< 5 Mosebok 4 >

1 Och nu hör, Israel, de bud och rätter, som jag eder lärer, att I dem göra skolen, på det I män lefva, och inkomma, och intaga landet, som Herren edra fäders Gud eder gifver.
Mverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuphunzitseni. Muwatsatire kuti mukhale ndi moyo ndi kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu akukupatsani.
2 I skolen intet lägga dertill, som jag eder bjuder; och skolen ej heller taga der något ifrå; på det I mågen bevara Herrans edars Guds bud, som jag bjuder eder.
Musawonjezere pa zimene ndikukulamulirani ndipo musachotserepo, koma muwasunge malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani.
3 Edor ögon hafva sett hvad Herren gjort hafver med BaalPeor; ty alla de som efterföljde BaalPeor, dem hafver Herren din Gud förgjort ibland eder.
Inu munaona ndi maso anu zimene Yehova anachita ku Baala-Peori. Yehova Mulungu wanu anawononga aliyense amene anatsata Baala wa ku Peori pakati panu.
4 Men I som höllen eder intill Herran edar Gud, I lefven alle på denna dag.
Koma inu nonse amene munagwiritsitsa Yehova Mulungu wanu mukanali ndi moyo mpaka lero.
5 Si, jag hafver lärt eder bud och rätter, såsom Herren min Gud mig budit hafver, att I så göra skolen i landet, der I inkommande varden till att intaga det.
Taonani, ndakuphunzitsani malangizo ndi malamulo monga Yehova Mulungu wanga anandilamulira kuti inuyo muwatsatire mʼdziko limene mukulowa ndi kulitengali.
6 Så behåller det nu, och görer det; ty så varder edor vishet och förstånd berömd för all folk, när de hörande varda all denna bud, så att de skola säga: Si, hvilket vist och förståndigt folk detta är, och ett härligit folk.
Muwasunge mosamalitsa pakuti zimenezi zidzaonetsa nzeru zanu ndi kuzindikira kwanu kwa anthu a mitundu ina, amene adzamva za malangizo onsewa nati, “Ndithudi, mtundu waukulu uwu ndi wa anthu anzeru ndi ozindikira.”
7 Ty hvad folk är så härligit, hvilko gudarna så nalkas, såsom Herren vår Gud, så ofta som vi åkalle honom?
Mtundu wina wa anthu ndi uti umene uli waukulu chomwechi, woti ukhoza kukhala ndi milungu yawo pafupi monga mmene alili Yehova Mulungu wathu ndi ife nthawi zonse pamene tipemphera kwa Iye?
8 Och hvar är något så härligit folk, som så rättfärdiga seder och bud hafver, såsom all denna lagen, som jag eder på denna dagen föregifver?
Ndipo ndi mtundu uti mwa mitundu ya anthu umene ndi waukulu chotere kuti nʼkukhala ndi malangizo ndi malamulo olungama ngati malamulo amene ndikuyika pamaso panu lero?
9 Så förvara dig nu och dina själ granneliga, att du icke förgäter hvad för din ögon skedt är, och att det icke gånger utu dino hjerta i alla dina lifsdagar; och skall förkunna dinom barnom, och dinom barnabarnom,
Inu mungosamala ndi kudziyangʼanira kwambiri nokha kuti musayiwale zimene maso anu aona. Musalole kuti zichoke mʼmitima mwanu pa moyo wanu wonse. Zimenezi muziphunzitse kwa ana anu ndi zidzukulu zanu ngakhale mʼtsogolo.
10 Den dagen, då du stod för Herranom dinom Gud vid berget Horeb, och Herren till mig sade: Församla mig folket, att jag skall låta dem höra min ord, och lära frukta mig i alla deras lifsdagar på jordene, och lära sin barn.
Kumbukirani tsiku limene munayimirira pamaso pa Yehova Mulungu wanu ku Horebu, pamene anati kwa ine, “Sonkhanitsa anthu pamaso panga kuti amve mawu anga ndi kuti aphunzire kundilemekeza mʼmoyo wawo onse mʼdzikomo ndi kuti ana awo aziwaphunzitsa zimenezi.”
11 Och I gingen fram, och stoden neder under berget, och berget brann halfväges upp till himmelen; och der var mörker, moln och töckna.
Munabwera pafupi ndi kuyima pa tsinde pa phiri pamene phirilo limayaka moto umene umafika mpaka kumwamba. Panalinso mtambo wakuda ndi mdima wambiri.
