaona mzindawo ndi nsanja imene anthu aja ankayimanga.
6 Och Herren sade: Si, det är enahanda folk, och enahanda mål ibland dem alla, och hafva detta begynt att göra, de varda icke aflåtande af allt det de hafva sig företagit att göra.
Yehova anati, “Anthuwa ndi amodzi, ndipo ali ndi chiyankhulo chimodzi. Izi akuchitazi nʼchiyambi chabe cha zomwe akufuna kukwaniritsa kuchita.
7 Kommer, låter oss stiga neder och förbistra der deras tungomål, så att ingen skall förstå den andras mål.
Tiyeni titsikireko tikasokoneze chiyankhulo chawo kuti asamamvetsetsane.”
8 Och så skingrade Herren dem dädan i all land, så att de återvände bygga staden.
Choncho Yehova anabalalitsa anthu aja pa dziko lonse lapansi ndipo analeka kumanga mzindawo.
9 Derföre kallades hans namn Babel, ty att Herren der förbistrade all lands tungomål, och Herren spridde dem dädan ut i all land.
Nʼchifukwa chake mzindawo unatchedwa Babeli, popeza Yehova anasokoneza chiyankhulo cha anthu onse. Powachotsa kumeneko, Yehova anawabalalitsira pa dziko lonse lapansi.
10 Detta är Sems slägt: Sem var hundrade år gammal, och födde Arphachsad, tu år efter floden.
Nayi mibado yochokera kwa Semu. Patapita zaka ziwiri chitatha chigumula, Semu ali ndi zaka 100, anabereka Aripakisadi.
11 Och lefde derefter i femhundrade år, och födde söner och döttrar.
Atabereka Aripakisadi, Semu anakhala ndi moyo zaka 500 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
12 Arphachsad var fem och tretio år gammal, och födde Salah.
Pamene Aripakisadi anali ndi zaka 35, anabereka Sela.
13 Och lefde derefter fyrahundrade och tre år, och födde söner och döttrar.
Atabereka Sela, Aripakisadi anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
14 Salah var tretio år gammal, och födde Eber.
Pamene Sela anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Eberi.
15 Och lefde derefter fyrahundrade och tre år, och födde söner och döttrar.
Atabereka Eberi, Sela anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
16 Eber var tretio och fyra år gammal, och födde Peleg.
Pamene Eberi anali ndi zaka 34 anabereka Pelegi.
17 Och lefde derefter fyrahundrade och tretio år, och födde söner och döttrar.
Atabereka Pelegi, Eberi anakhala ndi moyo zaka zina 430 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
18 Peleg var tretio år gammal, och födde Regu.
Pamene Pelegi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Reu.
19 Och lefde derefter i tuhundrade och nio år, och födde söner och döttrar.
Atabereka Reu, Pelegi anakhala zaka zina 209 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
20 Regu var tu och tretio år gammal, och födde Serug.
Pamene Reu anali ndi zaka 32, anabereka Serugi.
21 Och lefde derefter tuhundrade och sju år, och födde söner och döttrar.
Atabereka Serugi, Reu anakhala ndi moyo zaka zina 207 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
22 Serug var tretio år gammal, och födde Nahor.
Pamene Serugi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Nahori.
23 Och lefde derefter tuhundrade år, och födde söner och döttrar.
Atabereka Nahori, Serugi anakhala ndi moyo zaka zina 200 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
24 Nahor var nio och tjugu år gammal, och födde Tharah.
Pamene Nahori anali ndi zaka 29, anabereka Tera.
25 Och lefde derefter hundrade och nitton år, och födde söner och döttrar.
Atabereka Tera, Nahori anakhala ndi moyo zaka zina 119 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
26 Tharah var sjutio år gammal, och födde Abram, Nahor och Haran.
Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani.
27 Desse äro Tharahs slägter: Tharah födde Abram, Nahor och Haran. Haran födde Lot.
Nayi mibado yochokera mwa Tera. Tera anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. Ndipo Harani anabereka Loti.
28 Och dödde Haran när sinom fader Tharah, uti hans faders land i Ur i Chaldeen.
Abambo ake a Tera akanali ndi moyo, Harani anamwalira ku Uri wa ku Akaldeya kumene anabadwira.
29 Då togo Abram och Nahor sig hustrur: Abrams hustru het Sarai, och Nahors hustru Milca Harans dotter, den fader var åt Milca och åt Jisca.
Abramu ndi Nahori onse anakwatira. Dzina la mkazi wa Abramu linali Sarai, ndipo la mkazi wa Nahori linali Milika. Iyeyu ndi Isika abambo awo anali Harani.
30 Men Sarai var ofruktsam, och hade inga barn.
Sarai analibe ana chifukwa anali wosabereka.
31 Så tog Tharah sin son Abram, och Lot sins sons Harans son, och sina sonahustru Sarai, sins sons Abrams hustru, och förde dem ifrån Ur utu Chaldeen, på det de skulle fara i Canaans land; och de kommo till Haran, och bodde der.
Tera anatenga mwana wake Abramu, mdzukulu wake Loti, ndi mpongozi wake Sarai, mkazi wa Abramu natuluka mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kupita ku Kanaani. Pamene anafika ku Harani, anakhazikika kumeneko.
32 Och Tharah vardt tuhundrade och fem år gammal, och blef död i Haran.
Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.