< 2 Samuelsboken 1 >

1 Efter Sauls död, då David igenkommen var ifrå de Amalekiters slagtning, och hade blifvit två dagar i Ziklag,
Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri.
2 Si, på tredje dagen kom en man ifrå Sauls här, med sönderrifven kläder, och jord på hans hufvud. Och som han kom till David, föll han ned på jordena, och tillbad.
Pa tsiku lachitatu munthu wina wochokera ku msasa wa Sauli anafika, zovala zake zitangʼambika ndiponso anali atathira dothi pamutu pake. Atafika kwa Davide, anadzigwetsa pansi, kupereka ulemu kwa Davideyo.
3 Men David sade till honom: Hvadan kommer du? Han sade till honom: Ifrån Israels här hafver jag flytt.
Davide anamufunsa iye kuti, “Kodi iwe wachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndathawa ku misasa ya Aisraeli.”
4 David sade till honom: Säg mig, huru tillgånget är. Han sade: Folket är flydt af stridene, och mycket folk är fallet; dertill är ock Saul död, och hans son Jonathan.
Davide anafunsa, “Tandiwuza, chachitika ndi chiyani?” Iye anati, “Anthu athawa ku nkhondo ndipo ambiri aphedwa. Sauli ndi mwana wake Yonatani aphedwa.”
5 David sade till den ynglingen, som detta bådade: Hvaraf vetst du, att Saul och hans son Jonathan äro döde?
Ndipo Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa nkhaniyi, “Ukudziwa bwanji kuti Sauli ndi mwana wake Yonatani afa?”
6 Ynglingen, som detta bådade, sade: Jag kom oförvarandes upp på Gilboa berg; och si, Saul böjde sig neder på sitt spjut, och vagnar och resenärer jagade efter honom.
Mnyamatayo anati, “Zinangochitika kuti ndinali pa phiri la Gilibowa, ndipo Sauli anali komweko ataweramira pa mkondo wake, pamodzi ndi magaleta ndi okwera ake atamuyandikira.
7 Och han vände sig om, och fick se mig, och kallade mig, och jag sade: Här är jag.
Pamene anatembenuka ndi kundiona ine, iye anandiyitana, ndipo ndinati, ‘Kodi ndichite chiyani?’”
8 Och han talade till mig: Ho äst du? Jag sade till honom: Jag är en Amalekit.
Iye anandifunsa, “Iwe ndiwe yani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndine Mwamaleki.”
9 Och han sade till mig: Kom hit till mig, och dräp mig; ty ångest hafver begripit mig; ty mitt lif är ännu allt helt i mig.
“Kenaka iye anati kwa ine, ‘Bwera pafupi ndipo undiphe! Ndikumva ululu kwambiri, koma ndikanali ndi moyo!’
10 Så gick jag till honom, och drap honom; förty jag visste väl, att han icke skulle kunna lefva efter hans fall; och jag tog kronona af hans hufvud, och armsmidet af hans arm, och hafver burit det hit till dig, min herra.
“Kotero ndinabwera pafupi ndi kumupha, chifukwa ndinadziwa kuti mmene anagweramo sakanakhalanso ndi moyo. Ndipo ndatenga chipewa chaufumu chimene chinali pamutu pake ndi khoza la pa dzanja lake ndipo ndazibweretsa kwa inu mbuye wanga.”
11 Då fattade David sin kläder, och ref dem sönder, och alle de män, som när honom voro;
Apo Davide ndi anthu onse amene anali nawo anangʼamba zovala zawo.
12 Och jämrade sig, och greto, och fastade allt intill aftonen öfver Saul och Jonathan hans son; och öfver Herrans folk, och öfver Israels hus, att de genom svärd fallne voro.
Iwo analira maliro ndi kusala zakudya mpaka madzulo chifukwa cha Sauli ndi mwana wake Yonatani, komanso chifukwa cha gulu la ankhondo la Yehova ndi nyumba ya Israeli, chifukwa anaphedwa ndi lupanga.
13 Och David sade till ynglingen, som honom det bådat hade: Hvadan äst du? Han sade: Jag är en främling, en Amalekits son.
Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa uthengawo, “Iwe umachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mwana wa mlendo Mwamaleki.”
14 David sade till honom: Hvi hafver du icke fruktat dig komma dina hand vid Herrans smorda, till att dräpa honom?
Davide anamufunsanso kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunaope kukweza dzanja lako ndi kupha wodzozedwa wa Yehova?”
15 Och David sade till en af sina unga män: Fram, och slå honom. Och han slog honom, att han blef död.
Kenaka Davide anayitana mmodzi mwa anyamata ake ndipo anati, “Pita ukamukanthe!” Kotero iye anapita kukamukantha, ndipo mnyamata uja anafa.
16 Då sade David till honom: Ditt blod vare öfver ditt hufvud; ty din mun hafver talat emot dig sjelf, och sagt: Jag hafver dräpit Herrans smorda.
Pakuti Davide anali atanena kwa iye kuti, “Iwe wadzipha wekha. Pakamwa pako pakunena zokutsutsa wekha, pamene unanena kuti, ‘Ine ndapha wodzozedwa wa Yehova.’”
17 Och David klagade denna klagan öfver Saul och Jonathan hans son;
Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani.
18 Och befallde, att man skulle lära Juda barn bågan: Si, det är skrifvet uti den redeligas bok:
Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:
19 De ädlaste i Israel äro slagne på din berg; huru äro de hjeltar fallne!
“Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda. Taonani amphamvu agwa kumeneko!
20 Bebåder det icke i Gath, förkunner det icke på gatomen i Askelon; på det att de Philisteers döttrar sig icke fröjda skola, att de oomskornas döttrar icke glädjas skola.
“Musakanene zimenezi ku Gati, musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni, kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale, ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.
21 I Gilboa berg, komme på eder hvarken dagg eller regn, icke heller vare åkrar, der häfoffer af kommer; förty der är de hjeltars sköld afslagen, Sauls sköld, likasom han icke hade varit smord med oljo.
“Inu mapiri a ku Gilibowa, musakhalenso ndi mame kapena mvula, kapena minda yobereka zopereka za ufa. Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa, chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.
22 Jonathans båge felade icke, och Sauls svärd kom aldrig fåfängt igen ifrå de slagnas blod, och ifrå de hjeltars fetma.
“Pa magazi a ophedwa, pa mnofu wa amphamvu, uta wa Yonatani sunabwerere, lupanga la Sauli silinabwere chabe.
23 Saul och Jonathan, ljuflige och täcke medan de lefde, äro också icke åtskiljde i döden; raskare än örnar, och starkare än lejon.
“Sauli ndi Yonatani, pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima, ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe. Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga, anali ndi mphamvu zoposa mkango.
24 I Israels döttrar, gråter öfver Saul, den eder klädde med rosenfärgo i kräselighet, och prydde eder med gyldene klenodier på edor kläder.
“Inu ana aakazi a Israeli, mulireni Sauli, amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa, amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.
25 Huru äro de hjeltar så fallne i stridene; Jonathan är slagen på dina högar.
“Taonani amphamvu agwa ku nkhondo! Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.
26 Jag sörjer om dig, min broder Jonathan; du hafver varit mig mycket kär; din kärlek var mig närmare än qvinnokärlek.
Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani, unali wokondedwa kwambiri kwa ine. Chikondi chako pa ine chinali chopambana, chopambana kuposa chikondi cha akazi.
27 Huru äro de hjeltar fallne, och vapnen borto blefne!
“Taonani amphamvu agwa! Zida zankhondo zawonongeka!”

< 2 Samuelsboken 1 >