< Hesekiel 27 >

1 Och Herrans ord skedde till mig, och sade:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 Du menniskobarn, gör klagogråt öfver Tyrus;
“Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira Turo.
3 Och säg till Tyrus, som ligger vid hafvet, och handlar med många öars folk: Detta säger Herren Herren: O Tyrus, du hafver sagt: Jag är den aldraskönaste.
Uza Turo, mzinda wokhala pa dooko la nyanja, wochita malonda ndi anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja kuti: Ambuye Yehova akuti, “Iwe Turo, umanena kuti, ‘Ndine wokongola kwambiri.’
4 Dina gränsor äro midt i hafvena, och dina byggningsmän hafva tillpyntat dig som aldraskönast.
Malire ako anali mʼkati mwenimweni mwa nyanja; amisiri ako anakukongoletsa kwambiri.
5 Allt ditt brädeverk hafva de gjort af furoträ af Senir, och låtit föra cedreträ ifrå Libanon, och gjort din mastträ derutaf;
Anakupanga ndi matabwa a payini ochokera ku Seniri; anatenga mikungudza ya ku Lebanoni kupangira mlongoti wako.
6 Och dina åror af eketrä ifrå Basan, och dina bänkar af elphenben, och stolar af Chittims öar.
Ndi mitengo ya thundu ya ku Basani anapanga zopalasira zako; ndi matabwa a mitengo ya payini yochokera ku zilumba za Kitimu. Pakuti anapanga thandala lako pakati pa matabwawo panali minyanga ya njovu.
7 Ditt segel var af stickadt silke, utaf Egypten, och ditt märke stickadt deruti, och ditt täckelse af gult silke och purpur, ifrå de öar Elisa.
Nsalu yabafuta yopeta yochokera ku Igupto inali thanga yako, ndipo inakhala ngati mbendera. Nsalu zophimba matenti ako zinali za mtundu wamtambo ndi pepo zochokera ku zilumba za Elisa.
8 De af Zidon och Arvad voro dine båtsmän, och du hade skickeliga män i Tyro till skeppare.
Anthu a ku Sidoni ndi Arivadi ndi amene anali opalasa ako. Anthu aluso ako, iwe Turo, anali mwa iwe ndiwo amene ankakuyendetsa.
9 De äldste och kloke af Gebal måste bygga din skepp; all skepp i hafvena och skeppfolk fann man när dig, de hade sin handel när dig.
Akuluakulu ndi eni luso a ku Gebala anali mʼkati mwako, ngati okonza zibowo zako. Sitima za pa nyanja zonse, ndi oyendetsa ake ankabwera pamodzi ndi katundu kudzachita nawe malonda.
10 De utaf Persien, Lydien och Libyen voro ditt krigsfolk, hvilke sina sköldar och hjelmar uti dig upphängde, och dermed beprydde dig.
“Anthu a ku Perisiya, a ku Ludi ndi Puti anali asilikali mʼgulu lako la nkhondo. Iwo ankapachika zishango ndi zipewa zawo zankhondo pa makoma ako, kubweretsa kwa iwe ulemerero.
11 De af Arvad voro i dinom här, allt omkring på dina murar, och väktare på din torn; de hängde allestäds sina sköldar på murarna allt omkring, och gjorde dig så dägeligan.
Anthu a ku Arivadi ndi Heleki ankalondera mbali zonse za mpanda wako; anthu a ku Gamadi anali mu nsanja zako, Iwo ankapachika zishango zawo pa makoma ako onse. Amenewo ndiwo anakukongoletsa kwambiri.
12 Du hade din handel på hafvens, och lät komma allahanda varor, silfver, jern, tenn och bly, in uppå din marknad.
“Dziko la Tarisisi linachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa katundu wako wamtundumtundu. Iwo ankapereka siliva, chitsulo, chitini ndi mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
13 Javan, Thubal och Mesech handlade med dig, och förde trälar och koppar in uppå din marknad.
“Yavani, Tubala ndi Mesaki ankachita nawe malonda; iwo ankapereka akapolo ndi ziwiya za mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
14 De af Thogarma förde dig hästar, och vagnar, och mular, in på din marknad.
“Anthu a ku Beti Togarima ankapereka akavalo antchito, akavalo ankhondo ndi abulu mosinthanitsa ndi katundu wako.
15 De af Dedan voro dine köpmän, och du handlade allestäds på öomen; de sålde dig elphenben och hebenträ.
“Anthu a ku Dedani ankachita nawe malonda, ndipo anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja anali ogula malonda ako. Ankakupatsa minyanga ya njovu ndi phingo.
16 De Syrer hemtade ifrå dig ditt arbete, som du gjorde, och förde rubin, purpur, tapeter, silke och fogel, och christall, in på din marknad.
“Anthu a ku Aramu ankachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa zinthu zako. Iwo ankapereka miyala ya emeradi, nsalu zapepo, nsalu zopetapeta, nsalu zabafuta, korali ndi miyala ya rubi mosinthanitsa ndi katundu wako.
17 Juda och Israels land handlade ock med dig, och förde dig till din marknad hvete af Minnith, och balsam, och hannog, och oljo, och mastix.
“Yuda ndi Israeli ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka tirigu ochokera ku Miniti ndi zokometsera zakudya, uchi, mafuta ndi mankhwala mosinthanitsa ndi katundu wako.
18 Hemtade ock Damascus ditt arbete ifrå dig, och allahanda varo, för starkt vin och kosteliga ull.
“Anthu a ku Damasiko, chifukwa cha zinthu zako za malonda zambiri ndi katundu wako wosiyanasiyana, ankachita nawe malonda a vinyo wochokera ku Heliboni ndi ubweya wankhosa ochokera ku Zahari.
