< Hesekiel 20 >

1 Och det begaf sig i sjunde årena, på tionde dagen i femte månadenom, kommo någre af de äldsta i Israel till att fråga Herran, och satte sig neder för mig.
Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu, chaka chachisanu ndi chiwiri, ena mwa akuluakulu a Israeli anabwera kudzapempha nzeru kwa Yehova, ndipo anakhala pansi pamaso panga.
2 Då skedde Herrans ord till mig, och sade:
Tsono Yehova anandiyankhula nati:
3 Du menniskobarn, tala med Israels äldsta, och säg till dem: Detta säger Herren Herren: Ären I komne till att fråga mig? Så sant som jag lefver, jag vill intet svar gifva eder, säger Herren Herren.
“Iwe mwana wa munthu, ayankhule akuluakulu a Israeli ndi kuwawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Kodi mwabwera kudzapempha nzeru kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, Ine sindidzakulolani kupempha nzeru kwa Ine, akutero Ambuye Yehova.’
4 Men vill du menniskobarn straffa dem, så må du straffa dem alltså: Håll dem före deras fäders styggelse;
“Kodi uwaweruza? Iwe mwana wa munthu, kodi ugamula mlandu wawo? Uwadziwitse tsono zonyansa zimene anachita makolo awo, uwawuze kuti,
5 Och säg till dem: Detta säger Herren Herren: På den tid jag utvalde Israel, upphof jag mina hand till Jacobs hus säd, och lät dem känna mig uti Egypti land; ja, jag upphof mina hand till dem, och sade: Jag är Herren edar Gud.
‘Ambuye Yehova akuti: Pa tsiku limene ndinasankha Israeli, ndinalumbira kwa zidzukulu za nyumba ya Yakobo ndipo ndinadziwulula kwa iwo ku Igupto. Ndinalumbira ndi kuwawuza kuti: Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
6 Men jag upphof på samma tid mina hand, att jag skulle föra, dem utur Egypti land, in uti ett land som jag dem försett hade, det med mjölk och hannog flyter; ett ädla land för all land;
Pa tsiku limenelo ndinalumbira kwa iwo kuti ndidzawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kupita nawo ku dziko limene ndinawapezera, dziko la mwana alirenji, dziko lokongola kwambiri kupambana mayiko ena.
7 Och sade till dem: Hvar och en kaste bort styggelsen för sin ögon, och orener icke eder på Egypti afgudar; ty jag är Herren edar Gud.
Ndipo ndinawawuza kuti, ‘Aliyense ataye zinthu zonse zonyansa zimene ankasangalala nazo, ndipo musadziyipitse ndi mafano a Igupto, Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’
8 Men de voro mig ohörsamme, och ville intet höra mig, och ingen af dem kastade sin styggelse bort för sin ögon, och öfvergåfvo icke Egypti afgudar; då tänkte jag utgjuta mina grymhet öfver dem, och låta alla mina vrede gå öfver dem, midt uti Egypti land;
“‘Koma iwo anandiwukira ndipo sanafune kundimvera. Palibe amene anataya zonyansa zonse zimene ankasangalala nazo. Panalibenso amene anasiya mafano a ku Igupto. Tsono ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwaonetsa mkwiyo wanga mʼdziko la Igupto momwemo.
9 Men jag lät det tillbaka, för mitt Namns skull, att det icke skulle ohelgadt varda för Hedningomen, ibland hvilka de voro, och för hvilkom jag hade gifvit mig dem tillkänna, att jag dem utur Egypti land föra ville.
Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene ankakhala pakati pawo. Paja ndinali nditaonetsa mphamvu zanga pamaso pa mitunduyo potulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto.
10 Och då jag; dem utur Egypti land fört hade, och låtit dem komma in uti öknena;
Choncho ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kubwera nawo mʼchipululu.
11 Gaf jag dem min bud, och lärde dem mina rätter, genom hvilka menniskan lefver, den dem håller.
Ndinawapatsa malangizo anga ndi kuwadziwitsa malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo.
12 Jag gaf dem ock min Sabbath, till ett tecken emellan mig och dem, på det de skulle lära, att jag är Herren, som dem helgar.
Ndinawapatsanso Masabata ngati chizindikiro pakati pathu, kuti adziwe kuti Ine Yehova ndinawapatula.
