< 2 Mosebok 27 >

1 Och du skall göra ett altare af furoträ, fem alnar långt och bredt, så att det varder rätt fyrakant, och tre alnar högt.
“Upange guwa lansembe lamatabwa amtengo wa mkesha. Likhale lofanana mbali zonse, msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi mwake masentimita 229.
2 Horn skall du göra på alla fyra hörnen, och du skall öfverdraga det med koppar.
Upange nyanga imodziimodzi pa ngodya zake zinayizo kuti nyangazo ndi guwalo zikhale chinthu chimodzi, ndipo ulikute guwalo ndi mkuwa.
3 Gör ock askokäril, skoflar, bäcken, gafflar, kolpannor; allt det dertill hörer, skall du göra af koppar.
Upange ziwiya zamkuwa izi zogwirira ntchito pa guwalo: miphika yochotsera phulusa, mafosholo, mabeseni owazira magazi, ngowe zokowera nyama ndi zosonkhezera moto.
4 Du skall ock göra ett galler, såsom ett nät, af koppar, och fyra kopparringar på dess fyra hörn.
Upange sefa yachitsulo chamkuwa ndipo mʼngodya zake zinayizo upangiremo mphete zamkuwa.
5 Du skall ock görat ifrå nedan uppåt kringom altaret, så att gallret räcker midt uppå altaret.
Uyike sefayo mmunsi mwa khoma la guwa lansembelo, ndipo ilekezere pakati pa guwa lansembelo.
6 Och skall du göra stänger till altaret af furoträ, öfverdragna med koppar.
Upange nsichi zamtengo wa mkesha ndipo uzikutire ndi mkuwa.
7 Och skall du stinga stängerna in i ringarna, så att stängerna äro på båda sidor af altaret, der man må bära det med.
Pamene mukunyamula guwalo, muzilowetsa nsichizo mʼmphetemo mbali zonse ziwiri za guwalo.
8 Och skall du så görat af bräder, att det blifver ihålt, såsom dig på berget vist är.
Guwalo likhale lamatabwa ndi logoba mʼkati mwake. Ulipange monga momwe ndinakuonetsera pa phiri paja.
9 Du skall ock göra en gård till tabernaklet; en bonad af hvitt tvinnadt silke, på den ena sidon, hundrade alnar lång söderut;
“Upange bwalo la chihema. Mbali yakummwera ikhale yotalika mamita 46 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino.
10 Och tjugu stolpar på tjugu kopparfötter; och deras knappar med deras gjordar af silfver.
Upangenso mizati makumi awiri, matsinde makumi awiri amkuwa, ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
11 Sammalunda ock norruppå en bonad, hundrade alnar lång; tjugu stolpar på tjugu kopparfötter, och deras knappar med deras gjordar af silfver.
Mbali yakumpoto ikhalenso yotalika mamita 46 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga. Pakhalenso mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
12 Men vesterut öfver gårdsens bredd skall vara en bonad, femtio alnar lång; tio stolpar på tio fötter.
“Mbali yakumadzulo ya bwalolo ikhale yotalika mamita 23 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga, nsichi khumi ndi matsinde khumi.
13 Österut öfver gårdsens bredd skall vara femtio alnar;
Mbali yakummawa, kotulukira dzuwa, kutalika kwa bwalo kukhale mamita 23.
14 Så att bonaden hafver på ene sidone femton alnar; dertill tre stolpar på tre fötter;
Mbali imodzi yachipata kukhale nsalu yotchinga yotalika mamita asanu ndi awiri, mizati itatu ndi matsinde atatu.
15 Och femton alnar på den andra sidone; dertill tre stolpar på tre fötter.
Ndipo ku mbali inayo kukhale nsalu yotchinga ya mamita asanu ndi awiri pamodzi ndi mizati itatu ndi matsinde atatu.
16 Men i gårdsens ingång skall vara ett kläde, tjugu alnar bredt, stickadt med gult silke, skarlakan, rosenrödt och hvitt tvinnadt silke; dertill fyra stolpar på deras fyra fötter.
“Pa chipata cha bwalolo pakhale nsalu yotchinga yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira ndiponso yofewa yosalala. Nsaluyo ikhale yotalika mamita asanu ndi anayi, yopangidwa ndi anthu aluso. Pakhalenso mizati yake inayi ndi matsinde akenso anayi.
17 Alle stolparna kringom gården skola hafva silfvergjordar, och silfverknappar, och kopparfötter.
Mizati yonse yozungulira bwalolo ilumikizidwe ndi zingwe zasiliva. Ngowe zake zikhale zasiliva, koma matsinde ake akhale amkuwa.
18 Och längden på gården skall vara hundrade alnar, bredden femtio, höjden fem alnar, af hvitt tvinnadt silke, och deras fötter skola vara af koppar.
Kutalika kwa bwalolo kukhale mamita 46, mulifupi mwake mamita 23, msinkhu wake masentimita 230. Nsalu ya katani ikhale yofewa ndi yosalala bwino. Matsinde ake akhale amkuwa.
19 Och allt det som tabernaklet tillhörer till allahanda ämbete, och alle dess pålar, och alle gårdsens pålar, skola vara af koppar.
Zipangizo zonse zogwiritsa ntchito zosiyanasiyana pa chihemacho, zikhomo za chihema ndi zabwalolo zikhale zamkuwa.
20 Bjud Israels barnom, att de bära till dig den aldraklaresta oljo, stött af oljoträ, till lysning; att man alltid deraf låter i lamporna;
“Lamula Aisraeli kuti akupatse mafuta anyale a olivi wabwino kwambiri kuti nyalezo ziziyaka nthawi zonse.
21 Uti vittnesbördsens tabernakel utanför förlåten, som hänger för vittnesbördet. Och Aaron med hans söner skola detta sköta, ifrå morgonen allt intill aftonen för Herranom. Det skall vara eder en evig sed intill edra efterkommande, ibland Israels barn.
Mʼchihema cha msonkhano, koma kunja kwa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano, Aaroni ndi ana ake azionetsetsa kuti nyale ikukhala chiyakire pamaso pa Yehova kuyambira madzulo mpaka mmawa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pakati pa Aisraeli pa mibado yonse.”

< 2 Mosebok 27 >