< 2 Mosebok 9 >
1 Herren sade till Mose: Gack in till Pharao, och säg till honom: Detta säger Herren de Ebreers Gud: Släpp mitt folk, att de måga tjena mig.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Pita kwa Farao ndipo ukamuwuze kuti Yehova, Mulungu wa Ahebri akuti alole anthu anga apite kuti akandipembedze.
2 Hvar du icke vill, utan förhåller dem länger;
Koma ngati ukana kuti apite ndi kupitiriza kuwaletsa,
3 Si, så skall Herrans hand varda utöfver din boskap på markene; öfver hästar, öfver åsnar, öfver camelar, öfver oxar, öfver får, med en ganska stor pestilentie.
dzanja la Yehova lidzakantha ziweto zako zimene zili ku munda, pamodzi ndi akavalo, abulu, ngamira, ngʼombe, nkhosa ndi mbuzi ndi mliri woopsa kwambiri.
4 Och Herren skall göra ett besynnerligit emellan de Israeliters boskap, och de Egyptiers; så att intet skall dö utaf allt det som Israels barn hafva.
Koma Yehova adzasiyanitsa pakati pa ziweto za Israeli ndi ziweto za Igupto, kotero kuti palibe chiweto nʼchimodzi chomwe cha Aisraeli chimene chidzafe.”
5 Och Herren lade en tid före, och sade: I morgon skall Herren göra detta på jordene.
Yehova anayika nthawi ndipo anati, “Yehova adzachita zimenezi mmawa mʼdziko muno.”
6 Och Herren gjorde så om morgonen, och allahanda boskap blef död för de Egyptier; men af Israels barns boskap blef icke ett dödt.
Ndipo mmawa mwake Yehova anachitadi zimenezi. Ziweto zonse za Aigupto zinafa, koma palibe chiweto ndi chimodzi chomwe cha Aisraeli chomwe chinafa.
7 Och Pharao sände derefter, och si, der var icke ett blifvet dödt utaf Israels boskap. Men Pharaos hjerta vardt förstockadt, och släppte icke folket.
Farao anatuma anthu kuti akafufuze ndipo anapeza kuti palibe chiweto chilichonse cha Aisraeli chomwe chinafa. Komabe mtima wake sunagonje ndipo iye sanalole kuti anthu apite.
8 Då sade Herren till Mose och Aaron: Tager edra händer fulla med sot utaf skorstenen, och Mose stänke det upp åt himmelen för Pharao;
Kenaka Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Tapani phulusa la pa moto lodzaza dzanja ndipo Mose aliwaze mmwamba pamaso pa Farao.
9 Att stoft skall komma öfver hela Egypti land, och bölder och ond sår varda på menniskor, och på boskap i hela Egypti lande.
Phulusalo lidzasanduka fumbi pa dziko lonse la Igupto. Tsono fumbilo lidzasanduka zithupsa zomaphulika nʼkukhala zilonda pa munthu aliyense ndi pa nyama zomwe mʼdziko lonse la Igupto.”
10 Och de togo sotet utaf skorstenen, och stodo för Pharao, och Mose stänktet upp åt himmelen. Då vordo bölder och ond sår på menniskom, och på boskapen;
Kotero anatenga phulusa la pa moto ndi kuyima pamaso pa Farao. Mose analiwaza mmwamba, ndipo panabuka zotupa zophulika zokha pa munthu aliyense ndi pa ziweto.
11 Så att trollkarlarne icke kunde stå för Mose, för de bölders skull; ty på trollkarlarne voro ock så väl bölder, som på alla Egyptier.
Amatsenga sanathe kumuyandikira Mose chifukwa nawonso anali ndi zithupsa monga mmene analili Aigupto ena onse.
12 Men Herren förstockade Pharaos hjerta, så att han intet hörde dem, såsom Herren Mose sagt hade.
Koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao ndipo iye sanamvere Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova anamuwuzira Mose.
13 Då sade Herren till Mose: Statt bittida upp om morgonen, och gack fram för Pharao, och säg till honom: Detta säger Herren de Ebreers Gud: Släpp mitt folk, att de måga tjena mig.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Mawa mmawa upite ukakumane ndi Farao maso ndi maso ndipo ukamuwuze kuti Yehova Mulungu wa Ahebri akuti ulole anthu anga apite kuti akandipembedze.
14 Annars vill jag i denna resone sända alla mina plågor öfver dig, öfver dina tjenare, och öfver ditt folk; att du skall förnimma, att i all land är ingen min like.
Ngati suwalola, tsopano ndidzagwetsa miliri yanga yonse pa iwe ndi nduna zako ndiponso pa anthu ako, kuti udziwe kuti palibe wina wofanana nane pa dziko lonse lapansi.
15 Förty nu vill jag uträcka mina hand, och slå dig och ditt folk med pestilentie, att du skall förgås af jordene.
Pakuti ndikanakhala nditatukula kale dzanja langa ndikupheratu iwe pamodzi ndi anthu ako onse pa dziko lapansi.
16 Dock fördenskull hafver jag uppväckt dig, att min kraft skall synas på dig, och mitt Namn kunnigt varda i all land.
Koma ndakuyika kukhala mfumu ndi cholinga choti ndionetse mphamvu zanga kwa iwe ndiponso kuti dzina langa litchuke pa dziko lonse lapansi.
17 Du förhåller ännu mitt folk, och vill icke släppat.
Komabe iwe ukudzitukumula pa anthu anga osawalola kuti atuluke.
18 Si, jag vill i morgon på denna tiden låta komma ett mägtigt stort hagel, hvilkets like icke varit hafver i Egypten, ifrå den tid det funderadt vardt, intill nu.
