< Predikaren 8 >

1 Ho är som en vis? Och ho kan det uttyda? Menniskones vishet upplyser hennes ansigte; men den der oförvägen är, honom hatar man.
Ndani angafanane ndi munthu wanzeru? Ndani angadziwe kutanthauzira zinthu? Nzeru imabweretsa chimwemwe pa nkhope ya munthu ndipo imasintha maonekedwe ake awukali.
2 Jag håller Konungens ord, och Guds ed.
Ine ndikuti, mvera lamulo la mfumu, chifukwa unalumbira pamaso pa Mulungu.
3 Var icke för hastig till att gå ifrå hans ansigte, och blif icke i en ond sak; ty han gör hvad honom lyster.
Usafulumire kuchoka pamaso pa mfumu. Usawumirire chinthu choyipa, pakuti mfumu idzachita chilichonse chomwe imasangalatsidwa nacho.
4 I Konungens ord är magt, och ho kan säga till honom: Hvad gör du?
Popeza mawu a mfumu ali ndi mphamvu, ndani anganene kwa mfumuyo kuti, “Kodi mukuchita chiyani?”
5 Den der budet håller, han skall intet ondt försöka; men ens vis mans hjerta vet tid och sätt.
Aliyense amene amamvera lamulo lake sadzapeza vuto lililonse, ndipo munthu wanzeru amadziwa nthawi yoyenera ndi machitidwe ake.
6 Ty hvart och ett anslag hafver sin tid och sätt; ty menniskones olycka är mycken med henne.
Pakuti pali nthawi yoyenera ndiponso machitidwe a chinthu chilichonse, ngakhale kuti mavuto ake a munthu amupsinja kwambiri.
7 Ty hon vet icke hvad varit hafver; och ho kan säga henne, hvad varda skall?
Popeza palibe munthu amene amadziwa zamʼtsogolo, ndani angamuwuze zomwe zidzachitika mʼtsogolo?
8 En menniska hafver icke magt öfver andan, till att förmena andan; och hafver icke magt i dödsens tid, och varder icke lös gifven i stridene; och ett ogudaktigt väsende hjelper den ogudaktiga intet.
Palibe munthu amene ali ndi mphamvu yolamulira mpweya wa moyo kuti athe kuwusunga, choncho palibe amene ali ndi mphamvu pa tsiku la imfa yake. Nkhondo sithawika; tsono anthu ochita zoyipa, kuyipa kwawoko sikudzawapulumutsa.
9 Allt det hafver jag sett, och gaf mitt hjerta till all verk, som ske under solene; en menniska råder understundom öfver den andra, sig till skada.
Zonsezi ndinaziona pamene ndinalingalira mu mtima mwanga, zonse zimene zimachitika pansi pano. Ilipo nthawi imene ena amalamulira anzawo mwankhanza.
10 Och der såg jag ogudaktiga, som begrafne voro; som gångit och vandrat hade i heligt rum, och voro förgätne i staden, att de så gjort hade; det är ock fåfängelighet.
Kenaka, ndinaona anthu oyipa akuyikidwa mʼmanda, iwo amene ankalowa ndi kumatuluka mʼmalo opatulika ndipo ankatamandidwa mu mzindawo pamene ankachita zimenezi. Izinso ndi zopandapake.
11 Efter det icke straxt går domen öfver onda gerningar, varder menniskones hjerta fullt till att göra ondt.
Pamene chigamulo cha anthu opalamula mlandu chikuchedwa, mitima ya anthu imadzaza ndi malingaliro ochita zolakwa.
12 Om en syndare hundrade resor illa gör, och dock länge lefver, så vet jag likväl, att dem varder väl gångande, som Gud frukta, de som hans ansigte frukta.
Ngakhale munthu woyipa apalamule milandu yambirimbiri, nʼkumakhalabe ndi moyo wautali, ine ndikudziwa kuti anthu owopa Mulungu zinthu zidzawayendera bwino, omwe amapereka ulemu pamaso pa Mulungu.
13 Ty dem ogudaktiga varder icke väl gångandes, och såsom en skugge skola de icke länge lefva, som icke Gud frukta.
Koma popeza oyipa saopa Mulungu zinthu sizidzawayendera bwino, ndipo moyo wawo sudzakhalitsa monga mthunzi.
14 Det är en fåfängelighet, som sker uppå jordene. Någre äro rättfärdige, och dem går, såsom de hade de ogudaktigas gerningar gjort; och någre äro ogudaktige, och dem går, såsom de hade de rättfärdigas gerningar gjort. Jag sade: Det är ock fåfängelighet.
Palinso chinthu china chopanda phindu chomwe chimachitika pa dziko lapansi: anthu olungama amalangidwa ngati anthu osalungama. Pamene oyipa amalandira zabwino ngati kuti ndi anthu abwino.
15 Derföre prisade jag glädjena, att menniskan intet bättre hafver under solene, än äta och dricka, och vara glad; och sådant får hon af sitt arbete i sine lifsdagar, som Gud henne gifver under solene.
Nʼchifukwa chake ndikuti munthu azikondwerera moyo, pakuti munthu alibe chinanso chabwino pansi pano choposa kudya, kumwa ndi kumadzikondweretsa. Akamatero, munthuyo adzakhala ndi chimwemwe pa ntchito yake masiku onse a moyo wake amene Mulungu wamupatsa pansi pano.
16 Jag gaf mitt hjerta till att veta vishet, och till att skåda den vedermödo, som på jordene sker; att ock en hvarken dag eller natt får sömn i sin ögon.
Pamene ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe nzeru ndi kuonetsetsa ntchito za munthu pa dziko lapansi, osapeza tulo usana ndi usiku,
17 Och jag såg all Guds verk; ty en menniska kan icke finna det verk, som under solene sker; och ju mer menniskan arbetar till att söka, ju mindre finner hon. Om hon än säger: Jag är vis, och vet det, så kan hon dock icke finnat.
pamenepo ndinaona zonse zimene Mulungu anazichita. Palibe munthu amene angathe kuzimvetsa zonse zimene zimachitika pansi pano. Ngakhale munthu ayesetse kuzifufuza, sangathe kupeza tanthauzo lake. Ngakhale munthu wanzeru atanena kuti iye amadziwa, sangathe kuzimvetsetsa zinthuzo.

< Predikaren 8 >