< 2 Mosebok 31 >
1 Och Herren talade med Mose, och sade:
Ndipo Yehova anati kwa Mose,
2 Si, jag hafver vid namn kallat Bezaleel, Uri son, Hurs sons, af Juda slägte;
“Taona, ndasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda.
3 Och hafver fyllt honom med Guds Anda; med vishet och förstånd, och konst, och med allahanda verk;
Ndipo ndamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi:
4 Konsteliga till att arbeta på guld, silfver, koppar;
Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa,
5 Konsteliga utskära och insätta stenar, och konsteliga timbra på trä; till att göra allahanda verk.
kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja.
6 Och si, jag hafver fått honom till hjelp Aholiab, Ahisamachs son, af Dans slägte; och hafver hvarjom och enom visom gifvit visdom i hjertat, att de göra skola allt det jag dig budit hafver:
Ndasankhanso Oholiabu mwana wa Ahisamaki wa fuko la Dani. Ndiponso ndapereka nzeru kwa anthu aluso motero adzagwira ntchito zonse zimene ndakulamulira kuti zichitike monga izi:
7 Vittnesbördsens tabernakel, vittnesbördsens ark, nådastolen deruppå, och all tabernaklens tyg;
Kupanga tenti ya msonkhano, bokosi laumboni pamodzi ndi chophimbira chake, ndiponso zonse za mu tenti,
8 Bordet och dess tyg; den sköna ljusastakan och all hans tyg; rökaltaret;
tebulo ndi zida zake, choyikapo nyale cha golide wabwino kwambiri ndi ziwiya zake zonse, guwa lofukizirapo lubani,
9 Bränneoffersaltaret med all sin tyg; tvättekaret med sinom fot;
guwa lansembe yopsereza ndi ziwiya zake zonse, beseni ndi nsichi yake,
10 Ämbetskläden, och de helga kläden Prestens Aarons, och hans söners kläder, till att tjena i Presterskapena;
ndiponso zovala zonse zolukidwa, zovala zopatulika za Aaroni wansembe pamodzi ndi za ana ake, zovala pamene akutumikira monga ansembe,
11 Smörjooljona och rökverk af speceri till helgedomen. Allt det jag hafver budit dig, skola de göra.
ndiponso mafuta odzozera ndi lubani wonunkhira wa ku malo opatulika. Iwo azipanga monga momwe Ine ndinakulamulira.”
12 Och Herren talade med Mose, och sade:
Ndipo Yehova anati kwa Mose,
13 Tala till Israels barn, och säg: Håller min Sabbath; ty han är ett tecken emellan mig och eder, intill edra efterkommande, att I skolen veta, att jag är Herren, den eder helgar.
“Uza ana a Israeli kuti azisunga Masabata anga. Ichi chidzakhala chizindikiro pakati pa inu ndi Ine pamodzi ndi zidzukulu zanu mʼtsogolomo, chosonyeza kuti Ine ndine amene ndimakuyeretsani.
14 Derföre håller min Sabbath; ty han skall vara eder helig. Den som ohelgar honom, han skall döden dö; den som gör något arbete på honom, hans själ skall utrotad varda utu hans folk.
“Motero muzisunga tsiku la Sabata chifukwa ndi loyera kwa inu. Aliyense amene adetsa tsiku la Sabata ayenera kuphedwa. Aliyense amene agwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
15 Sex dagar skall man arbeta; men på sjunde dagen är Sabbath, Herrans helga hvila. Den som något arbete gör på Sabbathsdagen, han skall döden dö.
Mugwire ntchito kwa masiku asanu ndi limodzi koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, lopuma, tsiku lopatulika la Yehova. Aliyense amene agwira ntchito iliyonse pa tsiku la Sabata ayenera kuphedwa.
16 Derföre skola Israels barn hålla Sabbath, att de med deras efterkommande hålla honom till ett evigt förbund.
Aisraeli onse komanso zidzukulu zawo mʼtsogolo azidzasunga tsiku la Sabata ngati pangano lamuyaya.
17 Han är ett evigt tecken emellan mig och Israels barn. Ty i sex dagar gjorde Herren himmel och jord, men på sjunde dagen höll han upp, och hvilte sig.
Tsiku la Sabata lidzakhala chizindikiro chamuyaya pakati pa Ine ndi Aisraeli chosonyeza kuti Yehova analenga za kumwamba ndi dziko lapansi kwa masiku asanu ndi limodzi ndi kuti pa tsiku lachisanu ndi chiwiri analeka kugwira ntchito napumula.”
18 Och då han hade uttalat med Mose på Sinai berg, gaf han honom två vittnesbördsens taflor; de voro af sten, och skrifna med Guds finger.
Yehova atamaliza kuyankhula ndi Mose pa phiri la Sinai, anamupatsa Mose miyala iwiri yaumboni, imene Mulungu analembapo ndi chala chake.