Nʼchifukwa chake mawa, nthawi ngati ino, ndidzagwetsa matalala amphamvu amene sanagwepo pa Igupto, kuyambira pachiyambi mpaka lero.
19 Så sänd nu bort, och förvara din boskap, och allt det du på markene hafver; ty alla menniskor och boskap, som på markene funnen varder, och icke inhemtad är i husen, och haglet faller på dem, de blifva döde.
Tsopano lamula kuti ziweto zanu zonse ndi zinthu zonse zomwe zili ku minda kuti zilowetsedwe mʼkhola, chifukwa matalala adzagwera munthu aliyense ndi chiweto chilichonse chimene sichidzalowetsedwa mʼkhola ndipo zimene zidzakhala zili ku munda zidzafa.”
20 Den som nu ibland Pharaos tjenare fruktade Herrans ord, han lät sina tjenare och boskap fly in i husen;
Nduna za Farao zinachita mantha ndi mawu a Yehova, ndipo zinalowetsa antchito awo ndi ziweto zawo mʼnyumba.
21 Men hvilkas hjerta intet aktade Herrans ord, de läto deras tjenare och boskap blifva på markene.
Koma iwo amene ananyozera mawu a Yehova anasiya akapolo ndi ziweto zawo panja.
22 Då sade Herren till Mose: Räck dina hand upp åt himmelen, att det haglar öfver hela Egypti land; öfver menniskor, öfver boskap, och öfver all gröda på markene i Egypti lande.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Kweza dzanja lako kumwamba kuti matalala agwe pa dziko lonse la Igupto, pa munthu aliyense, pa ziweto ndi pa zonse zomera mʼminda ya Igupto.”
23 Så räckte Mose sin staf upp emot himmelen, och Herren lät dundra och hagla, så att elden flög på jordene. Alltså lät Herren komma hagel öfver Egypti land;
Mose ataloza ndodo yake kumwamba, Yehova anatumiza mabingu ndi matalala ndi ziphaliwali zongʼanima pa nthaka. Kotero Yehova anagwetsa matalala pa dziko la Igupto.
24 Att hagel och eld foro ibland hvartannat så grufveliga, att dess like icke varit hade i hela Egypti lande, ifrå den tid att det med folk besatt vardt.
Matalala anagwa ndipo ziphaliwali zinangʼanima. Inali mphepo ya mkuntho yoopsa kwambiri imene sinakhaleponso mʼdziko lonse la Igupto chiyambire pamene Aigupto anakhala mtundu woyima pa okha.
25 Och haglet slog i hela Egypti lande allt det på markene var, både menniskor och boskap, och slog allan grödan på markene, och sönderslog all trä på markene;
Matalala anawononga dziko lonse la Igupto, munthu aliyense pamodzi ndi ziweto. Matalala aja anawononga zomera zonse za mʼmunda ndi kukhadzula mtengo uliwonse.
26 Utan allena i det landet Gosen, der Israels barn voro, der haglade intet.
Ku malo kokhako kumene matalala sanafikeko ndi dera la Goseni kumene kunali Aisraeli.
27 Då sände Pharao bort, och lät kalla Mose och Aaron, och sade till dem: Jag hafver i denna resone syndat; Herren är rättfärdig, men jag och mitt folk äre ogudaktige.
Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati kwa iwo, “Tsopano ndachimwa, Yehova ndi wolungama, ine ndi anthu anga ndife olakwa.
28 Derföre beder Herran, att Guds dunder och hagel återvänder, så vill jag släppa eder, och icke länger förhålla eder.
Upemphere kwa Mulungu chifukwa mabingu ndi matalala atikwana. Ine ndidzakulolani kuti mupite. Simuyenera kukhalabe kuno.”
29 Mose sade till honom: När jag kommer utu stadenom, vill jag uträcka mina händer till Herran, så skall dundret återvända, och intet hagel mera vara; på det du skall förnimma, att jorden är Herrans.
Mose anayankha, “Ndikangotuluka mu mzinda muno, ine ndidzakweza manja anga kwa Yehova ndi kupemphera. Mabingu ndi matalalawa adzaleka ndipo inu mudzadziwa kuti Yehova ndiye akulamulira dziko lapansi.
30 Dock vet jag väl, att du och dine tjenare icke ännu frukten för Herran Gud.
Koma ine ndikudziwa kuti inu ndi nduna zanu simukuopabe Yehova Mulungu.”
31 Så vardt då slaget linet och bjugget; ty bjugget var i ax gånget, och linet hade knoppat sig.
Thonje ndi barele zinawonongeka, popeza barele anali atakhwima ndi thonje linali ndi maluwa.
32 Men hvetet och rågen vardt icke slaget; förty det var sensäd.
Koma tirigu ndi mchewere sizinawonongeke chifukwa zimakhwima mochedwa.
33 Så gick då Mose ifrå Pharao ut af stadenom, och räckte sina händer ut till Herran; och dundret och haglet vände igen, och regnet dröp intet mer på jordena.
Mose anasiyana ndi Farao natuluka mu mzindawo. Iye anakweza manja ake kwa Yehova. Mabingu ndi matalala zinaleka, ndipo mvula inalekeratu kugwa mʼdzikolo.
34 Då nu Pharao såg, att regnet, och dundret, och haglet vände igen, syndade han ändå ytterligare, och förhärdade sitt hjerta, han och hans tjenare.
Farao ataona kuti mvula, matalala ndi mabingu zaleka, anachimwanso. Iye ndi nduna zake anawumitsanso mitima yawo.
35 Alltså vardt Pharaos hjerta förstockadt, att han icke släppte Israels barn, såsom Herren sagt hade genom Mose.
Choncho Farao sanalole kuti Aisraeli apite monga momwe Yehova anamuwuzira Mose.