< 5 Mosebok 11 >

1 Så skall du nu älska Herran din Gud, och hålla hans lag, hans seder, hans rätter och hans bud, så länge du lefver.
Muzikonda Yehova Mulungu wanu ndipo nthawi zonse muzitsata zimene Iyeyo anakulamulani, malangizo, zikhazikitso ndi malamulo ake.
2 Och förnimmer i dag det edor barn icke veta, eller sett hafva; nämliga Herrans edars Guds tuktan, hans härlighet, och hans mägtiga hand, och uträckta arm;
Lero kumbukirani kuti si ana anu amene anaona ndi kulawa chilango cha Yehova Mulungu wanu: ukulu wake, dzanja lake lamphamvu, mkono wake wotambasuka;
3 Och hans tecken och verk, som han gjorde ibland de Egyptier, på Pharao, Konungen i Egypten, och på allt hans land;
zizindikiro zozizwitsa zimene anazionetsa ndi zinthu zimene anazichita mʼkati mwa Igupto, Farao mfumu ya Igupto ndi kwa dziko lake lonse;
4 Och hvad han gjorde på de Egyptiers magt; på deras hästar och vagnar, då han lät komma vattnet af det röda hafvet öfver dem, när de foro efter eder, och Herren förgjorde dem, allt intill denna dag;
zimene Iye anachita kwa gulu lankhondo la Aigupto, kwa akavalo ndi magaleta awo, mmene Iye anawamizira ndi madzi a mu Nyanja Yofiira pamene amakuthamangitsani, ndi mmene Yehova anawagonjetsera kufikira lero.
5 Och hvad han eder gjorde i öknene, intilldess I nu till detta rummet komne ären;
Si ana anu amene anaona zimene Iye anakuchitirani mʼchipululu kufikira pamene munafika pa malo anu,
6 Hvad han gjorde Dathan och Abiram, Eliabs sönom, Rubens sons; huru jorden öppnade sin mun, och uppsvalg dem med deras folk och tjäll, och alla deras ägodelar, som under dem voro, midt i hela Israel.
ndi zimene anachitira Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu mwana wa Rubeni, pamene nthaka inatsekula pakamwa pake pakati pa Aisraeli onse ndi kuwameza pamodzi ndi katundu wawo, matenti awo ndi chilichonse chawo.
7 Ty edor ögon hafva sett de stora Herrans gerningar, som han gjort hafver.
Koma ndinuyo amene munaona ntchito zonse zikuluzikulu zimenezi Yehova anakuchitirani.
8 Derföre skolen I hålla all de bud, som jag bjuder eder i dag, på det I skolen styrkte varda till att komma in, och intaga landet, dit I faren till att intaga det;
Tsono muzisunga malamulo onse amene ndikukupatsani lero kuti mukhale ndi mphamvu ndi kuti mupite kukalanda mʼdziko limene mwakhala pangʼono kulowamo mukawoloka Yorodani,
9 Och att du skall länge lefva i landena, som Herren edra fäder svorit hafver att gifva dem och deras säd, ett land der mjölk och hannog uti flyter.
ndiponso kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu ndi zidzukulu zawo, lomwe ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi.
10 Ty det landet, som du kommer till att intaga, är icke såsom Egypti land, der I utdragne ären, der man sår säd, och bär dit vatten till fots, såsom till en kålgård;
Dziko limene mukukalanda ndi kulowamo silokhala ngati dziko la ku Igupto kumene mukuchokera ayi, kuja mumadzala mbewu ndi kumathirira ndi mapazi anu ngati ku dimba.
11 Utan det hafver berg, och slättmarker, hvilka regn af himmelen vattna måste;
Koma dziko limene mukalande mukawoloka Yorodani ndi dziko la mapiri ndi zigwa, dziko limene limalandira mvula kuchokera kumwamba.
12 Om hvilket land Herren din Gud låter sig vårda, och Herrans dins Guds ögon se alltid deruppå, ifrå begynnelsen på året, intill ändan.
Ili ndi dziko limene Yehova Mulungu wanu amalisamalira. Maso a Yehova Mulungu wanu amaliyangʼanira nthawi zonse kuchokera ku mayambiriro a chaka mpaka kumapeto kwake.
13 Om I nu hören min bud, som jag bjuder eder i dag, att I älsken Herran edar Gud, och tjenen honom af allt hjerta, och af allo själ;
Choncho mukasunga mokhulupirika malamulo amene ndikukupatsani lero lino, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iyeyo ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse,
14 Så skall jag gifva edro lande regn i sinom tid, arla och serla, att du skall inberga din säd, ditt vin, och dina oljo;
pamenepo ndidzatumiza mvula mʼdziko mwanu pa nthawi yake mʼnyengo ya dzinja ndi chilimwe, kuti mudzakolole tirigu wambiri ndi kuti mudzakhale ndi vinyo watsopano ndi mafuta.
15 Och skall gifva dinom boskap gräs på dine mark, att I mågen äta och varda mätte.
Ndidzakupatsani udzu mʼminda mwanu woti muzidzadyetsera ngʼombe zanu ndipo inuyo mudzadya ndi kukhuta.
