< Amos 3 >

1 Hörer hvad Herren med eder talar, I Israels barn, nämliga med alla de slägter, som jag utur Egypti land fört hafver, och sade:
Inu Aisraeli, imvani mawu awa amene Yehova wayankhula kutsutsana nanu, kutsutsana ndi banja lonse limene analitulutsa mu Igupto:
2 Utaf alla slägter på jordene hafver jag upptagit eder allena; derföre vill jag ock hemsöka eder uti alla edra missgerningar.
“Inu nokha ndi amene ndinakusankhani pakati pa mabanja onse a dziko lapansi; nʼchifukwa chake ndidzakulangani chifukwa cha machimo anu onse.”
3 Kunna ock två vandra tillhopa, utan de draga öfverens med hvarannan?
Kodi anthu awiri nʼkuyendera limodzi asanapangane?
4 Ryter ock ett lejon i skogenom, utan det hafver rof? Ropar ock ett ungt lejon utu sine kulo, utan det något fångit hafver?
Kodi mkango umabangula mʼnkhalango usanagwire nyama? Kodi msona wamkango umalira mʼphanga mwake pamene sunagwire kanthu?
5 Kommer ock någor fogel i snarona på jordene, der ingen foglafångare är? Tager man ock snarona upp af jordene, den ännu intet fångit hafver?
Kodi mbalame nʼkutera pa msampha pamene palibe nyambo yake? Kodi msampha umafwamphuka usanakole kanthu?
6 Blås man ock i basun i enom stad, och folket deraf icke förskräckes? Är ock något ondt i stadenom, det Herren icke gör?
Kodi pamene lipenga la nkhondo lalira mu mzinda, anthu sanjenjemera? Pamene tsoka lafika mu mzinda, kodi si Yehova amene wachititsa zimenezo?
7 Ty Herren Herren gör intet, utan han uppenbarar sinom tjenarom, Prophetomen, sina hemlighet.
Zoonadi Ambuye Yehova sachita kanthu asanawulule zimene akufuna kuchita kwa atumiki ake, aneneri.
8 Lejonet ryter, ho skulle icke frukta sig? Herren Herren talar, ho skulle icke prophetera?
Mkango wabangula, ndani amene sachita mantha? Ambuye Yehova wayankhula, ndani amene sanganenere?
9 Förkunner uti palatsen i Asdod, och uti palatsen i Egypti land, och säger: Församler eder på Samarie berg, och ser till, hvilket stort mordskri och orätt der är.
Lengezani zimenezi ku nyumba zaufumu za ku Asidodi ndiponso ku nyumba zaufumu za ku Igupto: “Sonkhanani ku mapiri a ku Samariya; onani chisokonezo pakati pake ndiponso kuponderezana pakati pa anthu ake.”
10 De passa intet på någon rätt, säger Herren; utan öfvervåld och skada går hvart om annat i deras husom.
“Iwo sadziwa kuchita zolungama, ndipo amadzaza malo awo otetezedwa ndi zinthu zolanda ku nkhondo ndi zakuba,” akutero Yehova.
11 Derföre säger Herren Herren alltså: Man skall belägga detta landet allt omkring, och störta dig neder ifrå dine magt, och skinna din hus.
Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akunena izi: “Mdani adzalizungulira dzikoli; iye adzagwetsa malinga ako, ndi kufunkha nyumba zako zaufumu.”
12 Detta säger Herren: Lika som en herde rycker eno lejone två fötter, eller ett stycke af ett öra utu munnenom; alltså skola Israels barn utryckte varda, de som bo i Samarien, och hafva i hörnet ett lägre, och i Damasco ena säng.
Yehova akuti, “Monga mʼbusa amalanditsa mʼkamwa mwa mkango miyendo iwiri yokha kapena msonga yokha ya khutu, moteronso ndimo mmene adzapulumukire Aisraeli amene amakhala mu Samariya pa msonga za mabedi awo, ndi ku Damasiko pa akakhutagona awo.”
13 Hörer, och betyger i Jacobs hus, säger Herren, Herren Gud Zebaoth.
“Imvani izi ndipo mupereke umboni wotsutsa nyumba ya Yakobo,” akutero Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
14 Ty på den tiden, då jag Israels synder hemsökandes varder, vill jag hemsöka de altare i BethEl, och bortbryta hornen af altaret, att de skola falla neder på markena;
“Pa tsiku limene ndidzalange Israeli chifukwa cha machimo ake, ndidzagumula maguwa ansembe a ku Beteli; nyanga za guwa zidzathyoka ndipo zidzagwa pansi.
15 Och skall slå både vinterhus och sommarhus; och de elphenbenshus skola till intet varda, och mång hus förderfvad blifva, säger Herren.
Ndidzagwetsa nyumba ya pa nthawi yozizira pamodzi ndi nyumba ya pa nthawi yotentha; nyumba zokongoletsedwa ndi minyanga ya njovu zidzawonongedwa ndipo nyumba zikuluzikulu zidzaphwasulidwa,” akutero Yehova.

< Amos 3 >