13 Men Israels hus var mig också ohörsamt uti öknene, och lefde intet efter min bud, och föraktade mina rätter, genom hvilka menniskan lefver, som dem håller, och ohelgade min Sabbath ganska svårliga; då tänkte jag utgjuta mina grymhet öfver dem uti öknene, och platt förgöra dem;
“‘Komabe anthu a Israeli anandiwukira mʼchipululu. Iwo sanatsatire malangizo anga koma anakana malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo. Ndipo anayipitsa kotheratu Masabata anga. Choncho, ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawononga mʼchipululu.
14 Men jag lät det tillbaka, för mitt Namns skull, att det icke skulle ohelgadt varda ibland Hedningarna, för hvilkom jag dem utfört hade.
Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Igupto.
15 Ock hof jag mina hand upp emot dem i öknene, att jag icke ville låta dem komma in uti det land, som jag dem gifvit hade, det med mjölk och hannog flyter; ett ädla land för alla land;
Ndinalumbiranso kwa iwo mʼchipululu muja, nditakweza dzanja, kuti sindidzawalowetsanso mʼdziko limene ndinawapatsa, dziko la mwana alirenji, lokoma kwambiri kuposa mayiko ena onse.
16 Derföre, att de föraktade mina rätter, och lefde icke efter min bud, och mina Sabbather ohelgade; ty de vandrade efter deras hjertas afgudar.
Paja anakana malamulo anga, sanatsatire malangizo anga ndipo anayipitsa masabata anga. Mitima yawo inakonda mafano.
17 Men mitt öga skonade dem, att jag icke förderfvade eller platt förgjorde dem i öknene.
Komabe ndinawamvera chisoni ndipo sindinawawononge kapena kuwatheratu mʼchipululu.
18 Och jag sade till deras barn i öknene: I skolen icke lefva efter edra fäders bud, och icke hålla deras rätter, och icke orena eder uppå deras afgudar.
Tsono kwa ana awo mʼchipululu ndinati, ‘Musatsatire malangizo a makolo anu kapena kusunga malamulo awo kapena kudziyipitsa ndi mafano awo.
19 Ty jag är Herren edar Gud; efter min bud skolen I lefva, och mina rätter skolen I hålla, och göra derefter;
Ine ndine Yehova Mulungu wanu; tsatirani malangizo anga ndipo sungani malamulo anga.
20 Och mina Sabbather skolen I helga, att de skola vara ett tecken emellan mig och eder, på det I veta skolen att jag, Herren, är edar Gud.
Masabata anga muziwasunga ngati opatulika kuti akhale chizindikiro pakati pa Ine ndi inu. Mukatero mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’
21 Men barnen voro mig ock ohörsam, lefde icke efter min bud, höllo ock icke mina rätter, så att de gjorde derefter, genom hvilka menniskan lefver, den dem håller, och ohelgade mina Sabbather; då tänkte jag utgjuta mina grymhet öfver dem, och låta alla mina vrede gå öfver dem i öknene;
“‘Koma ana awo anandiwukira. Iwo sanatsatire malangizo anga, sanamvere malamulo anga, ngakhale kuti amapereka moyo kwa munthu amene amawamvera. Ndiponso anayipitsa Masabata anga. Choncho ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawonongeratu mʼchipululu momwemo.
22 Men jag vände mina hand, och lät det tillbaka, för mitt Namns skull, att det icke skulle ohelgadt varda för Hedningomen, för hvilkom jag dem utfört hade.
Koma sindinatero chifukwa cha dzina langa kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Iguptomo.
23 Jag hof ock mina hand upp emot dem i öknene, att jag skulle förströ dem ibland Hedningarna, och förskingra dem i landen;
Choncho ndinalumbira mʼchipululu, nditakweza dzanja langa, kuti ndidzawabalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwamwazira ku mayiko akutali,
24 Derföre, att de icke höllo min bud, och föraktade mina rätter, och ohelgade mina Sabbather, och sågo efter deras fäders afgudar.
chifukwa sanamvere malamulo anga, anakana malangizo anga, nayipitsa masabata anga, ndi kupembedza mafano a makolo awo.
25 Derföre gaf jag dem den lära, som intet god är; och de rätter, uti hvilka de intet lif hafva kunna;
Ine ndinawapatsanso malangizo amene sanali abwino ndi malamulo amene sakanatha kupeza nawo moyo.
26 Och förkastade dem med deras offer då de uppbrände i eld all förstföding; på det jag skulle bedröfva dem, och de lära skulle, att jag är Herren.
Ndinawalekerera kuti adziyipitse ndi mphatso zawo zomwe, makamaka popereka ana awo oyamba kubadwa ngati nsembe zopsereza. Ndinatero kuti ndiwadetse nkhawa ndi kuti adziwe kuti Ine ndine Yehova.’
