< Hesekiel 18 >

1 Och Herrans ord skedde till mig, och sade:
Yehova anandiyankhula nati:
2 Hvad drifven I ibland eder, uti Israels land, detta ordspråket, och sägen: Fäderna hafva ätit sura vindrufvor, men barnomen äro tänderna deraf ömma vordna?
“Kodi anthu inu mumatanthauza chiyani mukamabwerezabwereza kunena mwambi uwu wokhudza dziko la Israeli kuti: “‘Nkhuyu zodya akulu zimapota ndi ana omwe?’”
3 Så sant som jag lefver; säger Herren Herren, sådant ordspråk skall intet mer gå ibland eder i Israel;
“Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, simudzanenanso mwambi umenewu mu Israeli.
4 Ty si, alla själar äro mina; fadrens själ är så väl min, som, sonens själ; hvilken själ som syndar, hon skall dö.
Pakuti moyo uliwonse ndi wanga. Moyo wa abambo ndi wanga, wamwananso ndi wanga. Munthu wochimwa ndi amene adzafe.
5 Om nu en menniska är from, den der rätt och väl gör;
“Tiyerekeze kuti pali munthu wolungama amene amachita zolungama ndi zolondola.
6 Den på bergomen icke äter, den sin ögon icke upphäfver till Israels hus afgudar; och sina nästas hustru icke besmittar, och icke ligger när qvinno uti hennes krankhet;
Iye sadyera nawo pa mapiri a chipembedzo kapena kupembedza mafano a Aisraeli. Iye sayipitsa mkazi wa mnzake kapena kugonana ndi mkazi pamene akusamba.
7 Den ingom skada gör; den gäldenäromen sin pant igengifver; den ingom något ifråtager med våld; den sitt bröd delar med dem hungroga, och kläder den nakota;
Iye sapondereza munthu wina aliyense, koma amabwezera wangongole nʼchigwiriro chake. Iye salanda zinthu za osauka, koma amapereka chakudya kwa anthu anjala, ndipo amapereka zovala kwa anthu ausiwa.
8 Den intet ockrar; den ingen slem vinning tager; den icke hjelper till att göra orätt; den emellan menniskorna rätt dömer;
Iye sakongoletsa ndalama mwa katapira, kapena kulandira chiwongoladzanja chachikulu. Amadziletsa kuchita zoyipa ndipo sakondera poweruza milandu.
9 Den efter mina rätter vandrar, och min bud håller, så att han allvarliga gör derefter; det är en from man, han skall få lefva, säger Herren Herren.
Iye amatsatira malangizo anga, ndipo amasunga malamulo anga mokhulupirika. Munthu ameneyo ndi wolungama; iye adzakhala ndithu ndi moyo, akutero Ambuye Yehova.
10 Men om han föder en son, och den samme varder en mördare, den der blod utgjuter, eller något af dessa stycke gör;
“Tiyerekeze kuti munthu wolungama chotere wabala mwana chimbalangondo amene amakhalira kupha anthu ndi kuchita zinthu zina zotere.
11 Och intet af de andra stycken gör; utan äter på bergom, och besmittar sins nästas hustru;
Iye nʼkumachita zinthu zimene ngakhale abambo ake sanachitepo. “Amadyera nawo ku mapiri achipembedzo. Amayipitsa mkazi wa mnzake.
12 Gör dem fattiga och elända skada; tager något med våld; icke igengifver pant; upphäfver sin ögon till afgudar, dermed han en styggelse bedrifver;
Iye amapondereza munthu wosauka ndi wosowa. Amalanda zinthu za osauka. Sabweza chikole cha munthu wa ngongole. Iye amatembenukira ku mafano nachita zonyansa.
13 Får ut på ocker; tager vinning; skulle han lefva? Han skall icke lefva; utan efter han sådana styggelse gjort hafver, så skall han döden dö; hans blod skall vara öfver honom.
