< 2 Mosebok 35 >
1 Och Mose församlade hela menighetena af Israels barn, och sade till dem: Detta är det som Herren budit hafver, att I göra skolen:
Mose anasonkhanitsa gulu lonse la Aisraeli ndipo anawawuza kuti, “Zinthu zimene Yehova wakulamulirani kuti muzichite ndi izi:
2 I sex dagar skolen I arbeta; men den sjunde dagen skolen I hålla heligan, Herrans hvilos Sabbath. Den som något arbete gör på honom, han skall dö.
Muzigwira ntchito zanu pa masiku asanu ndi limodzi, koma tsiku la chisanu ndi chiwiri likhale la Sabata, tsiku lanu lopuma, lopatulika kwa Yehova. Aliyense amene adzagwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuphedwa.
3 I skolen ingen eld upptända på Sabbathsdagenom i alla edra boningar.
Pa tsiku la Sabata musakoleze moto paliponse pamene mukhala.”
4 Och Mose sade till alla menighetena af Israels barn: Detta är det Herren budit hafver:
Mose ananena kwa gulu lonse la Aisraeli kuti, “Zimene Yehova wakulamulirani ndi izi:
5 Gifver ibland eder häfoffer Herranom, alltså att hvar och en frambär häfoffer Herranom af ett fritt hjerta, guld, silfver, koppar;
Kuchokera pa zomwe muli nazo, mutenge chopereka cha Yehova. Aliyense amene ali ndi mtima wofuna kupereka abweretse kwa Yehova zopereka izi: Golide, siliva ndi mkuwa;
6 Gult silke, skarlakan, rosenrödt, hvitt silke, och getahår;
nsalu zobiriwira, zapepo, zofiira, nsalu zofewa; ubweya wambuzi;
7 Rödlett vädurskinn och tackskinn, furoträ;
zikopa za nkhosa zazimuna za utoto wofiira ndi zikopa za akatumbu; matabwa amtengo wa mkesha,
8 Oljo till lamporna, och speceri till smörjoolja, och till godt rökverk;
mafuta anyale a olivi, zonunkhiritsa mafuta odzozera ndi zopangira lubani wonunkhira;
9 Onich och infattade stenar till lifkjortelen, och till skölden.
miyala yokongola ya mtundu wa onikisi ndi ina yabwino yoyika pa Efodi ndi pa chovala cha pachifuwa.
10 Och den ibland eder förståndig är, han komme och göre hvad Herren budit hafver;
“Anthu onse aluso pakati panu abwere ndi kupanga zonse zimene Yehova walamula:
11 Nämliga tabernaklet med dess täckelse och öfvertäckelse; ringar, bräder, skottstänger, stolpar och fötter;
Chihema ndi tenti yake ndiponso chophimba chake, ngowe zake, maferemu ake, mitanda yake, mizati yake ndi matsinde ake;
12 Arken med hans stänger; nådastolen och förlåten;
Bokosi la Chipangano pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira ndiponso chovundikira chake cha bokosilo ndi nsalu zophimba bokosilo;
13 Bordet med sina stänger, och all dess tyg och förlåten;
tebulo pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira pamodzi ndi zipangizo zake zonse ndiponso buledi wokhala pamaso pa Yehova;
14 Ljusastakan till att lysa, och hans redskap, och hans lampor, och oljo till lysning;
choyikapo nyale yowunikira pamodzi ndi zipangizo zake, nyale ndi mafuta anyalezo;
15 Rökaltaret med sina stänger, smörjooljan, och speceri till rökverk; klädet för tabernaklets dörr;
guwa lofukizira lubani pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira, mafuta odzozera ndi lubani onunkhira; nsalu yotchinga pa khomo lolowera mʼchihema;
16 Bränneoffersaltaret med dess koppargallrar, stänger och all sin redskap; tvättekaret med sin fot;
guwa lansembe yopsereza pamodzi ndi sefa yamkuwa, mitengo yake yonyamulira ndi zipangizo zake zonse, beseni losambira lamkuwa ndi miyendo yake;
17 Bonaden till gården, med sina stolpar och fötter; och klädet till dörrena åt gårdenom;
nsalu yotchingira bwalo pamodzi ndi mizati yake ndi matsinde ake, ndiponso nsalu yotchingira pa khomo lolowera ku bwalo;
18 Pålarna till tabernaklet och till gården, med deras tåg;
zikhomo za tenti ya chihema ndiponso za bwalo, ndi zingwe zake;
19 Ämbetskläden till tjensten i det helga; de helga kläder till Presten Aaron, med hans söners kläder till Presterskapet.
zovala zolukidwa zovala potumikira kumalo opatulika, zovala zopatulika za wansembe, Aaroni pamodzi ndi za ana ake aamuna pamene akutumikira monga ansembe.”
