< Amos 5 >

1 Hörer, I af Israels hus, detta ordet: ty jag måste göra denna klagovisona öfver eder.
Israeli, imva mawu awa, nyimbo ya maliro imene ndikuyimba za iweyo:
2 Jungfrun Israel är fallen, så att hon intet mer uppstå kan; hon är stött neder till jordena, och ingen är som upphjelper henne.
“Namwali Israeli wagwa, moti sadzadzukanso, wasiyidwa mʼdziko lake lomwe, popanda woti ndi kumudzutsa.”
3 Ty så säger Herren Herren: Den staden, der tusende utgå, der skola icke utan hundrade qvar blifva i och der hundrade utgå, skola icke utan tio igen behållne blifva i Israels bus.
Ambuye Yehova akuti, “Mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 1,000 amphamvu udzatsala ndi anthu 100 okha; mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 100 amphamvu udzatsala ndi anthu khumi okha basi.”
4 Derföre, så säger Herren till Israels hus: Söker mig, så skolen I lefva.
Zimene Yehova akunena kwa nyumba ya Israeli ndi izi: “Mundifunefune kuti mukhale ndi moyo;
5 Söker icke BethEl, och kommer intet till Gilgal, och går icke till BerSeba; förty Gilgal, skall varda fånget bortfördt, och BethEl skall i jämmer komma.
musafunefune Beteli, musapite ku Giligala, musapite ku Beeriseba. Pakuti Giligala adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, ndipo Beteli adzawonongekeratu.”
6 Söker Herran, så skolen I lefva, på det i Josephs huse icke uppågå skall en eld, hvilken förtärer, och icke utsläckas kan uti BethEl.
Funani Yehova kuti mukhale ndi moyo, mukapanda kutero Iye adzatentha nyumba ya Yosefe ngati moto; motowo udzawononga, ndipo sipadzakhala wina wozimitsa motowo ku Beteli.
7 I som förvänden rätten uti malört, och stöten rättvisona neder till jordena;
Inu amene mumasandutsa chiweruzo cholungama kukhala chowawa ndi kunyoza chilungamo.
8 Han gör sjustjernorna och Orion han gör af mörkret morgonen, och af dagen mörka nattena; han kallar vattnet i hafvena, och gjuter det uppå jordenes krets; han heter Herren;
(Iye amene analenga nyenyezi za Nsangwe ndi Akamwiniatsatana, amene amasandutsa mdima kuti ukhale mmawa ndi kudetsa usana kuti ukhale usiku, amene amayitana madzi a mʼnyanja ndi kuwathira pa dziko lapansi, Yehova ndiye dzina lake.
9 Den der en förstöring beställer öfver den starka, och låter komma en förstöring öfver den fasta staden.
Iyeyo amabweretsa chiwonongeko modzidzimutsa pa anthu amphamvu ndi kuwononga mizinda yotetezedwa),
10 Men de äro honom gramse, som dem uppenbara straffar, och hafva en styggelse vid den som helsosamt lärer.
inu mumadana ndi amene amadzudzula mʼbwalo la milandu ndi kunyoza amene amanena zoona.
11 Derföre, efter I undertrycken den fattiga, och tagen korn af honom i storom bördom, så skolen I icke bo uti husomen, som I af huggen sten uppbyggt hafven, och icke dricka det vin, som I uti de sköna vingårdar planterat hafven.
Mumapondereza munthu wosauka ndi kumukakamiza kuti akupatseni tirigu. Nʼchifukwa chake, ngakhale mwamanga nyumba zamiyala yosema, inuyo simudzakhalamo. Ngakhale mwalima minda yabwino ya mphesa, inu simudzamwa vinyo wake.
12 Ty jag vet edor öfverträdelse, den mycken är, och edra synder, de der starka äro; huru I trängen de rättfärdiga, och tagen gåfvor, och undertrycken de fattiga i domenom.
Pakuti Ine ndikudziwa kuchuluka kwa zolakwa zanu ndi kukula kwa machimo anu. Inu mumapondereza anthu olungama ndi kulandira ziphuphu ndipo anthu osauka simuwaweruza mwachilungamo mʼmabwalo anu amilandu.
13 Derföre måste den kloke tiga på den tiden; ty det är en ond tid.
Nʼchifukwa chake pa nthawi yotere munthu wanzeru sayankhulapo kanthu, popeza ndi nthawi yoyipa.