12 Och Herren talade med eder midt utur elden; hans ords röst hörden I, men ingen liknelse sågen I, utan röstena.
Kenaka Yehova anayankhula nanu kuchokera mʼmotowo. Inu munamva mawu ake okha koma simunamuone pakuti panali mawu chabe.
13 Och han förkunnade eder sitt förbund, det han eder böd att göra; nämliga de tio ord, och skref dem på två stentaflor.
Iye anakuwuzani Malamulo Khumi omwe ndi pangano lake limene anakulamulirani kuti mutsatire. Ndipo anawalemba malamulowo pa mapale awiri a miyala.
14 Och Herren böd mig på samma tiden, att jag skulle lära eder bud och rätter, att I derefter göra skullen uti de lande, der I indragen till att intaga det.
Ndipo Yehova anandilamula nthawi imene ija kuti ndikuphunzitseni malangizo ndi malamulo amene muyenera kutsata mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani.
15 Så förvarer nu edra själar väl; ty I hafven ingen liknelse sett på den dagen, då Herren talade med eder utur elden på bergena Horeb;
Tsiku limene Yehova anayankhula nanu ku Horebu mʼmoto uja, simunaone thupi lake. Choncho mudziyangʼanire nokha mosamalitsa,
16 På det I icke skolen förderfva eder och göra eder något beläte, det en man likt är eller qvinno;
kuti musasokonezeke ndi kudzipangira nokha fano kapena chifanizo cha mtundu uliwonse, kaya chokhala ngati mwamuna kapena ngati mkazi,
17 Eller djure på jordene, eller fogle under himmelen;
kaya chokhala ngati nyama iliyonse ya pa dziko lapansi kapena mbalame iliyonse yowuluka mlengalenga.
18 Eller matke, som kräker på jordene, eller fiske i vattnena under jordene;
Kapena cholengedwa chilichonse choyenda pa nthaka kapena nsomba ya mʼmadzi akuya.
19 Och att du icke heller upphäfver din ögon till himmelen, och ser solen, och månan, och stjernorna, hela himmelens här, och faller af, och tillbeder dem, och tjenar dem, hvilka Herren din Gud förskickat hafver allom folkom under hela himmelen.
Ndipo pamene muyangʼana kumwamba muona dzuwa, mwezi ndi nyenyezi, zonse zakumwambazo musakopeke kuti muzigwadire ndi kumapembedza zinthu zimene Yehova wapereka kwa anthu a mitundu yonse pa dziko lapansi.
20 Men eder hafver Herren upptagit, och fört eder utu jernugnen, nämliga utur Egypten, att I skullen vara hans arffolk, som det ock är i denna dag.
Koma inuyo, Yehova anakutengani ndi kukutulutsani mʼngʼanjo yosungunulira zitsulo, ku Igupto kuti mukhale anthu olandira chuma chake monga mmene mulili tsopano.
21 Och Herren vardt vred på mig för edra gerningars skull, så att han svor, att jag icke skulle komma öfver Jordanen, eller i det goda landet, som Herren din Gud dig till arfvedel gifva skall;
Yehova anakwiya nane chifukwa cha inu, ndipo analumbira kwathunthu kuti sindidzawoloka Yorodani ndi kulowa mʼdziko labwinolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani inu ngati cholowa chanu.
22 Utan jag måste dö i detta land, och skall icke gå öfver Jordanen; men I skolen gå deröfver, och intaga det goda landet.
Ine ndifera mʼdziko lino, sindiwoloka Yorodani. Koma inu mwatsala pangʼono kuwoloka ndi kukatenga dziko labwinolo.
23 Så tager eder nu vara, att I Herrans edars Guds förbund icke förgäten, det han med eder gjort hafver; och icke görer beläte till någrahanda liknelse, såsom Herren din Gud dig budit hafver.
Samalani, musayiwale pangano limene Yehova Mulungu wanu anapangana nanu ndipo musadzipangire nokha fano la chinthu chilichonse chimene Yehova Mulungu wanu waletsa.
24 Förty Herren din Gud är en frätande eld, och en nitälskande Gud.
Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi moto wonyeketsa ndipo ndi Mulungu wansanje.