Iye amakongoletsa mwa katapira ndipo amalandira chiwongoladzanja chachikulu. Kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu! Chifukwa wachita zinthu zonyansa zonsezi, adzaphedwa ndipo adzalandira chilango chomuyenera.
14 Men om han föder en son, den der alla sådana synder ser, som hans fader gör, och han fruktar sig, och så icke gör;
“Tsono tiyerekeze kuti munthu woyipa uyu wabala mwana amene amaona machimo onse amene abambo ake ankachita. Ngakhale amaona koma osatsanzira ntchito zake zoyipazo.
15 Äter icke på bergom; upphäfver icke sin ögon till Israels hus afgudar; besmittar icke sins nästas hustru;
“Sadyera nawo pa mapiri achipembedzo. Sapembedza mafano a ku Israeli. Sayipitsa mkazi wa mnzake.
16 Gör ingom skada; behåller icke pant; tager intet med våld; delar sitt bröd med dem hungroga, och kläder den nakota;
Sapondereza munthu wina aliyense. Satenga chikole akabwereketsa chinthu. Salanda zinthu za osauka. Salanda zinthu za munthu. Amapereka chakudya kwa anthu anjala. Amapereka zovala kwa anthu aumphawi.
17 Hjelper icke emot den elända; tager intet ocker eller slem vinning; utan håller min bud, och lefver efter mina rätter; han skall intet dö för sins faders missgernings skull, utan lefva.
Amadziletsa kuchita zoyipa. Sakongoletsa kuti apezepo phindu. Salandira chiwongoladzanja. Amasunga malangizo anga ndi kumvera malamulo anga. Munthu wotereyo sadzafa chifukwa cha machimo a abambo ake. Adzakhala ndi moyo ndithu.
18 Men hans fader, den våld och orätt brukat hafver, och ibland sitt folk; det som intet doger, gjort hafver: si, han skall dö för sina missgernings skull.
Koma abambo ake, popeza kuti anazunza anthu ena ndi kubera mʼbale wawo ndiponso popeza kuti sanachitire zabwino anansi ake, adzafera machimo ake omwe.
19 Så sägen I: Hvi skall sonen icke bära sins faders missgerning? Derföre, att han hafver gjort rätt och väl, och hållit och gjort alla mina rätter, skall han lefva.
“Mwina inu mukhoza kufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mwana salangidwa chifukwa cha kulakwa kwa abambo ake? Ayi, mwanayo adzakhala ndi moyo chifukwa ankachita zolungama ndi zolondola ndipo ankasamala kumvera malamulo anga onse.
20 Ty hvilken själ som syndar, hon skall dö; sonen skall icke bära fadrens missgerning; och fadren skall icke bära sonens missgerning, utan dens rättfärdigas fromhet skall vara öfver honom, och dens orättfärdigas arghet skall vara öfver honom.
Munthu wochimwa ndiye amene adzafe. Mwana sadzapezeka wolakwa chifukwa cha abambo ake, kapena abambo kupezeka wolakwa chifukwa cha mwana wawo. Chilungamo cha munthu wolungama ndicho chidzamupulutse, ndipo kuyipa kwa munthu wochimwa ndiko kudzamuwonongetse.
21 Men om en ogudaktig omvänder sig ifrån alla sina synder, som han gjort hafver, och håller alla mina rätter, och gör rätt och väl, så skall han lefva, och icke dö.
“‘Munthu woyipa akatembenuka mtima ndi kusiya machimo amene ankachita ndi kuyamba kumvera malamulo anga ndi kumachita zolungama ndi zokhulupirika, ndiye kuti adzakhala ndi moyo. Sadzafa ayi.
22 Men på all hans öfverträdelse, som han gjort hafver, skall intet tänkt varda; utan skall lefva, för den rättfärdighets skull, som han gör.
Zoyipa zake zonse zidzakhululukidwa. Chifukwa cha zinthu zolungama zimene anazichita adzakhala ndi moyo.