14 Söker det goda, och icke det onda, på det I lefva mågen; så skall Herren Gud Zebaoth vara med eder, såsom I berömmen.
Muyike mtima wanu pa zabwino osati pa zoyipa, kuti mukhale ndi moyo. Mukatero Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzakhala nanu, monga mmene mumanenera kuti ali nanu.
15 Hater det onda, och älsker det goda; skaffer rätt i portenom; så skall Herren Gud Zebaoth vara nådelig öfver de igenlefda i Joseph.
Mudane ndi zoyipa, mukonde zabwino; mukhazikitse chiweruzo cholungama mʼmabwalo anu amilandu. Mwina mwake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzachitira chifundo anthu otsala a mʼbanja la Yosefe.
16 Derföre, så säger Herren Gud Zebaoth, Herren: Det skall varda klagogråt på alla gator, och på alla vägar skall man säga: Ack ve, ack ve! Och man skall kalla åkermannen till sorg, och till klagogråt den der gråta kan.
Choncho izi ndi zimene Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, akunena: “Mʼmisewu monse mudzakhala kulira mofuwula, ndi kulira chifukwa cha kuwawa kwa masautso kudzakhala paliponse. Adzayitana alimi kuti adzalire, ndipo anthu odziwa maliridwe anthetemya adzalira mofuwula.
17 Uti alla, vingårdar skall klagogråt vara; ty jag vill fara fram ibland eder, säger Herren.
Mʼminda yonse ya mpesa mudzakhala kulira kokhakokha, pakuti Ine ndidzadutsa pakati panu,” akutero Yehova.
18 Ve dem som begära Herrans dag! Hvad skall han eder? Ty Herrans dag är ett mörker, och icke ljus;
Tsoka kwa inu amene mumalakalaka tsiku la Yehova! Chifukwa chiyani mumalakalaka tsiku la Yehova? Tsikulo kudzakhala mdima osati kuwala.
19 Lika som då någor flydde för ett lejon, och honom mötte en björn; och lika som någor in uti ett hus komme, och ledde sig med handene utmed väggene, och en orm stunge honom.
Lidzakhala ngati tsiku limene munthu pothawa mkango amakumana ndi chimbalangondo, ngati pamene munthu walowa mʼnyumba, natsamira dzanja lake pa khoma ndipo njoka nʼkuluma.
20 Ty Herrans dag skall ju vara mörk, och icke ljus; skum, och icke klar?
Kodi tsiku la Yehova silidzakhala mdima osati kuwala, mdima wandiweyani, popanda powala pena paliponse?
21 Jag är edrom högtidom gramse, och föraktar dem, och kan icke lida edart rökoffer uti edra församlingar.
“Ndimadana nawo masiku anu achikondwerero ndipo ndimawanyoza; sindikondwera nayo misonkhano yanu.
22 Och om I mig än offraden bränneoffer och spisoffer, så hafver jag dock ingen lust dertill; så orkar jag ock icke se edart feta tackoffer.
Ngakhale mupereke nsembe zopsereza ndi nsembe zachakudya, Ine sindidzazilandira. Ngakhale mupereke nsembe zabwino zachiyanjano, Ine sindidzaziyangʼana nʼkomwe.
23 Haf bort dina visors buller ifrå mig; ty jag orkar icke höra ditt psaltarespel.
Musandisokose nazo nyimbo zanu! Sindidzamvetsera kulira kwa azeze anu.
24 Men rätten skall uppenbarad varda lika som vatten, och rättvisan såsom en stark flod.
Koma chiweruzo cholungama chiyende ngati madzi, chilungamo ngati mtsinje wosaphwa!
25 Hafven I, af Israels hus, ock offrat mig slagtoffer och spisoffer i öknene, i fyratio år långt? Ja, skönliga.
“Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?
26 I bären edars Molochs hyddor, och edra afgudars beläte, och edra gudars stjerno, som eder sjelfve gjort haden.
Inu mwanyamula kachisi wa mfumu yanu, ndi nyenyezi ija Kaiwani, mulungu wanu, mafano amene munadzipangira.
27 Så skall jag låta föra eder hädan bort till Damascus, säger Herren, som Gud Zebaoth heter.
Nʼchifukwa chake Ine ndidzakupititsani ku ukapolo, kutali kupitirira ku Damasiko,” akutero Yehova, amene dzina lake ndi Mulungu Wamphamvuzonse.

< Amos 5 >