27 Derföre tala, du menniskobarn, med Israels hus, och säg till dem: Detta säger Herren Herren: Edra fäder hafva ännu mer försmädat och trotsat mig.
“Tsono iwe mwana wa munthu, yankhula nawo Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti makolo anu anandinyozanso posaonetsa moyo wokhulupirika.
28 Ty då jag hade låtit dem komma in uti landet, öfver hvilket jag mina hand upphäfvit hade, att jag skulle det gifva dem; hvar de någorstäds sågo en hög backa, eller tjockqvistadt trä, der offrade de sitt offer, och båro dit sina obehageliga gåfvor, och rökte der sin söta rök, och utgöto der sitt drickoffer.
Nditawalowetsa mʼdziko limene ndinachita kulumbirira kuti ndidzawapatsa, iwo tsono ankapita kulikonse kumene anaona chitunda chachitali ndi mtengo wa masamba ambiri kukapereka kumeneko nsembe ndi zopereka zawo zimene zinkandikwiyitsa. Kumeneko ankapereka nsembe za fungo lokoma ndiponso nsembe za zakumwa.
29 Men jag sade till dem: Hvad skall dock den höjden, dit I gån? Och så kallades det en höjd, allt intill denna dag.
Tsono ndinawafunsa kuti: Kodi chitunda chimene mukupitako nʼchotani? Chitundachi chakhala chikutchedwa mpaka lero kuti ‘Chitunda cha Chipembedzo.’
30 Derföre säg till Israels hus: Detta säger Herren Herren: I orenen eder uti edra fäders väsende, och bedrifven horeri med edor styggelse;
“Tsono uwawuze Aisraeli kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi mudzadziyipitsa nokha monga anachitira makolo anu ndi kuchita chigololo ndi milungu yawo yonyansa?
31 Och besmitten eder på edra afgudar, hvilkom I offren edra gåfvor, och uppbrännen edra söner och döttrar i eld, allt intill denna dag; och jag skulle gifva eder af Israels hus svar? Så sant som jag lefver, säger Herren Herren, jag skall intet svar gifva eder.
Pamene mubwera kudzapereka mphatso zanu ndi kudzapereka ana kuti akhale ngati nsembe zopsereza mumadziyipitsa ndi mafano anu mpaka lero. Kodi Aisraeli, ndingathe kukulolani bwanji kuti mulandire malangizo kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, sindidzalola kuti mupemphe nzeru kwa Ine.
32 Dertill, då I tänken: Vi vilje göra lika som Hedningarna, och såsom annor folk i landen, och tillbedja stockar och stenar, skall det fela eder.
“‘Inu munanena kuti, ‘Tikufuna tikhale ngati anthu a mitundu ina, ngati anthu adziko lapansi, amene amapembedza mtengo ndi mwala.’ Koma zimene mukuganizazo sizidzachitika.
33 Så sant som jag lefver, säger Herren Herren, jag skall råda öfver eder med starka hand och uträcktom arm, och med utgjuten grymhet;
Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ndi dzanja langa lamphamvu, nditasamula mkono wanga mokwiya kwambiri, Ine ndidzakhala wokulamulani.
34 Och skall föra eder ifrå folken, och församla eder utu de land, dit I förströdde ären, med starka hand, med uträcktom arm, och med utgjuten grymhet;
Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndikukusonkhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munamwazikirako, ndi dzanja langa lamphamvu ndi lotambasuka ndili wokwiya kwambiri.
35 Och skall låta eder komma uti folks öken, och der vara i rätta med eder, ansigte emot ansigte.
Ndidzakulowetsani mʼchipululu cha anthu a mitundu ina ndipo kumeneko, moonana maso ndi maso, ndidzakuzengani mlandu.
36 Lika som jag med edra fäder uti öknene vid Egypten i rätta var, rätt så skall jag vara i rätta med eder, säger Herren Herren.
Monga ndinawalangira makolo anu mʼchipululu cha dziko la Igupto, motero ndidzakulangani, akutero Ambuye Yehova.
37 Jag skall låta komma eder under riset, och tvinga eder uti förbundsens bandom.
Ndidzakuwerengani ndi ndodo ya mʼbusa, kukulowetsani mʼchimango cha pangano langa.
38 Och jag skall utfäja de affälliga, och de som emot mig öfverträda, ibland eder; ja, jag skall föra dem utu det land, der I nu bon, och intet låta dem komma in uti Israels land, att I lära skolen, att jag är Herren.