23 Menar du, att jag lust hafver öfver dens ogudaktigas död, säger Herren Herren, och icke mycket mer, att han omvänder sig ifrå sitt onda väsende, och lefver?
Kodi Ine ndimakondwera ndi imfa ya munthu woyipa? Ayi, ndimakondwera pamene woyipa watembenuka mtima kuti akhale ndi moyo. Akutero Ambuye Yehova.
24 Och om den rättfärdige vänder sig ifrå sine rättfärdighet, och gör det ondt är, och lefver efter all den styggelse som en ogudaktig gör, skulle han lefva? Ja, all hans rättfärdighet, som han gjort hafver, skall intet ihågkommen varda; utan han skall dö uti sin öfverträdelse och syndom, som han gjort hafver.
“‘Koma ngati munthu wolungama apatuka kusiya zachilungamo ndi kuyamba kuchita tchimo ndi zonyansa za mtundu uliwonse zimene amachita anthu oyipa, kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu, zolungama zake zonse sizidzakumbukiridwa. Iye adzayenera kufa chifukwa cha machimo amene anachita.
25 Och ändå sägen I: Herren handlar icke rätt. Derföre hörer nu, I af Israels hus: Hafver jag icke rätt, och I orätt?
“Komabe inu mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Tamvani tsono inu Aisraeli: Kodi zochita zanga ndizo zosalungama? Kodi si zochita zanu zimene ndi zosalungama?
26 Ty när den rättfärdige vänder sig ifrå sine rättfärdighet, och gör det ondt är, så måste han dö; men han måste dö för sina ondskos skull, som han gjort hafver.
Ngati munthu wolungama atembenuka kusiya chilungamo chake ndi kuchita tchimo, iye adzafa chifukwa cha tchimolo.
27 Tvärtom, när den ogudaktige vänder sig ifrå sine orättfärdighet, som han gjort hafver, och gör nu rätt och väl, han varder behållandes sina själ lefvande.
Koma ngati munthu woyipa aleka zoyipa zake zimene anazichita ndi kuyamba kuchita zimene ndi zolungama ndi zolondola, iye adzapulumutsa moyo wake.
28 Ty efter han fruktar sig, och vänder åter af sine ondsko, så skall han lefva, och icke dö.
Popeza waganizira za zolakwa zonse ankachita ndipo wazileka, iye adzakhala ndi moyo ndithu; sadzafa.
29 Och ännu säga de af Israels hus: Herren handlar icke rätt. Skulle jag hafva orätt? I af Israels hus hafven orätt.
Komabe Aisraeli akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Kodi zochita zanga ndizo zopanda chilungamo, inu Aisraeli? Kodi si zochita zanu zimene ndi zopanda chilungamo?
30 Derföre vill jag döma eder, I af Israels hus, hvar och en efter hans väsende, säger Herren Herren. Derföre vänder eder om, och låter eder omvända, på det I icke skolen falla för missgerningenes skull.
“Chifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: inu Aisraeli, Ine ndidzakuweruzani aliyense wa inu molingana ndi ntchito zake. Lapani! Lekani zoyipa zanu kuti musawonongeke nazo.
31 Kaster ifrån eder all edor öfverträdelse, der I med öfverträdt hafven, och görer eder ett nytt hjerta, och ny anda; ty hvi vill du så dö, du Israels hus?
Tayani zolakwa zanu zonse zimene munandichimwira nazo ndipo khalani ndi mtima watsopano ndi mzimu watsopano. Kodi muferanji inu Aisraeli?
32 Ty jag hafver ingen lust till hans död, som dör, säger Herren Herren; derföre omvänder eder, så fån I lefva.
Ine sindikondwera ndi imfa ya munthu aliyense, akutero Ambuye Yehova. Chifukwa chake, lapani kuti mukhale ndi moyo.”

< Hesekiel 18 >