25 När I nu föden barn, och barnabarn, och bon på landena, och förderfven eder, och gören eder beläte till någrahanda liknelse, så att I gören illa för Herranom edrom Gud, och förtörnen honom;
Mukadzakhala nthawi yayitali mʼdzikomo ndi kubereka ana ndi kukhala ndi zidzukulu ndipo mukadzasokonekera ndi kupanga fano la mtundu uliwonse, nʼkumachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kumukwiyitsa,
26 Så kallar jag i denna dag himmel och jord till vittne öfver eder, att I skolen snart förgås utaf landena, uti hvilket I ingån öfver Jordanen, till att intaga det. I skolen icke länge blifva deruti; utan skolen förgjorde varda;
ine ndi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni lero zokutsutsani kuti mudzawonongedwa msanga ndipo mudzachotsedwa mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani. Simudzakhalitsa kumeneko koma mudzawonongedwa ndithu.
27 Och Herren skall förströ eder ibland folk, och I varden ett fögo folk qvart blifvande ibland Hedningarna, dit Herren eder drifvandes varder.
Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu ena. Ochepa okha pakati panu ndi amene adzapulumuke pakati pa anthu a mitundu ina kumene Yehova adzakupirikitsireniko.
28 Der skall du tjena afgudom, som menniskohandaverk äro, stock och sten, hvilke hvarken se eller höra, eller äta, eller lukta.
Kumeneko mudzapembedza milungu ya mitengo ndi miyala yopangidwa ndi anthu, imene singaone kapena kumva kapena kudya kapena kununkhiza.
29 Om du då der söker Herran din Gud, så skall du finna honom; om du söker honom af allo hjerta, och af allo själ.
Mukanali komweko, ngati mudzamufunafuna Yehova Mulungu wanu mudzamupeza koma ngati mutamufunafuna ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
30 När du bedröfvad varder, och dig all denna tingen uppåkomma i de yttersta dagar, så skall du vända dig till Herran din Gud, och skall höra hans röst;
Mukadzakhala pa chipsinjo ndipo zonsezi zikadzakuchitikirani, ndi pamene pambuyo pake mudzabwerera kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera Iye.
31 Förty Herren din Gud är en barmhertig Gud; han varder dig icke öfvergifvandes, eller förderfvandes; och skall han icke förgäta det förbund med dina fäder, som han dem svorit hafver.
Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wachifundo, Iye sadzakutayani kapena kukuwonongani kapena kuyiwala pangano lake ndi makolo anu, limene analitsimikiza mwa lumbiro.
32 Befråga efter förtiden, som för dig varit hafver, ifrå den dagen då Gud skop menniskona på jordene, ifrå den ena himmelens ända till den andra, om någon tid en sådana stor ting skedd, eller dess like någon tid hörd är;
Tsopano tafunsani za masiku a mʼmbuyomu, zakale inu musanabadwe, kuyambira tsiku limene Mulungu analenga munthu pa dziko lapansi. Tafufuzani kuyambira kumapeto mpaka mapeto anzake a thambo. Kodi chinachitikako china chachikulu ngati ichi, kapena chinayamba chamvekako chokhala ngati ichi?
33 Att något folk hade hört Guds röst talandes utur elden, såsom du hört hafver, och likväl lefver?
Kodi uliponso mtundu wina wa anthu umene unamva mawu a Mulungu akuyankhula kuchokera mʼmoto nʼkukhala ndi moyo monga mwachitira inumu?
34 Eller om Gud försökt hafver att ingå, och taga sig ett folk midt utur eno folke, genom frestelse, genom tecken, genom under, genom strid, och genom mägtiga hand, och genom uträcktan arm, och genom stora syner, såsom Herren edar Gud allt detta med eder gjort hafver, för din ögon uti Egypten?
Kodi alipo mulungu amene anayeserapo kudzitengera mtundu wa anthu kuwachotsa mu mtundu unzake mwa mayesero, zizindikiro zozizwitsa, nkhondo, komanso mwa mphamvu zake zopanda malire, kapena mwa zochita zazikulu ndi zochititsa mantha, monga zimene Yehova Mulungu wanu anakuchitirani ku Igupto inu mukupenya?
35 Du hafver sett det, på det du skall veta, att Herren är allena Gud, och ingen annan.
Iye anakuonetsani zonsezi kuti inu muzindikire kuti Yehova ndiye Mulungu, palibenso wina wofanana naye.
36 Af himmelen hafver han låtit dig höra sina röst, att han skulle lära dig; och på jordene hafver han låtit dig se sin stora eld, och utur elden hafver du hört hans ord;
Kuchokera kumwamba, Iye anafuna kuti inu mumve mawu ake ndi kuti mukhale osunga mwambo. Pa dziko lapansi anakuonetsani moto waukulu, ndipo inu munamva mawu ake kuchokera mʼmotomo.