Ndidzakuchotserani anthu amene anandigalukira ndi kundiwukira. Ngakhale ndidzawatulutsa mʼdziko limene akukhalamo, koma sadzalowamo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
39 Derföre, I af Israels hus, detta säger Herren Herren: Efter I ju intet viljen höra mig, så görer som eder täckes, och hvar edra tjene sinom afgud; men mitt helga Namn låter härefter oskämdt vara, med edor offer och afgudar.
“‘Koma inu Aisraeli, zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Pitani katumikireni mafano anu onse, aliyense wa inu! Koma mʼtsogolo mwake mudzandimvera ndithu ndipo simudzayipitsa dzina langa lopatulika popereka mphatso zanu kwa mafano.
40 Ty detta säger Herren Herren: På mino heligo berge, på de höga bergena Israel, der skall hela Israels hus, och alle de som i landet äro, tjena mig; der skola de vara mig tacknämlige, och der skall jag äska uppå edor häfoffer och edars offers förstling, med allt det I mig helgen.
Pakuti pa phiri langa lopatulika, phiri lalitali la ku Israeli, akutero Ambuye Yehova, Aisraeli onse adzanditumikira, ndipo kumeneko Ine ndidzawalandira. Kumeneko ndidzayembekeza zopereka zanu ndi mphatso zanu zopambana, pamodzi ndi nsembe zanu zonse zopatulika.
41 I skolen varda mig tacknämlige med sötom rök, när jag låter eder komma ifrå folken, och varder eder församlande utu landen, dit I förströdde ären, och jag skull varda helgad i eder för Hedningomen.
Ndidzakulandirani ngati nsembe ya fungo lokoma ndikadzakutulutsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukusokhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munabalalitsidwirako. Motero ndidzadzionetsa pakati panu kuti ndine woyera ndipo mitundu ya anthu idzaona.
42 Och I skolen förnimma, att jag är Herren, när jag hafver låtit eder komma in uti Israels land, uti det land, om hvilket jag upphof mina hand, att jag det edra fäder gifva skulle.
Tsono mudzadziwa kuti ndine Yehova ndikadzabwera nanu ku dziko la Israeli, dziko limene ndinalumbira kuti ndidzapereka kwa makolo anu.
43 Der skolen I tänka uppå edart väsende, och uppå all edar handel, der I utinnan orenade ären, och skolen hafva ett misshag till all edor ondsko, som I bedrifvit hafven;
Kumeneko mudzakumbukira makhalidwe anu ndi machitidwe anu onse amene munadziyipitsa nawo, ndipo mudzanyansidwa nokha chifukwa cha zoyipa zimene munachita.
44 Och skolen förnimma, att jag är Herren, när jag gör med eder för mitt Namns skull, och icke efter edart onda väsende och skadeliga handel, du Israels hus, säger Herren Herren.
Inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzakuchitirani zabwino chifukwa cha dzina langa koma osati molingana ndi njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu okhota, inu Aisraeli, akutero Ambuye Yehova.’”
45 Och Herrans ord skedde till mig, och sade:
Yehova anandiyankhula nati:
46 Du menniskobarn, ställ ditt ansigte emot Theman, och tala söderut, och prophetera emot den skogen i den markene söderut.
“Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane kummwera; ndipo lalika mawu odzudzula anthu akummwera ndipo unenere zodzudzula dziko la nkhalango ya kummwera.
47 Och säg till den skogen söderut: Hör Herrans ord. Detta säger Herren Herren: Si, jag skall upptända i dig en eld, han skall förtära både färsk trä och torr, så att man icke skall kunna utsläcka hans låga; utan allt det som ifrå sunnan norråt står, det skall uppbrändt varda.
Iwuze nkhalango yakummwera kuti, ‘Imvani mawu a Yehova! Ambuye Yehova akuti: Ndikuyatsa moto ndipo motowo udzapsereza mitengo yako yonse yayiwisi ndi yowuma yomwe. Malawi ake sadzazimitsika ndipo aliyense kuchokera kummwera mpaka kumpoto adzapsa nawo.
48 Och allt kött skall se att jag, Herren, det upptändt hafver, och ingen det utsläcka kan.
Aliyense adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndayatsa motowo, ndipo sudzazimitsidwa.’”
49 Och jag sade: Ack Herre Herre! de säga om mig: Denne talar icke annat än förtäckt ord:
Ndipo ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova! Anthu akungondinena kuti, ‘Kodi suja amangonena nthano chabe ameneyu!’”

< Hesekiel 20 >