20 Då gick hela menigheten af Israels barn ut ifrå Mose.
Kenaka gulu lonse la Aisraeli linachoka pamaso pa Mose,
21 Och alle de som gerna och välviljeliga gåfvo, kommo och båro det fram till ett häfoffer Herranom, till vittnesbördsens tabernakels verk, och till all dess tjenste, och till de helga kläden.
ndipo aliyense amene anakhudzidwa mu mtima mwake nafuna kupereka, anabwera kudzapereka chopereka kwa Yehova cha ntchito yokonza tenti ya msonkhano, cha ntchito zonse za mʼtentimo ndi cha zovala zopatulika.
22 Både man och qvinna båro fram, hvilken som helst dertill hade vilja, spänner, örnaringar, ringar och spann, och allahanda gyldene redskap; bar ock hvar man fram guld, till veftoffer Herranom.
Onse amene anali ndi mtima wofuna, amuna ndi amayi omwe anabwera kudzapereka zodzikometsera zagolide za mtundu uliwonse: zomangira zovala, ndolo, mphete ndi zokometsera. Onse anapereka golide wawo monga nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
23 Och den som när sig fann gult silke, skarlakan, rosenrödt, hvitt silke, getahår, rödlett vädurskinn och tackskinn, han bar det fram.
Aliyense amene anali ndi nsalu ya mtundu wa mtambo, yapepo kapena yofiira kapena yofewa, yosalala, kapena ubweya wambuzi, zikopa za nkhosa zonyika mu utoto wofiira kapena zikopa anazibweretsa.
24 Och den som silfver eller koppar hof, han bar det fram Herranom till häfoffer. Och den som fann furoträ när sig, han bar det fram till allahanda Gudstjenstens verk.
Onse amene anapereka chopereka cha siliva kapena mkuwa anabweretsa monga chopereka kwa Yehova. Ndipo aliyense amene anali ndi matabwa a mtengo wa mkesha kuti awagwiritse ntchito mbali ina iliyonse ya ntchitoyo, anabweretsa.
25 Och de der förståndiga qvinnor voro, de virkade med sina händer, och båro sitt verk fram af gult silke, skarlakan, rosenrödt, och hvitt silke.
Mayi aliyense waluso analuka ndi manja ake ndi kubweretsa chomwe analuka cha mtundu wa mtambo, chapepo kapena chofiira kapena chofewa, chosalala.
26 Och de qvinnor, som skickeliga voro, de virkade getahår.
Ndipo amayi onse amene anali ndi mtima wofuna ndipo anali ndi luso analuka ubweya wa mbuzi.
27 Men förstarna båro fram onich, och infattade stenar till lifkjortelen och till skölden;
Atsogoleri anabweretsa miyala ya onikisi ndi miyala yokongola yoyika pa efodi ndi chovala chapachifuwa.
28 Och speceri och oljo till lysning, och till smörjo, och till godt rökverk.
Anabweretsanso zonunkhiritsa ndiponso mafuta owunikira a olivi ndi odzozera ndi zofukizira zonunkhira.
29 Alltså båro Israels barn fram Herranom friviljoge, både män och qvinnor, till allahanda verk, som Herren budit hade genom Mose, att göras skulle.
Aisraeli onse aamuna ndi aakazi amene anali ndi mtima wofuna, anabweretsa kwa Yehova chopereka chaufulu ku ntchito yonse ya Yehova imene analamulira kudzera mwa Mose kuti achite.
30 Och Mose sade till Israels barn: Ser, Herren hafver kallat Bezaleel vid namn, Uri son, Hurs sons, af Juda slägte;
Kenaka Mose anati kwa Aisraeli, “Taonani, Yehova wasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda,
31 Och hafver uppfyllt honom med Guds Anda, att han är vis, förståndig, och skickelig till allahanda verk;
ndipo wamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi:
32 Till att konsteliga arbeta på guld, silfver och koppar;
Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa,
33 Snida, och insätta ädla stenar; till att timbra af trä; till att göra allt konsteligit arbete;
kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja.
34 Och hafver gifvit honom undervisning i hans hjerta; samt med Aholiab, Ahisamachs son, af Dans slägte.
Ndipo Iye wapereka kwa Bezaleli pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani luso lophunzitsa ena.
35 Han hafver uppfyllt deras hjerta med vishet, till att göra allahanda verk, till att snida, virka och sticka, med gult silke, skarlakan, rosenrödt, och hvitt silke, och med väfvande, så att de göra allahanda verk, och konsteligit arbete påfinna.
Mulungu wawapatsa maluso osiyanasiyana, maluso ogoba, olemba ndondomeko, opeta zokometsera pa nsalu zamtundu wamtambo, zapepo ndi zofiira ndiponso zofewa zosalala ndi zoluka. Onsewa ndi amisiri a ntchito zamanja ndi zokonza ndondomeko.