< Predikaren 1 >
1 Detta är Predikarens ord, Davids sons, Konungs i Jerusalem.
Mawu a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya ku Yerusalemu:
2 Allt är fåfängelighet, sade Predikaren; allt är icke annat än fåfängelighet.
“Zopandapake! Zopandapake!” atero Mlaliki. “Zopandapake kotheratu! Zopandapake.”
3 Hvad hafver menniskan mer af alla sine mödo, som hon hafver under solene?
Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zake zonse zimene amasautsidwa nazo pansi pano?
4 En slägt förgås, den andra kommer till; men jorden blifver evinnerliga.
Mibado imabwera ndipo mibado imapita, koma dziko lapansi limakhalapobe nthawi zonse.
5 Solen går upp, och går neder, och löper till sitt rum, att hon der igen uppgå skall.
Dzuwa limatuluka ndipo dzuwa limalowa ndipo limapita mwamsanga kumene limatulukira.
6 Vädret går söder ut, och kommer norr igen, och åter på det rum igen, der det begynte.
Mphepo imawombera cha kummwera ndi kukhotera cha kumpoto; imawomba mozungulirazungulira, kumangobwererabwerera komwe yachokera.
7 Alla floder löpa i hafvet, dock varder icke hafvet dess fullare; till det rum, der de utflyta, dit flyta de igen.
Mitsinje yonse imakathira ku nyanja, koma nyanjayo sidzaza; kumene madziwo amachokera, amabwereranso komweko.
8 All ting är mödosam, så att ingen kan uttalat. Ögat ser sig aldrig mätt, och örat hörer sig aldrig mätt.
Zinthu zonse ndi zotopetsa, kutopetsa kwake ndi kosaneneka. Maso satopa ndi kuona kapena khutu kukwaniritsidwa ndi kumva.
9 Hvad är det, som skedt är? Detsamma, som härefter ske skall. Hvad är det man gjort hafver? Detsamma, som man härefter ännu göra skall; och sker intet nytt under solene.
Zomwe zinalipo kale zidzakhalaponso, zomwe zinachitika kale zidzachitikanso. Ndiye kuti chatsopano palibiretu pansi pano.
10 Sker ock något, der man af sägs kan: Si, det är nytt? Ty det är ock förr skedt i de förra tider, som för oss varit hafva.
Kodi chilipo chinthu chimene wina anganene kuti, “Taona! Ichi ndiye chatsopano?” Chinalipo kale, kalekale; chinalipo ife kulibe.
11 Man kommer intet ihåg, huru det tillförene gånget är, ej heller kommer man ihåg, hvad härefter kommer, när dem som tillkommande äro.
Anthu akale sakumbukiridwa, ngakhale amene adzabwera mʼtsogolomu sadzakumbukiridwa ndi iwo amene adzabwere pambuyo pawo.
12 Jag, Predikare, var Konung öfver Israel i Jerusalem;
Ine, Mlalikine, ndinali mfumu ya Israeli mu Yerusalemu.
13 Och gaf mitt hjerta till att visliga söka och ransaka allt det man gör under himmelen. Sådana usla mödo hafver Gud gifvit menniskors barn, att de sig deruti qvälja skola.
Ndinayika mtima wanga pophunzira ndi kufunafuna mwa nzeru zinthu zonse zimene zimachitika pansi pa thambo. Ndi ntchito yolemetsa ndithu imene Mulungu anayipereka kwa anthu!
14 Jag såg på allt det under solene sker, och si, det var allt fåfängelighet och jämmer.
Ine ndaona zinthu zonse zochitika pansi pano; zinthu zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
15 Krokot kan icke varda rätt; icke heller kunna bristerna varda räknade.
Chinthu chokhota sichingathe kuwongoledwa; chimene palibe sichingathe kuwerengedwa.
16 Jag sade i mitt hjerta: Si, jag är härlig vorden, och hafver mer vishet, än alla de som för mig varit hafva i Jerusalem, och mitt hjerta hafver mycket lärt och försökt.
Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Taona, ine ndakula ndi kukhala wa nzeru zochuluka kupambana aliyense amene analamulirapo Yerusalemu ndisanabadwe; ndaphunzira nzeru zochuluka ndi luntha.”
17 Och gaf också mitt hjerta dertill, att jag måtte lära vishet, och dårskap, och klokhet; men jag förnam, att det är ock möda.
Ndipo ndinadzipereka kuti ndithe kumvetsa kuti nzeru nʼchiyani, misala nʼchiyani, uchitsiru nʼchiyani, koma ndinazindikira ichi, kuti kuteronso nʼkungodzivuta chabe.
18 Ty der mycken vishet är, der är mycken grämelse; och den mycket försöker, han måste mycket lida.
Pakuti nzeru zochuluka zimabweretsa chisoni chochulukanso: chidziwitso chochuluka, zowawa zochulukanso.