37 Derföre, att han dina fäder älskat, och deras säd efter dem utvalt hafver; och fört dig utur Egypten med sitt ansigte, genom sina stora magt;
Popeza anakonda makolo anu ndi kusankha adzukulu awo, a pambuyo pawo, anakutulutsani kuchoka ku Igupto ali pakati panu ndi mphamvu yake,
38 På det han skulle för dig fördrifva stor folk, och starkare än du äst, och föra dig derin, och gifva dig deras land till arfvedel, såsom det tillstår i denna dag.
kuti akupirikitsireni mayiko akuluakulu ndi amphamvu kuposa inu, ndi kukubweretsani inu ku dziko lawo kuti likhale lanu, monga liliri lero.
39 Så skall du nu veta i dag, och lägga det på hjertat, att Herren är en Gud, ofvan i himmelen, och nedre uppå jordene, och ingen annan;
Vomerezani lero ndipo dziwani mu mtima mwanu kuti Yehova ndiye Mulungu kumwamba ndi pa dziko lapansi. Palibenso wina.
40 Att du håller hans rätter och bud, som jag i dag bjuder dig, så varder dig och dinom barnom efter dig väl gåendes, att ditt lif skall länge vara i landena, som Herren din Gud dig gifver evärdeliga.
Sungani malangizo ake ndi malamulo ake amene ndikukupatsani lero lino, kuti zikuyendereni bwino inu ndi ana anu kutsogoloko, ndi kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kwa nthawi zonse.
41 Då afskiljde Mose tre städer hinsidon Jordan, österut;
Kenaka Mose anapatula mizinda itatu cha kummawa kwa Yorodani,
42 Att dit fly skulle ho som sin nästa ihjälsloge med våda, och tillförene icke hade varit hans ovän; den skulle fly in uti en af de städer, på det han måtte blifva vid lif;
kumene aliyense amene wapha munthu akhoza kuthawirako ngati wopha munthuyo sanaphe mnzakeyo mwadala ndi maganizo oyipa. Iye akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi napulumutsa moyo wake.
43 Bezer i öknene på den slättmarkene ibland de Rubeniter, och Ramoth i Gilead ibland de Gaditer, och Golan i Basan ibland de Manassiter.
Mizindayo inali iyi: ku fuko la Rubeni, unali mzinda wa Bezeri ku mapiri a ku chipululu; ku fuko la Gadi, unali Ramoti ku Giliyadi; ndipo ku fuko la Manase, unali Golani ku Basani.
44 Detta är den lag, som Mose Israels barnom föregaf;
Awa ndi malamulo amene Mose anapereka kwa Aisraeli.
45 Och detta är vittnesbördet, och bud, och rätter, som Mose sade Israels barnom, då de utur Egypten dragne voro;
Izi ndi ndondomeko, malangizo ndi malamulo amene Mose anawapatsa iwo pamene anatuluka ku Igupto.
46 Hinsidon Jordan uti den dalenom in mot Peors hus, uti Sihons lande, de Amoreers Konungs, som i Hesbon bodde, hvilken Mose och Israels barn slogo, då de utur Egypten komne voro,
Anali ku chigwa cha kufupi ndi Beti-Peori mbali ya kummawa kwa Yorodani, mʼdziko la Sihoni mfumu ya Aamori amene ankalamulira ku Hesiboni ndipo anagonjetsedwa ndi Mose ndi Aisraeli pamene ankachokera ku Igupto.
47 Och togo hans land in; dertill Ogs land, Konungens i Basan, de två Amoreers Konungars, som på hinsidon Jordan voro, österut;
Iye anamulanda dziko lake ndi dziko la Ogi mfumu ya ku Basani. Awa anali mafumu awiri Aamori a kummawa kwa Yorodani.
48 Ifrån Aroer, hvilken på den bäckens strand vid Arnon ligger, intill berget Sion, det är Hermon;
Dziko ili linayambira ku Aroeri cha kumphepete kwa khwawa la Arinoni ku phiri la Siyoni (limeneli ndi phiri la Herimoni),
49 Och allt släta landet hinsidon Jordan, österut, allt intill hafvet, på slättene, nedanför berget Pisga.
ndi kuphatikizapo dziko lonse la Araba cha kummawa kwa Yorodani mpaka kukafika ku Nyanja ya Araba, kumunsi kwa Phiri la Pisiga.

< 5 Mosebok 4 >