< Amos 2 >

1 Detta säger Herren: För tre och fyra Moabs lasters skull, vill jag intet skona honom; derföre, att de hafva uppbränt Konungens ben i Edom till asko;
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Mowabu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu, mpaka kuwasandutsa phulusa,
2 Utan jag vill sända en eld i Moab; han skall förtära palatsen i Kerioth, och Moab skall dö uti buller, rop och basunsklang.
Ine ndidzatumiza moto pa Mowabu, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Keriyoti. Mowabu adzafera pakati pa nkhondo yoopsa, mʼkati mwa mfuwu wa nkhondo ndi kuliza malipenga.
3 Och jag skall borttaga domaren ifrå honom, och dräpa alla hans Förstar med honom, säger Herren.
Ndidzawononga wolamulira wake ndi kupha akuluakulu onse amene ali pamodzi ndi iye,” akutero Yehova.
4 Detta säger Herren: För tre och fyra Juda lasters skull, vill jag intet skona honom; derföre, att de förakta Herrans lag, och icke hålla hans rätter, och låta sina lögn förföra sig, hvilka deras fäder efterföljt hafva,
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Yuda akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo akana lamulo la Yehova ndipo sanasunge malangizo ake, popeza asocheretsedwa ndi milungu yabodza, milungu imene makolo awo ankayitsatira,
5 Utan jag vill sända en eld i Juda han skall förtära palatsen i Jerusalem.
Ine ndidzatumiza moto pa Yuda, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu.”
6 Detta säger Herren: För tre och fyra Israels lasters skull, vill jag intet skona honom; derföre, att de sälja de rättfärdiga för penningar, och de fattiga för ett par skor.
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Israeli akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Iwo amagulitsa anthu olungama ndi siliva, ndi osauka ndi nsapato.
7 De gå med fötterna öfver de fattiga, och hindra de elända allestäds; sonen och fadren sofva när ena qvinno, med hvilko de ohelga mitt Namn.
Amapondereza anthu osauka ngati akuponda fumbi, ndipo sawaweruza mwachilungamo anthu oponderezedwa. Abambo ndi mwana wawo amagonana ndi mtsikana mmodzi yemweyo, ndipo potero amanyozetsa dzina langa loyera.
8 Och vid all altare slösa de af förpantad kläder, och dricka vin i sins Guds huse af saköre.
Anthuwo amakagonana mʼmbali mwa guwa lililonse la nsembe pa zovala zimene anatenga ngati chikole. Mʼnyumba ya mulungu wawo amamweramo vinyo amene analipiritsa anthu pa milandu.
9 Nu hafver jag dock förlagt Amoreen för dem, den så hög var som cedreträ, och hans magt såsom eker; och jag förderfvade hans frukt ofvantill, och bans rötter nedantill.
“Ine ndinawononga Aamori pamaso pawo, ngakhale iwo anali anthu ataliatali ngati mikungudza ndiponso amphamvu ngati mitengo ya thundu. Ndinawononga zipatso zawo ndiponso mizu yawo.
10 Hafver jag ock fört eder utur Egypti land, och ledt eder uti öknene i fyratio år, att I de Amoreers land besitta skullen?
“Ine ndinakutulutsani ku Igupto, ndipo ndinakutsogolerani mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kudzakupatsani dziko la Aamori.
11 Och af edrom barnom uppväckt eder Propheter, och af edrom ynglingom Nazareer? Är det icke så, I Israels barn? säger Herren.
Ine ndinawutsanso ena mwa ana ako kuti akhale aneneri, ndi ena mwa anyamata ako kuti akhale anaziri. Kodi si choncho, inu Aisraeli?” akutero Yehova.
12 Så gåfven I de Nazareer dricka vin, och Prophetomen böden I, och saden: I skolen intet prophetera.
“Koma inu munawamwetsa vinyo anaziri aja, ndipo munalamula aneneri kuti asanenere.
13 Si, jag vill göra ibland eder ett gnisslande, såsom en vagn full af kärfvar gnisslar;
“Tsono Ine ndidzakupsinjani monga imapsinjikira ngolo imene yadzaza ndi tirigu.
14 Att den der rask är, skall icke kunna undfly, ej heller den starke något förmå, och den mägtige skall icke kunna undsätta sitt lif;
Munthu waliwiro sadzatha kuthawa, munthu wamphamvu sadzakhalanso ndi nyonga, wankhondo sadzapulumutsa moyo wake.
15 Och de bågaskyttar skola icke bestå; och den der rask är till att löpa, skall icke undlöpa; och den der rider, skall icke rädda sitt lit;
Munthu wa uta sadzalimbika, msilikali wothamanga kwambiri sadzapulumuka, ndipo wokwera pa akavalo sadzapulumutsa moyo wake.
16 Och den der aldramanligast är ibland de starka, måste i den tiden nakot undfly, säger Herren.
Ngakhale asilikali olimba mtima kwambiri adzathawa ali maliseche pa tsikulo,” akutero Yehova.

< Amos 2 >