19 Dan och Javan, och Meussal förde ock på din marknad jernverk, casia och calmus, att du dermed handla skulle.
Adani ndi Agriki ochokera ku Uzala ankagula katundu wako. Iwo ankapereka chitsulo chosalala, kasiya ndi bango lonunkhira mosinthanitsa ndi katundu wako.
20 Dedan handlade med dig med täcken, der man uppå sitter.
“Anthu a ku Dedani ankakugulitsa nsalu zoyika pa zishalo za akavalo.
21 Arabien, och alle Förstar af Kedar, handlade med dig, med får, vädrar och bockar.
“Arabiya ndi mafumu onse a ku Kedara anali ogula malonda ako. Iwo ankachita nawe malonda a ana ankhosa onenepa, nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
22 De köpmän af Seba och Raema handlade med dig, och förde till din marknad allahanda kosteligit speceri, och ädla stenar och guld.
“Anthu amalonda a ku Seba ndi Raama ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka zonunkhira zosiyanasiyana zabwino kwambiri, miyala yokongola ndi golide mosinthanitsa ndi katundu wako.
23 Haran, och Canne, och Eden, samt med de köpmän af Seba, Assur och Chilmad, voro ock dine köpmän.
“Amalonda a ku Harani, Kane, Edeni, Seba, Asuri ndi Kilimadi ankachita nawe malonda.
24 Alle handlade de med dig, med kosteligit kläde, med silkes och stickade mantlar, hvilka de uti kosteliga cedrekistor och väl förvarad, till din marknad förde.
Iwowa ankasinthanitsana nawe zovala zokongola, nsalu zopetapeta, zoyala pansi za mawangamawanga, atazimanga bwino ndi zingwe zolimba.
25 Men skeppen utaf hafvet voro de yppersta i dinom marknad; alltså äst du mycket rik och härlig vorden midt i hafvena;
“Sitima za pa madzi za ku Tarisisi zinali zonyamula malonda ako. Motero iwe uli ngati sitima yapamadzi yodzaza ndi katundu wolemera.
26 Och dine skeppmän förde till dig på stort vatten. Men ett östanväder skall sönderbråka dig midt uppå hafvena;
Anthu opalasa ako amakupititsa pa nyanja yozama. Koma mphepo yakummawa idzakuthyolathyola pakati pa nyanja.
27 Så att dina varor, köpmän, handlare, skaffare, skeppare och skeppbyggare, och dine handterare, och alle dine örligsmän, och allt folket i dig, skola förgås midt uppå hafvena, på den tiden du nederlägges;
Chuma chako, katundu wako, malonda ako, okuyendetsa ako, okuwongolera ako ndi opanga sitima za pa madzi, anthu ako amalonda ndi asilikali ako onse ndiponso aliyense amene ali mʼmenemo adzamira mʼnyanja tsiku limene udzawonongeka.
28 Så att ock hamnerna varda bäfvande, för dina skeppares rops skull.
Madera a mʼmbali mwa nyanja adzagwedezeka chifukwa cha kufuwula kwa oyendetsa sitimawo.
29 Och alle de som med årom ro, samt med båtsmän och styromän, skola stiga utu skeppen upp på landet;
Onse amene amapalasa sitima zapamadzi, adzatuluka mʼsitima zawo; oyendetsa ndi onse owongolera sitima zapamadzi adzayimirira mʼmbali mwa nyanja.
30 Och högt ropa öfver dig, bitterliga klaga, och kasta stoft uppå sitt hufvud, och besöla sig i asko.
Iwo akufuwula, kukulira iwe kwambiri; akudzithira fumbi kumutu, ndi kudzigubuduza pa phulusa.
31 De skola raka sig håret af öfver dig, och draga säcker uppå sig, och af hjertat bitterliga gråta öfver dig och sörja.
Akumeta mpala mitu yawo chifukwa cha iwe ndipo akuvala ziguduli. Akukulira iweyo ndi mitima yowawa kwambiri.
32 Och skola deras barn begråta dig: Ack! ho är någon tid så stilla vorden på hafvena, som du Tyrus?
Akuyimba nyimbo yokudandaulira nʼkumati: ‘Ndani anawonongedwapo ngati Turo pakati pa nyanja?’
33 Då du dref din handel på hafvena, gjorde du mång land rik; ja, med dina många varor, och dinom köpenskap, gjorde du Konungarna på jordena rika.
Pamene malonda ako ankawoloka nyanja unakhutitsa mitundu yambiri ya anthu. Mafumu a dziko lapansi analemera ndi chuma chako komanso ndi malonda ako.
34 Men nu äst du af hafvena stört uti det rätta djupa vattnet, så att din handel och allt ditt folk i dig förgånget är.
Koma tsopano wathyokera mʼnyanja, pansi penipeni pa nyanja. Katundu wako ndi onse amene anali nawe amira pamodzi nawe.
35 Alle de, som på öarna bo, förskräckas öfver dig, och deras Konungar grufva sig, och se ömkeliga ut.
Onse amene amakhala mʼmbali mwa nyanja aopsedwa ndi zimene zakuchitikira. Mafumu awo akuchita mantha ndipo nkhope zangoti khululu.
36 De köpmän i landena hvissla till dig, att du så hastigt förgången äst, och kan intet mer uppkomma.
Anthu amalonda a mitundu ina akukunyogodola. Watha mochititsa mantha ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.”

< Hesekiel 27 >