16 Men tager eder vara, att edart hjerta icke låter draga sig dertill, att I afträden, och tjenen andra gudar, och tillbedjen dem;
Dzisamalireni nokha, kuopa kuti mungakopeke mtima ndi kubwerera mʼmbuyo kuyamba kutumikira milungu ina ndi kumayigwadira.
17 Och Herrans vrede förgrymmar sig då öfver eder, och lycker himmelen till, att intet regn kommer, och jorden icke gifver sin växt, och I snarliga förgås utaf det goda landet, som Herren eder gifvit hafver.
Mukatero Yehova Mulungu wanu adzakukwiyirani kwambiri, nadzaletsa thambo kuti lisabweretsenso mvula ndipo dziko silidzapereka zokolola. Choncho mudzawonongeka msanga mʼdziko limene Yehova akukupatsani.
18 Så fatter nu dessa orden i hjertat, och i edra själar, och binder dem för ett tecken på edra hand, att de äro till en åminnelse för edor ögon;
Sungani mawu amenewa mu mtima mwanu ndi mʼmaganizo mwanu, muwamangirire pa mikono yanu ndipo muwayike pamphumi panu.
19 Och lärer dem edor barn, så att du talar derom, när du sitter i dino huse, eller går på vägen; när du lägger dig neder, och när du uppstår.
Mawuwa muziphunzitsa ana anu, muzikamba za iwo pamene mukhala pansi mʼnyumba zanu, pamene mukuyenda mʼnjira, pamene mugona ndi pamene mukudzuka.
20 Och skrif dem på dörrträn i dino huse, och på dine dörr;
Muwalembe pa mphuthu za nyumba zanu ndi pa zipata zanu,
21 Att du och din barn mågen länge lefva i landena, som Herren dine fäder svorit hafver att gifva dem, så länge dagarna af himmelen på jordene vara.
kuti inu ndi ana anu mukhale mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu mpaka kalekale monga umakhalira mlengalenga pamwamba pa dziko.
22 Ty om I alla dessa buden hållen, som jag bjuder eder, och derefter gören, så att I älsken Herran edar Gud, och vandren i alla hans vägar, och håller eder intill honom;
Mukatsatira mosamalitsa malamulo amene ndikukupatsaniwa, kukonda Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira zake zonse ndi kumugwiritsitsa Iye
23 Så skall Herren fördrifva allt detta folket för eder, så att I skolen intaga större och starkare folk än I ären.
Yehova adzapirikitsa mitundu ina yonseyi inu musanafike ndipo mudzagonjetsa mitundu ikuluikulu ndi yamphamvu kuposa inu.
24 All rum, som edar fot på träder, skola vara edor; ifrån öknene och ifrå berget Libanon, och ifrån älfvene Phrath, allt intill det yttersta hafvet, skall edart landamäre vara.
Malo aliwonse amene mudzaponda adzakhala anu: dziko lanu lidzachokera ku chipululu mpaka ku Lebanoni, ndi ku Mtsinje wa Yufurate mpaka ku nyanja ya kumadzulo.
25 Ingen skall kunna stå eder emot; edar räddhåga och förfärelse skall Herren låta komma öfver all de land, der I inresen, såsom han eder sagt hafver.
Palibe munthu amene adzalimbana nanu. Monga analonjezera, Yehova adzachititsa kuti anthu onse mʼdziko limene mukupitalo adzachite nanu mantha ndi kukuopani.
26 Si, jag lägger eder före i dag välsignelse och förbannelse:
Taonani, lero ndikuyika dalitso ndi temberero pakati panu,
27 Välsignelse, om I lyden Herrans edars Guds bud, som jag bjuder eder i dag;
dalitso ngati mumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero.
28 Förbannelse, om I icke lyden Herrans edars Guds bud, och afträden ifrå den vägen, som jag bjuder eder i dag, så att I vandren efter andra gudar, de I icke kännen.
Temberero ngati simumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu ndi kupatuka pa njira imene ndikulamulirani lero potsata milungu ina imene simunayidziwe.
29 När Herren din Gud förer dig in i det land, der du inkommer till att intagat, så skall du låta tala välsignelsen på det berget Grisim, och förbannelsen på det berget Ebal;
Yehova Mulungu wanu akakakufikitsani mʼdziko mukukalandalo kuti mulowemo mukanene za madalitso pa Phiri la Gerizimu, ndi za matemberero pa Phiri la Ebala.
30 Hvilke äro på hinsidon Jordan, på den vägen vesterut, i de Cananeers lande, som bo på den slättmarkene in emot Gilgal, vid den lunden More.
Monga mudziwa, mapiriwa ali kutsidya kwa Yorodani, kumadzulo kolowera dzuwa, kufupi ndi mitengo ya thundu ya More, mʼdziko la Akanaani aja okhala ku Araba moyangʼanana ndi Giligala.
31 Ty du måste gå öfver Jordan, att du inkommer, och tager landet in, som Herren edar Gud eder gifvit hafver, att I det intaga och deruti bo skolen.
Mwatsala pangʼono kuwoloka Yorodani kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. Mukadzalitenga dzikolo ndi kukhalamo,
32 Så ser nu till, att I gören efter all de bud och rätter, som jag eder i dag förelägger.
mudzaonetsetse kuti mukumvera malangizo ndi malamulo amene ndikukuwuzani lero.

< 5 Mosebok 11 >