< Amos 6 >
1 Ve dem stoltom i Zion, och dem som förlåta sig uppå Samarie berg, hvilke sig hålla får de aldrabästa i hela verldene; och regera i Israels hus, såsom dem täckes.
Tsoka kwa amene simukulabadira kanthu ku Ziyoni, ndiponso kwa inu amene mukukhala mwamtendere pa Phiri la Samariya, inu anthu otchuka ochokera ku mtundu wa anthu omveka, kumene Aisraeli amafikako!
2 Går bort till Calne, och skåder; och dädan bort till Hamath, den stora staden; och drager dädan neder till Gath de Philisteers, hvilka bättre Konungarike varit hafva än dessa, och deras gränsa större än edor gränsa;
Pitani ku mzinda wa Kaline mukawuyangʼane; mukapitenso ku Hamati-raba mzinda waukulu uja, ndipo mukatsikirenso ku Gati kwa Afilisti. Kodi mizinda imeneyi ndi yopambana maufumu anu awiriwa? Kodi dziko lawo ndi lalikulu kupambana lanu?
3 Likväl vordo de förjagade, då deras onda stund kom; och I regeren med öfvervåld;
Inu simulabadirako kuti tsiku loyipa lidzafika, zochita zanu zimafulumizitsa ulamuliro wankhanza.
4 Och liggen i elphenbenssängar, och prålen på edor tapeter; och äten det bästa, af hjordenom, och de gödda kalfvar;
Mumagona pa mabedi owakongoletsa ndi minyanga ya njovu, mumagona pa mipando yanu ya wofuwofu. Mumadya ana ankhosa onona ndi ana angʼombe onenepa.
5 Och spelen på psaltare, och dikten eder visor, såsom David;
Mumayimba azeze anu ndi kumangopeka nyimbo pa zingʼwenyengʼwenye ngati Davide.
6 Och dricken vin utu skålar, och smörj en eder med balsam; och bekymrer eder intet om Josephs skada.
Mumamwera vinyo mʼzipanda zodzaza ndipo mumadzola mafuta abwino kwambiri, koma simumva chisoni ndi kuwonongeka kwa Yosefe.
7 Derföre skola de nu gå främst ibland dem som fångne bortförde varda; och de prålares slösande skall återvända.
Nʼchifukwa chake inu mudzakhala mʼgulu la anthu oyamba kupita ku ukapolo; maphwando ndi zikondwerero zanu zidzatheratu.
8 Ty Herren Herren hafver svorit vid sina själ, säger Herren Gud Zebaoth: Mig förtryter Jacobs högfärd, och är deras palatsom gramse; och jag skall desslikes öfvergifva staden, med allt det deruti är.
Ambuye Yehova walumbira mʼdzina lake. Yehova Mulungu Wamphamvuzonse walengeza kuti, “Ndimanyansidwa ndi kunyada kwa Yakobo, ndimadana ndi nyumba zake zaufumu; Ine ndidzawupereka mzindawu pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.”
9 Och om än tio män qvare blefvo uti ett hus, skola de likväl dö;
Ngati anthu khumi otsala adzabisala mʼnyumba imodzi, nawonso adzafa ndithu.
10 Så att hvars och ens faderbroder och moderbroder tager honom, och måste draga hans ben utu huset, och säga till den som i husens kammar är: Äro der ock flere? Och han skall svara: De äro alle sin kos: och skall säga: Var tillfrids; ty de ville icke, att man på Herrans Namn tänka skulle.
Ndipo ngati mʼbale wake wa wina wakufayo, woyenera kusamala za maliro, adzafika kudzatulutsa mitembo mʼnyumbamo nʼkufunsa aliyense amene akubisalabe mʼnyumbamo kuti, “Kodi uli ndi wina wamoyo mʼmenemo?” Ndipo munthu wobisalayo ndi kuyankha kuti, “Ayi,” mʼbaleyo adzanena kuti, “Khala chete! Ife tisayerekeze kutchula dzina la Yehova.”
11 Ty si, Herren hafver budit, att man skall slå de stora husen, att de skola få refvor, och de små husen, att de få hål.
Pakuti Yehova walamula kuti nyumba zikuluzikulu Iye adzazigamulagamula, ndipo nyumba zazingʼono zidzasanduka maduka okhaokha.
12 Ho kan ränna med hästom, eller plöja med oxom på hälleberget? Ty I vänden rätten uti galla, och rättvisones frukt uti malört;
Kodi akavalo amathamanga pa thanthwe? Kodi wina amatipula ndi ngʼombe mʼnyanja? Koma chiweruzo cholungama mwachisandutsa kukhala zinthu zakupha ndipo chipatso cha chilungamo mwachisandutsa kukhala chowawa.
13 Och förtrösten eder uppå det som platt intet är, och sägen: Äro vi icke mägtige och starke nog?
Inu amene mukunyadira kuti munagonjetsa Lo Debara ndipo mukunena kuti, “Kodi sitinatenge Karinaimu ndi mphamvu zathu zokha?”
14 Derföre, si, jag skall uppväcka ett folk öfver eder af Israels hus, säger Herren Gud Zebaoth; det skall tränga eder ifrå det rummet, der man går till Hamath, intill pilträbäcken.
Koma Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akulengeza kuti, “Inu nyumba ya Israeli, ndidzakudzutsirani mtundu wina wa anthu umene udzakuzunzani kuchokera ku Lebo Hamati mpaka ku Chigwa cha Araba.”