< Hesekiel 6 >
1 Och Herrans ord skedde till mig, och sade:
Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti,
2 Du menniskobarn, vänd ditt ansigte åt Israels berg, och prophetera emot dem;
“Iwe mwana wa munthu, yangʼana ku mapiri a Israeli; yankhula nawo modzudzula
3 Och säg: I Israels berg, hörer Herrans Herrans ord; detta säger Herren Herren, både till berg och högar, både till bäckar och dalar: Si, jag skall låta komma svärdet öfver eder och förgöra edra höjder.
kuti, ‘Inu mapiri a ku Israeli, imvani mawu a Ambuye Yehova. Iye akuwuza mapiri, magomo, mitsinje ndi zigwa kuti: Ine ndizakuthirani nkhondo ndipo ndidzawononga nyumba zanu mʼmene mukupembedzeramo mafano.
4 Att edor altare skola förödd varda, och edra afgudar sönderslagne och skall låta ihjälslå edra kroppar inför beläten.
Maguwa anu ansembe adzagumulidwa ndipo maguwa anu ofukizira lubani adzaphwanyidwa; ndipo ndidzapha anthu anu pamaso pa mafano anu.
5 Ja, jag skall fälla Israels barnas kroppar inför edor beläte, och förströ edor ben kringom edor altare.
Ine ndidzagoneka mitembo ya Aisraeli pamaso pa mafano awo, ndipo ndidzamwaza mafupa anu mozungulira maguwa anu ansembe.
6 Der I bon, der skola städerna öde varda, och höjderna ödeläggas; ty man skall förlägga edor altare, och göra dem öde, och sönderslå edra afgudar, och göra dem till intet och sönderslå edor beläte, och förlägga det I stiktat hafven.
Konse kumene mumakhala, mizinda yanu idzasanduka bwinja. Nyumba zanu zopembedzera mafano zidzagumulidwa kotero kuti maguwa anu adzawonongedwa ndi kusakazidwa, mafano anu adzaphwanyidwa ndi kuwonongedwa. Maguwa anu ofukizirapo lubani adzagwetsedwa pansi ndipo zonse zimene munapanga zidzatheratu.
7 Och de slagne skola ligga ibland eder, att I skolen förnimma att jag är Herren.
Anthu anu adzaphedwa pakati panu, ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
8 Men jag vill låta några igenblifva af eder, de der svärdet undslippa skola ibland Hedningarna, när jag eder i landen förstrött hafver.
“Komabe ndidzasiya ena pangʼono opulumuka ku nkhondo. Iwowa ndidzawamwazira ku mayiko ena pakati pa anthu a mitundu ina.
9 De samme edre igenblefne skola då tänka uppå mig ibland Hedningarna, der de fångne vara måste, när jag förkrossat hafver deras horiska hjerta, det ifrå mig viket är, och deras horiska ögon, som efter deras afgudar sett hafva; och dem skall ångra den ondska, som de genom all sin styggelse bedrifvit hafva;
Pamenepo opulumuka mwa inu adzandikumbukira ku mayiko kumene anatengedwa ukapolo. Ndidzawamvetsa chisoni chifukwa cha kusakhulupirika kwawo ndi kundipandukira kuja ndiponso chifukwa kuti anayika mtima wawo pa mafano. Choncho adzachita okha manyazi chifukwa cha zoyipa zimene ankachita ndi miyambo yonyansa imene ankatsata.
10 Och skola förnimma, att jag är Herren, och hafver icke fåfängt talat, att jag sådana olycka skulle göra dem.
Ndipo iwo adzadziwa kuti ndine Yehova ndi kuti sindinkawaopseza chabe pamene ndinanena kuti ndidzawawononga.
11 Detta säger Herren Herren: Slå dina händer samman, och stampa med dina fötter, och säg ve öfver all den ondskas styggelse i Israels hus, för hvilkas skull de genom svärd, hunger och pestilentie falla måste.
“Ambuye Yehova akuti: Womba mʼmanja mwako ndipo uponde mapazi ako pansi mwamphamvu ndipo ufuwule kuti, ‘Mayo!’ chifukwa cha zonyansa ndi zoyipa zonse zimene Aisraeli achita, pakuti adzaphedwa ndi lupanga, njala ndi mliri.
12 Den som långt borto är, han skall dö af pestilentie, och den hardt när är, han skall falla genom svärd; men den som öfverblifver, och derföre förvarad är, han skall dö af hunger; alltså skall jag fullkomna mina grymhet ibland dem;
Amene ali kutali adzafa ndi mliri, ndipo amene ali pafupi adzafa pa nkhondo, ndipo amene adzapulumuke ndi kusaphedwa adzafa ndi njala. Kotero ndidzakwaniritsa ukali wanga pa iwo.
13 Att I förnimma skolen, att jag är Herren, när deras slagne skola ligga ibland deras afgudar omkring deras altare, på alla högar, och på all berg, och under all grön trä, och under alla tjocka ekar, i hvilka rum de allahanda afgudom sött rökoffer gjort hafva.
Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene anthu awo adzagona atafa pakati pa mafano awo mozungulira maguwa awo ansembe, pamwamba pa magomo ndi mapiri onse, pansi pa mtengo uliwonse watambalala ndi wa thundu uliwonse wamasamba ambiri, kumalo kumene ankapereka nsembe zonunkhira kwa mafano awo onse.
14 Jag skall utsträcka mina hand emot dem, och göra landet tomt och öde, allt ifrån öknene intill Diblath, ehvar de bo; och de skola förnimma, att jag är Herren.
Choncho ndidzawalanga ndi mkono wanga ndi kusandutsa dziko kukhala bwinja. Dziko lonse kumene akukhala kuyambira ku chipululu mpaka ku mzinda wa Ribula ndidzalisandutsa bwinja. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”